Nehemiya 9 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 9:1-38

Aisraeli Avomereza Kuchimwa Kwawo

1Pa tsiku la 24 la mwezi womwewo, Aisraeli anasonkhana pamodzi ndi kusala chakudya, kuvala ziguduli ndi kudzithira dothi pa mutu. 2Aisraeliwa anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anayimirira nayamba kuwulula machimo awo ndi zolakwa za makolo awo. 3Anthuwo anayimirira pomwepo, ndipo anamva mawu a mʼbuku la malamulo a Yehova akuwerengedwa kwa maora enanso atatu ndipo anakhala maora ena atatu akuwulula machimo awo ndi kupembedza Yehova Mulungu wawo. 4Pa makwerero okhalapo alevi anayimirirapo anthu awa: Yesuwa, Bani, Kadimieli, Sebaniya, Buni, Serebiya, Bani ndi Kenani. Iwowa ankapemphera mokweza mawu kwa Yehova Mulungu wawo. 5Ndipo Alevi awa: Yesuwa, Kadimieli, Bani, Hasabaneya, Serebiya, Hodiya, Sebaniya ndi Petahiya anati: “Imirirani ndipo mutamande Yehova Mulungu wanu, amene ndi wamuyaya.”

“Litamandike dzina lake laulemerero limene liposa madalitso ndi matamando onse. 6Inu nokha ndiye Yehova. Munalenga kumwamba, ngakhale kumwambamwamba, zolengedwa zonse zimene zili mʼmenemo. Munalenga dziko ndi zonse zokhalamo, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo. Zonse mumazisunga ndi moyo ndipo zonse za kumwamba zimakupembedzani.

7“Inu ndinu Yehova Mulungu amene munasankha Abramu ndi kumutulutsa mʼdziko la Uri wa ku Kaldeya ndi kumutcha dzina lake Abrahamu. 8Inu munaona kuti mtima wake unali wokhulupirika kwa inu, ndipo munapangana naye pangano lakuti mudzapereka kwa zidzukulu zake dziko la Akanaani Ahiti, Aamori, Aperezi, Ayebusi ndi Agirigasi. Inu mwasunga lonjezo lanu chifukwa ndinu wolungama.

9“Munaona kuzunzika kwa makolo athu ku Igupto. Munamva kufuwula kwawo pa Nyanja Yofiira. 10Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa kutsutsana ndi Farao, pamaso pa Farao, nduna zake ndi anthu onse a mʼdziko lake, pakuti Inu munadziwa kuti anazunza makolo athu. Inu munadzipangira nokha dzina, monga zilili mpaka lero lino. 11Inu munagawa nyanja anthu anu akupenya, kotero kuti anadutsa powuma, koma munamiza mʼmadzi akuya anthu amene ankawalondola monga mmene uchitira mwala mʼmadzi ozama. 12Masana munkawunikira ndi chipilala cha mtambo ndipo usiku munkawunikira ndi chipilala cha moto njira yonse imene ankayendamo.

13“Munatsika pa Phiri la Sinai, ndipo munawayankhula kuchokera kumwamba. Munawapatsa malangizo olungama, ziphunzitso zoona ndiponso malamulo abwino. 14Inu munawadziwitsa kuti tsiku lanu la Sabata ndi loyera ndipo munawapatsa malamulo ndi ziphunzitso. 15Pamene anali ndi njala munawapatsa buledi wochokera kumwamba. Pamene anali ndi ludzu munawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe. Munawawuza kuti apite kukalanda dziko limene munalonjeza kuti mudzawapatsa.”

16“Koma makolo athu anadzikuza ndi kuwumitsa khosi, ndipo iwo sanamvere malamulo anu. 17Anakana kumvera ndipo sanakumbukire zodabwitsa zimene munachita pakati pawo. Koma iwo anawumitsa khosi, nakuwukirani podzisankhira okha mtsogoleri kuti awatsogolere kubwerera ku ukapolo ku dziko la Igupto. Koma ndinu Mulungu wokhululukira, wokoma mtima ndi wachifundo wosapsa mtima msanga ndi wachikondi chachikulu chosasinthika. Choncho Inu simunawasiye. 18Ngakhale pamene iwo anadziwumbira fano la mwana wangʼombe ndi kuti, ‘Uyu ndi mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto,’ kapena pamene anachita chipongwe choopsa.

