Numeri 1 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 1:1-54

Kalembera

1Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti, 2“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi. 3Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali. 4Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi. 5Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa:

Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,

6Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,

7Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,

8Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,

9Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,

10Mwa ana a Yosefe:

kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi;

kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;

11Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,

12Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,

13Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,

14Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,

15Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”

16Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.

17Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa, 18ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi 19monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:

20Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 21Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.

22Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 23Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.

24Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 25Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.

26Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 27Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.

28Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 29Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.

30Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 31Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.

32Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe:

Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 33Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.

34Kuchokera mwa zidzukulu za Manase:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 35Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.

36Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 37Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.

38Kuchokera mwa zidzukulu za Dani:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 39Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.

40Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 41Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.

42Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali:

Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 43Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.

44Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake. 45Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo. 46Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.

47Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena. 48Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, 49“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli. 50Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo. 51Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa. 52Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake. 53Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”

54Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

La Bible du Semeur

Nombres 1:1-54

Recensement et organisation des Israélites

Le premier recensement d’Israël

1Le premier jour du deuxième mois de la deuxième année après la sortie d’Egypte1.1 C’est-à-dire onze mois après l’arrivée des Israélites dans le désert du Sinaï (Ex 19.1), un mois après l’achèvement du tabernacle (Ex 40.17) et quinze jours après la célébration de la Pâque au Sinaï (9.1-5)., l’Eternel s’adressa à Moïse dans le désert du Sinaï dans la tente de la Rencontre. Il lui dit : 2Faites le recensement de toute la communauté des Israélites selon leurs familles et leurs groupes familiaux, en comptant tous les hommes 3âgés de vingt ans et plus, tous ceux qui sont aptes à servir dans l’armée d’Israël. Toi et Aaron, vous les dénombrerez par corps d’armée.

4Vous vous adjoindrez un homme par tribu ; vous prendrez celui qui se trouve à la tête de son groupe familial. 5Voici le nom des hommes qui vous assisteront1.5 Les tribus sont mentionnées dans l’ordre suivant : 1. les fils de Léa (sans Lévi, v. 47) ; 2. les fils de Rachel ; 3. les fils des servantes. Les noms de ces hommes reviennent aux chap. 2 ; 7 et 10. :

– pour Ruben : Elitsour, fils de Shedéour ;

6pour Siméon : Sheloumiel, fils de Tsourishaddaï ;

7pour Juda : Nahshôn, fils d’Amminadab ;

8pour Issacar : Netanéel, fils de Tsouar ;

9pour Zabulon : Eliab, fils de Hélôn ;

10pour les fils de Joseph :

pour Ephraïm : Elishama, fils d’Ammihoud ;

pour Manassé : Gamliel, fils de Pédahtsour ;

11pour Benjamin : Abidân, fils de Guideoni ;

12pour Dan : Ahiézer, fils d’Ammishaddaï ;

13pour Aser : Paguiel, fils d’Okrân ;

14pour Gad : Eliasaph, fils de Deouel1.14 L’ancienne version grecque et la version syriaque ont : Reouel (voir 2.14). ;

15pour Nephtali : Ahira, fils d’Enân.

16Tels sont les membres de la communauté qui furent convoqués. C’étaient les chefs de leurs tribus, ils étaient aussi à la tête des corps d’armée d’Israël. 17Moïse et Aaron s’adjoignirent ces hommes qui avaient été nommément désignés 18et convoquèrent toute l’assemblée, le premier jour du second mois ; les Israélites furent recensés, selon leurs familles et leurs groupes familiaux, on releva le nom des hommes de vingt ans et au-dessus, un par un, 19comme l’Eternel l’avait ordonné à Moïse. De cette manière, Moïse fit leur dénombrement au désert du Sinaï.

20On établit le recensement des descendants de Ruben, premier-né d’Israël, par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 21On en dénombra 46 5001.21 Tous les nombres sont arrondis à la centaine (sauf pour Gad, v. 25, dont le total est aussi arrondi dans certaines versions). Selon certains, les milliers que contiennent les divers nombres du recensement ne désigneraient pas mille individus mais des corps d’armées moins nombreux ou des chefs de troupe, conformément au sens que peut avoir le terme en hébreu (voir, p. ex., 31.14, 48). Une telle interprétation pose le problème du total des v. 45-46..

22On établit le recensement des descendants de Siméon par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 23On en dénombra 59 300.

24On établit le recensement des descendants de Gad par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 25On en dénombra 45 650.

26On établit le recensement des descendants de Juda par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 27On en dénombra 74 600.

28On établit le recensement des descendants d’Issacar par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 29On en dénombra 54 400.

30On établit le recensement des descendants de Zabulon par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 31On en dénombra 57 400.

32Parmi les fils de Joseph1.32 Les descendants de Lévi étant exclus de ce recensement (v. 47), les descendants de Joseph sont groupés en deux tribus composées de la famille de ses deux fils, Ephraïm et Manassé. Le nombre de douze tribus est ainsi maintenu, et Joseph, qui devait recevoir le droit d’aînesse (1 Ch 5.2), a un héritage double. : on établit le recensement des descendants d’Ephraïm par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 33On en dénombra 40 500. 34On établit le recensement des descendants de Manassé par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 35On en dénombra 32 200.

36On établit le recensement des descendants de Benjamin par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 37On en dénombra 35 400.

38On établit le recensement des descendants de Dan par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 39On en dénombra 62 700.

40On établit le recensement des descendants d’Aser par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 41On en dénombra 41 500.

42On établit le recensement des descendants de Nephtali par familles et par groupes familiaux en relevant un par un le nom de tous les hommes de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée. 43On en dénombra 53 400.

44Tels sont les effectifs que recensèrent Moïse et Aaron, assistés de douze chefs d’Israël, un par tribu. 45Le total des Israélites de vingt ans et plus, aptes à servir dans l’armée, dont on fit le recensement selon leurs groupes familiaux, 46était de 603 550.

47Les lévites, en tant que tribu patriarcale, ne furent pas recensés avec les autres tribus. 48En effet, l’Eternel avait dit à Moïse : 49N’inclus pas la tribu de Lévi dans le recensement et ne les compte pas avec les Israélites1.49 Ils seront recensés à part (3.14-39 ; 4.34-49).. 50Charge-les du service du tabernacle qui abrite l’acte de l’alliance1.50 C’est-à-dire les dix commandements gravés sur des tablettes de pierre (Ex 31.18 ; 32.15 ; 34.29) déposées dans le coffre (Ex 25.16, 21 ; 40.20)., de tous ses ustensiles et de tout son matériel ; ce sont eux qui transporteront le tabernacle avec tous ses accessoires et qui en assureront le service ; ils camperont autour du tabernacle. 51Quand il sera déplacé, les lévites le démonteront, puis ils le dresseront au nouveau campement. Tout membre étranger à leur tribu qui en approchera sera puni de mort. 52Les Israélites camperont chacun dans l’aire qui lui sera assignée, sous sa bannière, et selon leurs corps d’armée. 53Les lévites camperont autour du tabernacle qui abrite l’acte de l’alliance, pour que ma colère ne s’abatte pas sur la communauté des Israélites. Les lévites prendront soin du tabernacle.

54Les Israélites obéirent à tous les ordres que l’Eternel avait donnés à Moïse et les accomplirent.