Numeri 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 1:1-54

Kalembera

1Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti, 2“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi. 3Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali. 4Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi. 5Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa:

Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,

6Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,

7Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,

8Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,

9Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,

10Mwa ana a Yosefe:

kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi;

kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;

11Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,

12Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,

13Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,

14Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,

15Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”

16Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.

17Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa, 18ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi 19monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:

20Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 21Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.

22Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 23Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.

24Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 25Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.

26Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 27Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.

28Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 29Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.

30Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 31Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.

32Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe:

Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 33Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.

34Kuchokera mwa zidzukulu za Manase:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 35Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.

36Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 37Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.

38Kuchokera mwa zidzukulu za Dani:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 39Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.

40Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 41Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.

42Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali:

Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 43Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.

44Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake. 45Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo. 46Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.

47Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena. 48Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, 49“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli. 50Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo. 51Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa. 52Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake. 53Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”

54Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

Bibelen på hverdagsdansk

4. Mosebog 1:1-54

Israels første folketælling

1På den første dag i den anden måned1,1 Den anden måned svarer til april-maj. året efter, at israelitterne havde forladt Egypten, talte Herren til Moses i åbenbaringsteltet, mens folket opholdt sig i Sinais ørken.

Herren sagde: 2-4„Lav en liste over alle våbenføre mænd over 20 år med deres stamme- og slægtsnavne. Du og Aron skal være ansvarlige for optællingen, som skal uddelegeres til en leder fra hver enkelt stamme. 5Følgende ledere skal hjælpe jer: fra Rubens stamme: Elitzur, Shedeurs søn; 6fra Simeons stamme: Shelumiel, Zurishaddajs søn; 7fra Judas stamme: Nahshon, Amminadabs søn; 8fra Issakars stamme: Netanel, Suars søn; 9fra Zebulons stamme: Eliab, Helons søn; 10fra Efraims, Josefs søns, stamme: Elishama, Ammihuds søn; fra Manasses, Josefs søns, stamme: Gamliel, Pedasurs søn; 11fra Benjamins stamme: Abidan, Gidonis søn; 12fra Dans stamme: Ahiezer, Ammishaddajs søn; 13fra Ashers stamme: Pagiel, Okrans søn; 14fra Gads stamme: Eljasaf, Deuels søn; 15fra Naftalis stamme: Ahira, Enans søn.” 16Disse mænd var ledere blandt folket, overhoveder for hver deres slægt.

17-46Samme dag sammenkaldte Moses, Aron og de ovennævnte ledere samtlige våbenføre mænd i Israel over 20 år. Hver person fik besked på at oplyse sit stamme- og slægtsnavn, sådan som Herren havde befalet Moses. Her følger den samlede opgørelse: Jakobs førstefødte søns, Rubens, stamme: 46.500; Simeons stamme: 59.300; Gads stamme: 45.650; Judas stamme: 74.600; Issakars stamme: 54.400; Zebulons stamme: 57.400; Efraims, Josefs søns, stamme: 40.500; Manasses, Josefs søns, stamme: 32.200; Benjamins stamme: 35.400; Dans stamme: 62.700; Ashers stamme: 41.500; Naftalis stamme: 53.400. Det samlede antal våbenføre mænd udgjorde 603.550 personer.

47-49Dette tal indbefatter dog ikke levitterne, for Herren havde sagt til Moses: „Du må ikke bruge levitterne som soldater, og du skal ikke tage dem med på listen. 50Jeg har nemlig givet dem ansvar for at tage sig af min bolig, det hellige telt, som indeholder pagtens ark. Derfor skal de altid have deres lejr i nærheden af boligen. 51Det er levitternes opgave at pakke teltet sammen og rejse det igen, og hvis nogen andre blander sig i den opgave eller blot rører ved teltet, skal de henrettes. 52Resten af Israels stammer skal tildeles hver deres lejrplads med hver deres banner, 53men levitterne skal slå lejr rundt om teltet med pagtens ark, så de udgør en mur mellem folket og Herren, for at ingen af de menige israelitter skal komme til at røre ved teltet og rammes af Herrens vrede.”

54Israels folk fulgte omhyggeligt de befalinger, som Herren havde givet Moses.