19“Koma Inu ndi chifundo chanu chachikulu, simunawasiye mʼchipululu. Chipilala cha mtambo sichinasiye kuwatsogolera pa njira yawo masana ndipo chipilala cha moto sichinasiye kuwatsogolera pa njira yawo usiku. 20Inu munawapatsa mzimu wanu wabwino kuti uwalangize. Inu simunawamane chakudya cha mana chija, ndipo munawapatsa madzi akumwa. 21Munawasunga zaka makumi anayi mʼchipululu ndipo sanasowe kanthu kalikonse. Zovala zawo sizinathe kapena mapazi awo kutupa.”

22“Inu munawapatsa mafumu ndi mayiko mʼmanja mwawo. Munawagawiranso mayiko achilendo akutali kwambiri. Munabwera nawo mʼdziko la Sihoni mfumu ya Hesiboni ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani kuti alowemo nʼkulitenga kukhala lawo. 23Munachulukitsa ana awo aamuna ngati nyenyezi za mlengalenga. Ndipo munawabweretsa mʼdziko limene munawuza makolo awo kuti alilowe ndi kulitenga. 24Choncho zidzukulu zawo zinapita ndi kukalandira dzikolo. Inu munagonjetsa pamaso pawo, Akanaani amene amakhala mʼdzikolo. Inde munapereka mʼmanja mwawo mafumu awo pamodzi ndi anthu a mʼdzikomo kuti achite nawo monga angafunire. 25Iwo analanda mizinda yotetezedwa ndi dziko lachonde. Anatenganso nyumba zodzaza ndi zinthu zonse zabwino, zitsime zokumbidwa kale, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndi mitengo yambiri ya zipatso. Ndipo anadya nakhuta ndipo anali athanzi. Choncho ankakondwa chifukwa cha ubwino wanu wopambana.

26“Komabe iwo anakhala osamvera ndipo anakuwukirani nafulatira malamulo anu. Anapha aneneri anu, amene anakawadandaulira kuti abwerere kwa Inu. Anachita chipongwe choopsa. 27Pamene anazunzidwa anafuwulira kwa Inu, ndipo Inu munawamvera muli kumwambako. Ndipo mwa chifundo chanu chachikulu munkawapatsa atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo.”

28“Koma akangokhala pa mtendere ankayambanso kuchita zoyipa pamaso panu. Choncho munkawapereka mʼmanja mwa adani awo amene ankawalamulira. Komabe pamene ankabwerera ndi kumalira kwa Inu, Inu munkawamva muli kumwambako. Chifukwa cha chifundo chanu chochuluka, nthawi zonse munkawapulumutsa.

29“Inu munkawachenjeza kuti abwerere ndi kuyamba kutsata malamulo anu. Koma iwo ankadzitukumula ndipo sankamvera malamulo anu. Iwo anachimwira malangizo anu amene munati ‘Amapatsa moyo kwa munthu wowamvera.’ Iwo ankakufulatirani, nawumitsa makosi awo osafuna kukumverani. 30Munapirira nawo kwa zaka zambiri. Munkawachenjeza ndi Mzimu wanu kudzera mwa aneneri anu, koma iwo sankakumverani. Choncho munawapereka mʼmanja mwa anthu a mayiko ena. 31Komabe mwachifundo chanu chachikulu simuwatheretu kapena kuwataya pakuti ndinu Mulungu wokoma mtima ndi wachifundo.

32“Nʼchifukwa chake, tsono, Inu Mulungu wathu, Mulungu wamkulu, wamphamvu ndi woopsa kwambiri mumasunga pangano ndi chikondi chosasinthika. Musalole kuti mavuto onse amene atigwera ife, mafumu athu, atsogoleri athu, ansembe athu, aneneri athu, makolo athu ndi anthu ena onse kuyambira nthawi ya mafumu a ku Asiriya mpaka lero aoneke ochepa pamaso panu. 33Koma Inu mwakhala wolungama pa zonse zimene zakhala zikutichitikira. Mwachita zokhulupirika, koma ife tachita zolakwa. 34Ndipotu mafumu athu, atsogoleri athu, ansembe athu ndi makolo athu sanatsatire mawu anu. Iwo sanalabadire za malamulo anu ngakhale mawu anu owachenjeza amene munawapatsa. 35Ngakhale ankadzilamulira okha, nʼkumalandira zabwino zochuluka mʼdziko lalikulu ndi lachonde limene munawapatsa, koma iwo sanakutumikireni kapena kusiya ntchito zawo zoyipa.

