Numeri 16 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 16:1-50

Kora, Datani ndi Abiramu Awukira Mose

1Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza, 2ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano. 3Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”

4Mose atamva izi, anagwa chafufumimba. 5Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi. 6Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira 7ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”

8Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani! 9Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira? 10Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe. 11Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”

12Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera! 13Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa? 14Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”

15Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”

16Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni. 17Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.” 18Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano. 19Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo. 20Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti, 21“Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”

22Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”

23Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, 24“Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’ ”

25Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira. 26Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.” 27Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.

28Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga. 29Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume. 30Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.”

31Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana 32ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense. 33Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. 34Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”

35Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.

36Yehova anawuza Mose kuti, 37“Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika. 38Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”

39Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, 40monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.

41Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”

42Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera. 43Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija 44ndipo Yehova anawuza Mose kuti, 45“Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.

46Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.” 47Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo. 48Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka. 49Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora. 50Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.

Священное Писание

Числа 16:1-50

Корах, Датан и Авирам восстают против Мусы

1Корах, сын Ицхара, внук Каафа, правнук Леви, и рувимиты – Датан и Авирам, сыновья Элиава, и Авнан, сын Пелета, составили заговор 2и восстали против Мусы. С ними были двести пятьдесят исраильтян, вождей народа, прославленной среди народа знати. 3Они собрались против Мусы и Харуна и сказали им:

– Вы зашли слишком далеко! Все в народе святы, каждый из них, и Вечный пребывает с ними. Почему же вы ставите себя выше всего народа Вечного?

4Услышав это, Муса пал лицом на землю. 5Он сказал Кораху и его сообщникам:

– Завтра утром Вечный покажет, кто принадлежит Ему, кто свят и кому будет дано приближаться к Нему. Кого Он изберёт, тому и будет дано приближаться к Нему. 6Ты, Корах, и твои сообщники сделайте вот что: возьмите сосуды для возжигания благовоний 7и завтра положите в них горящие угли, а на них положите перед Вечным благовония. Кого Вечный изберёт, тот и будет свят. Вы, левиты, зашли слишком далеко!

8Муса сказал Кораху:

– Послушайте, левиты! 9Разве не достаточно вам того, что Бог Исраила отделил вас от народа Исраила и приблизил к Себе, чтобы вы работали при священном шатре Вечного, стояли перед обществом и служили ему? 10Он приблизил к Себе вас и ваших собратьев левитов, но вы пытаетесь получить и священство. 11Вы и ваши сообщники ополчились против Вечного. Ведь кто такой Харун, чтобы вам роптать на него?

12Муса призвал Датана и Авирама, сыновей Элиава. Но они сказали:

– Мы не придём! 13Разве не достаточно, что ты вывел нас из земли, где течёт молоко и мёд, чтобы убить в пустыне? А теперь ты хочешь ещё и властвовать над нами? 14Ты не привёл нас в землю, где течёт молоко и мёд, и не дал нам поля и виноградники. Хочешь запорошить этим людям глаза? Мы не придём!

15Муса сильно разгневался и сказал Вечному:

– Не принимай их приношений. Я не брал у них даже осла и никому из них не причинил зла.

16Муса сказал Кораху:

– Что до тебя с твоими сообщниками, предстаньте завтра перед Вечным: ты, они и Харун. 17Пусть каждый возьмёт свой сосуд, положит в него благовония и принесёт его Вечному – всего двести пятьдесят сосудов. Ты и Харун тоже принесите каждый свой сосуд.

18Каждый взял сосуд, положил в него горящие угли, а на них – благовония, и встал с Мусой и Харуном у входа в шатёр встречи. 19Когда Корах собрал против них всех сообщников к входу в шатёр встречи, слава Вечного явилась всему народу. 20Вечный сказал Мусе и Харуну:

21– Отделитесь от этого народа, чтобы Я уничтожил их в одно мгновение.

22Но Муса и Харун пали лицом на землю и сказали:

– Всевышний, Бог духов всякой плоти, неужели Ты прогневаешься на весь народ, когда согрешит один?

Наказание Кораха, Датана и Авирама

23Тогда Вечный сказал Мусе:

24– Скажи народу: «Отойдите от жилищ Кораха, Датана и Авирама».

25Муса встал и пошёл к Датану и Авираму, а старейшины Исраила пошли за ним. 26Он предупредил народ:

– Отойдите от шатров этих нечестивцев! Не трогайте ничего из их пожитков, иначе вы погибнете из-за их грехов.

27Они отошли от жилищ Кораха, Датана и Авирама. Датан и Авирам вышли и стояли с жёнами, сыновьями и маленькими детьми у входов в свои шатры.

28И Муса сказал:

– Вот как вы узнаете, что Вечный послал меня сделать всё это, и что я делаю это не по своей воле: 29если они умрут обычной смертью и участь их будет подобна участи всех людей, то Вечный меня не посылал. 30Но если Вечный сотворит небывалое, если под ними разверзнется земля и поглотит их со всем их добром, и они живыми сойдут в мир мёртвых, то вы поймёте, что эти люди презирали Вечного.

31Едва он окончил говорить это, земля под ними разошлась. 32Земля разверзлась и поглотила их и их сородичей – всех людей Кораха со всем их имуществом. 33Они живыми сошли в мир мёртвых, со всем своим добром; земля сомкнулась над ними, и они сгинули из среды народа. 34Под их крики исраильтяне, которые были вокруг, разбежались, крича: «Земля хочет поглотить и нас!»

35Вечный послал огонь и сжёг двести пятьдесят человек, которые приносили благовония.

36Вечный сказал Мусе:

37– Вели Элеазару, сыну священнослужителя Харуна, собрать сосуды среди сожжённых останков и разбросать из них угли, потому что они святы, – 38это сосуды грешников, которые поплатились жизнью. Расплющь сосуды в листы, чтобы покрыть ими жертвенник, так как их принесли Вечному, и они стали освящёнными. Пусть они будут для исраильтян предостережением.

39Священнослужитель Элеазар собрал бронзовые сосуды, принесённые сожжёнными, и их расплющили, чтобы покрыть жертвенник, 40как повелел ему через Мусу Вечный. Таково было напоминание исраильтянам, что никому, кроме потомка Харуна, нельзя приходить, чтобы возжигать благовония перед Вечным, чтобы не разделить участь Кораха и его сообщников.

Муса и Харун заступаются за народ

41На другой день всё общество исраильтян роптало на Мусу и Харуна. «Вы погубили народ Вечного», – говорили они. 42Но когда, собравшись против Мусы и Харуна, народ повернулся к шатру встречи, его покрыло облако и явилась слава Вечного. 43Муса и Харун подошли к шатру встречи, 44и Вечный сказал Мусе:

45– Оставь этот народ, чтобы Я уничтожил их в одно мгновение.

Они пали лицом на землю.

46Муса сказал Харуну:

– Возьми сосуд, положи в него горящие угли с жертвенника и благовония и поспеши к народу, чтобы очистить его. Вечный разгневался; начался мор.

47Харун сделал, как сказал ему Муса, и поспешил к народу. Среди них уже начался мор, но Харун возжёг благовония и очистил народ. 48Он встал между мёртвыми и живыми, и мор прекратился. 49Но четырнадцать тысяч семьсот человек умерло от мора, не считая тех, кто умер из-за Кораха. 50Харун вернулся к Мусе к входу в шатёр встречи, потому что мор прекратился.