Numeri 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 1:1-54

Kalembera

1Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti, 2“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi. 3Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali. 4Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi. 5Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa:

Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,

6Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,

7Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,

8Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,

9Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,

10Mwa ana a Yosefe:

kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi;

kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;

11Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,

12Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,

13Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,

14Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,

15Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”

16Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.

17Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa, 18ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi 19monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:

20Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 21Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.

22Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 23Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.

24Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 25Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.

26Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 27Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.

28Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 29Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.

30Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 31Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.

32Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe:

Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 33Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.

34Kuchokera mwa zidzukulu za Manase:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 35Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.

36Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 37Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.

38Kuchokera mwa zidzukulu za Dani:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 39Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.

40Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 41Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.

42Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali:

Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 43Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.

44Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake. 45Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo. 46Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.

47Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena. 48Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, 49“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli. 50Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo. 51Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa. 52Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake. 53Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”

54Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

New Russian Translation

Числа 1:1-54

Перепись израильского народа

1В первый день второго месяца, во второй год после исхода израильтян из Египта, Господь говорил с Моисеем в шатре собрания в Синайской пустыне. Он сказал:

2– Сделайте перепись израильского народа по кланам и семьям, перечисляя каждого мужчину по имени, одного за другим. 3Исчисли вместе с Аароном всех израильтян, годных к военной службе, от двадцати лет и старше, по ополчениям. 4Пусть от каждого рода вам помогает один человек, который является главой своей семьи. 5Вот имена тех, кто будет вам помогать:

от Рувима – Элицур, сын Шедеура;

6от Симеона – Шелумиил, сын Цуришаддая;

7от Иуды – Нахшон, сын Аминадава;

8от Иссахара – Нафанаил, сын Цуара;

9от Завулона – Элиав, сын Хелона;

10от сыновей Иосифа:

от Ефрема – Элишама, сын Аммиуда;

от Манассии – Гамалиил, сын Педацура;

11от Вениамина – Авидан, сын Гидеония;

12от Дана – Ахиезер, сын Аммишаддая;

13от Асира – Пагиил, сын Охрана;

14от Гада – Элиасаф, сын Дегуила;

15от Неффалима – Ахира, сын Енана.

16Это те, кто был назначен от общества, вожди отцовских родов. Это главы кланов Израиля.

17Моисей и Аарон с людьми, указанными поименно, 18созвали собрание в первый день второго месяца. Израильтяне объявляли свои родословия по кланам и семьям, и мужчины от двадцати лет и старше были перечислены по именам, один за другим, 19как повелел Моисею Господь. Так он исчислил их в Синайской пустыне:

20из потомков Рувима, первенца Израиля:

все мужчины от двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, один за другим, по свидетельствам их кланов и семей. 21В роду Рувима их было 46 500.

22Из потомков Симеона:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были исчислены и перечислены по именам, один за другим, по свидетельствам их кланов и семей. 23В роду Симеона их было 59 300.

24Из потомков Гада:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 25В роду Гада их было 45 650.

26Из потомков Иуды:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 27В роду Иуды их было 74 600.

28Из потомков Иссахара:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 29В роду Иссахара их было 54 400.

30Из потомков Завулона:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 31В роду Завулона их было 57 400.

32Из сыновей Иосифа:

из потомков Ефрема:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 33В роду Ефрема их было 40 500.

34Из потомков Манассии:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 35В роду Манассии их было 32 200.

36Из потомков Вениамина:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 37В роду Вениамина их было 35 400.

38Из потомков Дана:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 39В роду Дана их было 62 700.

40Из потомков Асира:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 41В роду Асира их было 41 500.

42Из потомков Неффалима:

все мужчины двадцати лет и старше, годные к военной службе, были перечислены по именам, по свидетельствам их кланов и семей. 43В роду Неффалима их было 53 400.

44Это мужчины, исчисленные Моисеем и Аароном и двенадцатью вождями Израиля, из которых каждый представлял свою семью. 45Все израильтяне двадцати лет и старше, годные в Израиле к военной службе, были исчислены по их семьям. 46Всего их было 603 550.

47Однако семьи из рода Левия, не были исчислены вместе с остальными. 48Господь сказал Моисею:

49– Не исчисляй род Левия и не включай их в перепись вместе с остальными израильтянами. 50Поручи левитам скинию свидетельства, всю ее утварь и все, что при ней. Пусть они будут носить скинию и всю ее утварь, пусть заботятся о них и разбивают вокруг скинии свой лагерь. 51Когда скинию нужно будет перенести, пусть левиты снимают ее, а когда ее нужно будет поставить, то пусть и это делают они. Если к ней приблизится посторонний, он будет предан смерти. 52Израильтяне будут ставить шатры по ополчениям, каждый в своем лагере, под своим знаменем. 53Но левиты будут ставить шатры вокруг скинии свидетельства, чтобы на род израильтян не пал гнев. Левиты будут нести стражу при скинии свидетельства.

54Израильтяне сделали все точно так, как повелел Моисею Господь.