36“Tsono, taonani! Ife lero ndife akapolo, ndife akapolo mʼdziko limene munapereka kwa makolo athu kuti azidya zipatso zake ndi zabwino zake zonse. 37Tsono chifukwa cha machimo athu, mafumu amene munawayika kuti azitilamulira angodzilemeretsa ndi chuma chambiri cha dzikoli. Iwo ali ndi mphamvu zolamulira matupi athu ndi ngʼombe zathu momwe afunira. Zedi, ife tili mʼmavuto aakulu.”

Mgwirizano wa Anthu

38“Chifukwa cha zonsezi, ife tikuchita mgwirizano wokhazikika, pochita kulemba, ndipo atsogoleri athu, Alevi athu ndi ansembe athu asindikiza chidindo chawo pa mgwirizanowo.”

Bibelen på hverdagsdansk

Nehemiasʼ Bog 9:1-37

Folket bekender deres synd

1Den 24. dag i den syvende måned samledes folket igen i Jerusalem. Denne gang fastede de og klædte sig i sækkelærred og kom jord på hovedet for at vise deres sorg. 2Israelitterne skilte sig ud fra alle de fremmede og bekendte deres egen og deres forfædres synd. 3-4I tre timer blev der læst op af Toraen, mens folk stod op og lyttede. I de næste tre timer bekendte folket deres synd og tilbad Herren deres Gud under ledelse af levitterne Jeshua, Bani, Kadmiel, Shebanja, Bunni, Sherebja, Bani og Kenani, der alle stod på trapper eller forhøjninger.

5Derefter råbte levitterne Jeshua, Kadmiel, Bani, Hashabneja, Sherebja, Hodija, Shebanja og Petaja til folket: „Rejs jer og pris Herren, jeres Gud, fra evighed og til evighed! Højlovet være Herren, han som er langt større end nogen kan fatte og udtrykke.” Derefter ledte Ezra9,5 Oversat fra LXX, da den hebraiske tekst mangler indledningen. lovsangen:

6„Du er Gud, du er den eneste!

Du skabte himlen med alle dens stjerner,

jorden med alt, hvad den rummer,

havene med alt, hvad der findes i dem.

Fra dig udspringer alt liv,

og hele himlen tilbeder dig.

7Det var dig, Herre, vor Gud,

som udvalgte Abram,

førte ham ud af Ur i Kaldæa

og gav ham navnet Abraham.

8Du så hans hjertes trofasthed.

Derfor sluttede du pagt med ham

og gav ham løftet om landet,

hvor kana’anæerne og hittitterne,

amoritterne og perizzitterne,

jebusitterne og girgashitterne boede.

Og du holdt dit løfte, som du altid gør!

9Du så vores forfædres nød i Egypten,

hørte deres råb ved Det Røde Hav.

10Du fældede Farao og alle hans folk,

du vidste, hvor hovmodige de var.

Med tegn og undere greb du ind.

Derfor er du æret den dag i dag!

11Du kløvede havet for folkets øjne

og lod dem vandre tørskoet over.

Men deres fjender fejede du bort.

Du druknede dem på havets bund,

de sank som sten i bølgernes brus.

12Med en skysøjle viste du vej om dagen,

en ildsøjle lyste for dem om natten.

13Du steg ned på Sinais bjerg

og talte til folket fra Himlen.

Du gav dem retfærdige regler,

gode love, bud og befalinger.

14Du bød dem at holde Sabbatten hellig,

gav dem din lov gennem Moses, din tjener.

15Du stillede deres sult med brød fra himlen,

slukkede deres tørst med vand fra en klippe.

