Numeri 12 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 12:1-16

Miriamu ndi Aaroni Atsutsana ndi Mose

1Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi. 2Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.

3(Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).

4Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko. 5Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo, 6Mulungu anati, “Mverani mawu anga:

“Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu,

ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya,

ndimayankhula naye mʼmaloto.

7Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga;

Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.

8Ndimayankhula naye maso ndi maso,

momveka bwino osati mophiphiritsa;

ndipo amaona maonekedwe a Yehova.

Nʼchifukwa chiyani simunaope

kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”

9Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.

10Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate; 11ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa. 12Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”

13Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”

14Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.” 15Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.

16Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.

Korean Living Bible

민수기 12:1-16

모세를 비난하는 미리암과 아론

1어느 날 미리암과 아론이 모세가 구스 여자와 결혼한 것을 비난하며

2“여호와가 모세를 통해서만 말씀하셨느냐? 우리를 통해서도 말씀하시지 않았느냐?” 하고 투덜대자 여호와께서 이 말을 들으셨다.

3모세는 세상의 그 누구보다도 겸손한 사람이었다.

4여호와께서 갑자기 모세와 아론과 미리암에게 “너희 세 사람은 모두 성막으로 나오너라” 하고 말씀하셨다. 그래서 그들이 성막으로 나아가자

5여호와께서 구름 기둥 가운데 내려와 성막 입구에 서서 아론과 미리암을 부르셨다. 그들이 앞으로 나아가자

6여호와께서 이렇게 말씀하셨다. “내가 하는 말을 잘 들어라. 예언자에게는 내가 환상으로 나를 나타내며 꿈으로 말하지만

7내 종 모세에게는 그렇게 하지 않는다. 그는 내 집에 충성스러운 종이므로

8내가 그와 말할 때는 직접 대면하여 분명하게 말하고 모호한 말로 하지 않는다. 내 종 모세는 내 모습까지 보는 자인데 너희가 어떻게 두려운 줄 모르고 감히 그를 비난하느냐?”

9여호와께서 그들에게 분노하시고 떠나시자

10구름이 성막 위에서 사라지고 미리암은 갑자기 문둥병에 걸려 온 몸이 하얗게 되었다. 아론이 이것을 보고

11모세에게 “우리가 어리석었네. 우리의 잘못을 용서해 주게.

12제발 누님이 모태에서 살이 반이나 썩어 죽어서 나온 아기처럼 되지 않게 해 다오” 하였다.

13그래서 모세가 여호와께 “하나님이시여, 누님을 고쳐 주소서” 하고 부르짖자

14여호와께서 모세에게 말씀하셨다. “만일 그 아버지가 그녀에게 침을 뱉았어도 7일간은 부끄러워하지 않겠느냐? 그러므로 너는 그녀를 7일 동안 진영 밖에 가두어 두었다가 그 기간이 지나면 다시 들어오게 하여라.”

15그래서 미리암은 7일 동안 진영 밖에 갇혀 있었으며 백성들은 그녀가 다시 들어올 때까지 행진하지 않았다.

16그 후에 그들은 하세롯을 떠나 바란 광야에 진을 쳤다.