Numeri 10 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 10:1-36

Malipenga Asiliva

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa. 3Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano. 4Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe. 5Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka. 6Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo. 7Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.

8“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse. 9Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu. 10Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”

Aisraeli Achoka ku Sinai

11Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni. 12Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani. 13Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.

14Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu. 15Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara, 16Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni. 17Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.

18Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri. 19Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai, 20ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi. 21Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.

22Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo. 23Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase. 24Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.

25Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai. 26Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri, 27ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani. 28Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.

29Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”

30Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”

31Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu. 32Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”

33Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo. 34Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.

35Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti,

“Dzukani, Inu Yehova!

Adani anu abalalike;

Odana nanu athawe pamaso panu.

36“Pamene likupumula, ankanena kuti,

“Bwererani, Inu Yehova,

ku chinamtindi cha Aisraeli.”

New International Version

Numbers 10:1-36

The Silver Trumpets

1The Lord said to Moses: 2“Make two trumpets of hammered silver, and use them for calling the community together and for having the camps set out. 3When both are sounded, the whole community is to assemble before you at the entrance to the tent of meeting. 4If only one is sounded, the leaders—the heads of the clans of Israel—are to assemble before you. 5When a trumpet blast is sounded, the tribes camping on the east are to set out. 6At the sounding of a second blast, the camps on the south are to set out. The blast will be the signal for setting out. 7To gather the assembly, blow the trumpets, but not with the signal for setting out.

8“The sons of Aaron, the priests, are to blow the trumpets. This is to be a lasting ordinance for you and the generations to come. 9When you go into battle in your own land against an enemy who is oppressing you, sound a blast on the trumpets. Then you will be remembered by the Lord your God and rescued from your enemies. 10Also at your times of rejoicing—your appointed festivals and New Moon feasts—you are to sound the trumpets over your burnt offerings and fellowship offerings, and they will be a memorial for you before your God. I am the Lord your God.”

The Israelites Leave Sinai

11On the twentieth day of the second month of the second year, the cloud lifted from above the tabernacle of the covenant law. 12Then the Israelites set out from the Desert of Sinai and traveled from place to place until the cloud came to rest in the Desert of Paran. 13They set out, this first time, at the Lord’s command through Moses.

14The divisions of the camp of Judah went first, under their standard. Nahshon son of Amminadab was in command. 15Nethanel son of Zuar was over the division of the tribe of Issachar, 16and Eliab son of Helon was over the division of the tribe of Zebulun. 17Then the tabernacle was taken down, and the Gershonites and Merarites, who carried it, set out.

18The divisions of the camp of Reuben went next, under their standard. Elizur son of Shedeur was in command. 19Shelumiel son of Zurishaddai was over the division of the tribe of Simeon, 20and Eliasaph son of Deuel was over the division of the tribe of Gad. 21Then the Kohathites set out, carrying the holy things. The tabernacle was to be set up before they arrived.

22The divisions of the camp of Ephraim went next, under their standard. Elishama son of Ammihud was in command. 23Gamaliel son of Pedahzur was over the division of the tribe of Manasseh, 24and Abidan son of Gideoni was over the division of the tribe of Benjamin.

25Finally, as the rear guard for all the units, the divisions of the camp of Dan set out under their standard. Ahiezer son of Ammishaddai was in command. 26Pagiel son of Okran was over the division of the tribe of Asher, 27and Ahira son of Enan was over the division of the tribe of Naphtali. 28This was the order of march for the Israelite divisions as they set out.

29Now Moses said to Hobab son of Reuel the Midianite, Moses’ father-in-law, “We are setting out for the place about which the Lord said, ‘I will give it to you.’ Come with us and we will treat you well, for the Lord has promised good things to Israel.”

30He answered, “No, I will not go; I am going back to my own land and my own people.”

31But Moses said, “Please do not leave us. You know where we should camp in the wilderness, and you can be our eyes. 32If you come with us, we will share with you whatever good things the Lord gives us.”

33So they set out from the mountain of the Lord and traveled for three days. The ark of the covenant of the Lord went before them during those three days to find them a place to rest. 34The cloud of the Lord was over them by day when they set out from the camp.

35Whenever the ark set out, Moses said,

“Rise up, Lord!

May your enemies be scattered;

may your foes flee before you.”

36Whenever it came to rest, he said,

“Return, Lord,

to the countless thousands of Israel.”