Du bød dem gå hen og indtage landet,

det land, du havde lovet dem.

16Men vores forfædre blev hovmodige,

hørte ikke på dine bud.

De adlød ikke dine befalinger,

17men fortsatte i deres ulydighed.

De glemte alle de undere,

som du gjorde engang.

De nægtede stædigt at ydmyge sig,

ville hellere tilbage til Egyptens slaveri!

Men du, oh Gud, er barmhjertig og god.

Du vredes nødigt, men tilgiver gerne.

Stor er din nåde og trofasthed,

du lod dem ikke i stikken.

18De støbte en tyrekalv af guld og råbte:

‚Her er den gud, som førte os ud af Egypten!’

De hånede dig op i dit åbne ansigt,

19men du viste dem alligevel nåde.

Du prisgav dem ikke i ørkenen!

Skysøjlen ledte dem fremad om dagen,

ildsøjlen viste dem vej om natten.

20Du vejledte dem ved din gode Ånd,

gav dem manna at spise

og vand til at slukke deres tørst.

21Du sørgede for dem i 40 år,

de manglede intet i ørkenen.

Deres klæder blev ikke slidt op,

deres fødder blev ikke ømme!

22Du gav dem sejr over mægtige folkeslag,

hjalp dem indtage landet stykke for stykke.

De erobrede kong Sihon af Heshbons land

og siden kong Og af Bashans rige.

23Du gjorde dem talrige som himlens stjerner.

Du førte dem ind i det dejlige land,

som du havde lovet deres forfædre,

at de skulle få i arv og eje.

24Deres børn kom og indtog landet.

Du overgav kana’anæerne til dem,

så de kunne gøre, hvad de ville,

med både konger og folkeslag.

25De indtog befæstede byer,

overtog fornemme huse med store vandreservoirer.

De overtog frugtbare jordlodder og vingårde,

olivenlunde og frugtplantager.

De spiste sig mætte og fede

og glædede sig over dine gaver.

26Men de gjorde oprør imod dig,

var ulydige og tilsidesatte din lov.

De myrdede dine profeter,

som formanede dem til omvendelse.

De hånede dig op i dit åbne ansigt.

27Da udleverede du dem til fjenderne,

og de kom i stor nød og ulykke.

I deres lidelser råbte de til dig,

og du hørte deres råb i din Himmel.

I din nåde sendte du dem ledere,

som frelste dem fra deres fjender.

28Men så snart der igen var fred,

gjorde de atter oprør imod dig.

Du gav dem påny i fjendevold,

så de igen måtte råbe til dig om hjælp.

Du hørte deres bøn i himlen

og reddede dem gang på gang.

29Du formanede dem til at følge din love,

men de ville ikke høre på dine bud.

De overtrådte de befalinger,

som netop skulle holde dem i live.

De var stædige og stivnakkede,

de nægtede at adlyde dig.

30I mange år bar du over med dem.

Du advarede dem ved din Ånd

gennem dine profeters ord.

Men de vendte det døve øre til,

og fremmede folk besejrede dem.

31Men på grund af din trofasthed,

udryddede du dem aldrig helt.

I din nåde svigtede du dem aldrig,

for du er en barmhjertig Gud.

32Og nu, Herre, vor Gud,

du store, mægtige, frygtindgydende,

du, som holder fast ved din pagt og nåde,

du ved, hvilke lidelser der har ramt os:

vores konger, fyrster og præster,

profeter, forfædre og hele vores folk,

siden assyrerkongerne indtog vores land.

33Hver gang du straffede os, var det retfærdigt.

Du havde ret, og vi havde uret.

34Vores konger adlød ikke dine love,

vores fyrster, præster og forfædre

lyttede ikke til dine gentagne advarsler.

35Du gav dem deres eget land,

du viste dem godhed gang på gang.

De nød godt af et stort og frugtbart land,

men vendte sig ikke fra deres ondskab.

36Derfor sidder vi som slaver i vores eget land,

det dejlige land, du gav vores forfædre

for at de skulle nyde dets goder.

37Landets rigdom går nu til de konger,

du har sat over os på grund af vores synd.

De har hånds- og halsret over os.

Vi er i stor nød!