Numeri 21 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 21:1-35

Kuwonongedwa kwa Aradi

1Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo. 2Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.” 3Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.

Njoka Yamkuwa

4Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo 5ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”

6Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa. 7Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.

8Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.” 9Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.

Ulendo wa ku Mowabu

10Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti. 11Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa. 12Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi. 13Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori. 14Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati,

“Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa,

mu zigwa za Arinoni, 15ku matsitso a zigwa

amene afika mpaka ku Ari

nakhudza malire a dziko la Mowabu.”

16Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”

17Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi:

“Tulutsa madzi, chitsime iwe!

Chiyimbireni nyimbo,

18chitsime chomwe anakumba mafumu,

chomwe anakumba anthu omveka,

ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.”

Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana. 19Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti, 20ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.

Kugonjetsedwa kwa Sihoni ndi Ogi

21Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,

22“Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”

23Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli. 24Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa. 25Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira. 26Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.

27Nʼchifukwa chake alakatuli amati:

“Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso;

mzinda wa Sihoni ukhazikike.

28“Moto unabuka ku Hesiboni,

malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni.

Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu,

nzika za ku malo okwera a Arinoni.

29Tsoka kwa iwe Mowabu!

Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi!

Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa

ndipo ana ake aakazi ngati akapolo,

akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.

30“Koma ife tawagonjetsa;

Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni.

Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa,

mzinda womwe umafika ku Medeba.

31“Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”

32Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko. 33Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.

34Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”

35Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.

Bibelen på hverdagsdansk

4. Mosebog 21:1-35

Moses laver en kobberslange

1Da kongen af Arad i Negev hørte, at israelitterne kom op ad vejen mod Atarim, samlede han sin hær og angreb dem, og det lykkedes ham at tage en del af dem til fange. 2Da lovede Israels folk højt og helligt Herren, at hvis han ville hjælpe dem med at besejre kongen af Arad og hans hær, ville de totalt udslette alle de kana’anæiske byer i området uden at tage noget bytte til sig selv. 3Herren hørte deres bøn og gav dem sejr over kana’anæerne, så alle byerne og deres indbyggere blev udslettet. Stedet er siden kendt under navnet Horma.21,3 Det hebraiske ord betyder „udslettelse” og henviser til noget, som er overgivet til Herrens dom.

4Derfra vendte israelitterne tilbage til Hors bjerg, hvorefter de fortsatte ad vejen mod Det Røde Hav i en bue uden om Edom. Men undervejs blev de utålmodige, 5og de begyndte atter at kritisere både Gud og Moses. „Hvorfor førte du os ud af Egypten?” klagede de. „Var det for at lade os dø her i ørkenen? Her er jo hverken vand eller mad—og vi er trætte af den evindelige manna.”

6Da sendte Herren giftslanger imod dem, og mange blev bidt og døde.

7Nu kom folket til Moses og sagde: „Vi har syndet ved at gøre oprør mod dig og Herren. Bed Herren om at fjerne slangerne fra os.” Da gik Moses i forbøn for folket, 8og Herren sagde Moses: „Lav en slange af kobber21,8 Eller: „bronze”. Hebraisk brugte det samme ord for kobber og bronze. og hæng den op på en stang—så skal alle, som ser hen på den, leve, selvom de er blevet bidt af giftslangerne.”

9Så lavede Moses en kobberslange og satte den op på en stang. Og alle, som så hen på den, når de var blevet bidt af en slange, reddede livet.

Rejsen fortsætter uden om Edom gennem Moab

10Derefter rejste Israels folk videre og slog lejr ved Obot. 11Fra Obot tog de til Ijje-ha-Abarim i ørkenen umiddelbart øst for Moab, 12og videre til Zereddalen, hvor de igen slog lejr. 13Fra Zereddalen rejste de videre mod nord til det øde område på den anden side af Arnonfloden ved grænsen til amoritternes land. Arnonfloden danner grænse mellem moabitterne og amoritterne. 14„Bogen om Herrens krige” nævner byen Vaheb med dens bække i Sufaområdet i Arnonflodens kløft, 15som strækker sig langs grænsen til Moab helt til byen Ar.

16Derfra rejste israelitterne til Be’er.21,16 Det betyder: „brønd”. Det var ved dette vandsted, at Herren sagde til Moses: „Kald folket sammen, så vil jeg give dem vand.” 17-18Episoden står beskrevet i følgende sang:

„Du ældgamle brønd, hvor kilden fremsprang,

vi viser vor glæde ved at synge en sang.

Denne brønd lod stormænd grave,

fyrster med scepter og herskerstave.”

Så forlod de ørkenen og fortsatte gennem Mattana, 19Nahaliel og Bamot 20og videre gennem dalen i Moabs højland, hvorfra man kan se ørkenen og Pisgas bjergtinder længere borte.

Israelitterne besejrer kong Sihon og Kong Og

21Da sendte Israel følgende budskab til amoritterkongen Sihon: 22„Giv os tilladelse til at rejse igennem dit land. Vi lover, at vi ikke vil nedtrampe jeres marker og vingårde eller drikke jeres vand, men holde os på Kongevejen, så længe vi er i jeres land.”

23Men kong Sihon gav dem ikke lov. I stedet samlede han sin hær og rykkede ud mod israelitterne i ørkenen. Ved Jahatz mødtes de to hære, 24og Israel huggede amoritterne ned. Derefter besatte de området fra Arnonfloden i syd til Jabbokfloden mod nord og ud til ammonitternes område mod øst, men ikke længere, for ammonitternes grænse var stærkt befæstet.

25-26Israelitterne indtog således amoritternes byer, og de slog sig ned i disse byer, også i Heshbon, kong Sihons residensby, og i området op til Arnonfloden, der tidligere havde tilhørt moabitterne, men som kong Sihon havde erobret. 27-30Den gamle digter udtrykker det sådan:

„Kom til Heshbon, Sihons by

som nu bygges op på ny.

Ild fór ud fra Heshbon,

flammer skød frem fra Sihon.

Moabs byer gik op i røg,

Arnons fjelde, hver en høj.

Moabitter, nu er det forbi

med jeres Kemosh-afguderi.

Han sendte jo jer alle på flugt,

kvinder blev fanger—åh, hvor smukt!

Men vi erobred’ Heshbon,

indtog landet op til Dibon.

Vi dræbte dem helt til Nofa

som ligger tæt ved Medeba.”

31-32Mens Israels folk opholdt sig i amoritternes land, sendte Moses nogle spioner ud for at undersøge, hvordan han lettest kunne indtage byen Jazer. Derefter angreb de byen og de omkringliggende landsbyer, og amoritterne måtte flygte.

33Derefter satte de kursen nordpå mod Bashan, hvor kong Og straks mobiliserede sin hær og rykkede ud mod dem ved byen Edrei. 34Men Herren sagde til Moses: „Du skal ikke være bange. Jeg vil udlevere kongen og hans hær og hans land til dig. Du skal gøre med ham, som du gjorde med amoritternes kong Sihon af Heshbon.” 35Og ganske rigtigt: Israelitterne sejrede og dræbte kong Og, hans sønner og hans hær, så der ikke var en eneste overlevende tilbage. Således lykkedes det israelitterne at erobre hele området.