Numeri 23 – CCL & CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 23:1-30

Uthenga Woyamba wa Balaamu

1Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.” 2Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.

3Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.

4Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”

5Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”

6Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu. 7Ndipo Balaamu ananena uthenga wake:

“Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu,

mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa.

Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga,

pita nyoza Israeli.’

8Ndingatemberere bwanji

amene Mulungu sanawatemberere?

Ndinganyoze bwanji

amene Yehova sanawanyoze?

9Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu,

ndikuwaona kuchokera pa zitunda.

Ndikuona anthu okhala pawokha,

osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.

10Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi,

kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli?

Lekeni ndife imfa ya oyera mtima,

ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”

11Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”

12Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”

Uthenga Wachiwiri wa Balaamu

13Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.” 14Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.

15Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”

16Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”

17Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”

18Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake:

“Nyamuka Balaki ndipo tamvera;

Undimvere iwe mwana wa Zipori.

19Mulungu si munthu kuti aname,

kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake.

Kodi amayankhula koma osachita?

Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?

20Wandilamula kuti ndidalitse,

Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.

21“Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo,

sanaone chovuta mu Israeli.

Yehova Mulungu wawo ali nawo:

mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.

22Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto,

ali ndi mphamvu ngati za njati.

23Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo,

palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli.

Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti,

‘Onani zimene Mulungu wachita!’

24Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi;

adzuka okha ngati mkango waumuna

umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira

ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”

25Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!

26“Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’ ”

Uthenga Wachitatu wa Balaamu

27Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.” 28Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.

29Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.” 30Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 23:1-30

Uthenga Woyamba wa Balaamu

1Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.” 2Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.

3Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.

4Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”

5Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”

6Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu. 7Ndipo Balaamu ananena uthenga wake:

“Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu,

mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa.

Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga,

pita nyoza Israeli.’

8Ndingatemberere bwanji

amene Mulungu sanawatemberere?

Ndinganyoze bwanji

amene Yehova sanawanyoze?

9Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu,

ndikuwaona kuchokera pa zitunda.

Ndikuona anthu okhala pawokha,

osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.

10Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi,

kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli?

Lekeni ndife imfa ya oyera mtima,

ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”

11Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”

12Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”

Uthenga Wachiwiri wa Balaamu

13Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.” 14Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.

15Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”

16Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”

17Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”

18Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake:

“Nyamuka Balaki ndipo tamvera;

Undimvere iwe mwana wa Zipori.

19Mulungu si munthu kuti aname,

kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake.

Kodi amayankhula koma osachita?

Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?

20Wandilamula kuti ndidalitse,

Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.

21“Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo,

sanaone chovuta mu Israeli.

Yehova Mulungu wawo ali nawo:

mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.

22Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto,

ali ndi mphamvu ngati za njati.

23Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo,

palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli.

Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti,

‘Onani zimene Mulungu wachita!’

24Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi;

adzuka okha ngati mkango waumuna

umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira

ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”

25Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!

26“Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’ ”

Uthenga Wachitatu wa Balaamu

27Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.” 28Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.

29Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.” 30Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.