Nehemiya 4 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 4:1-23

Adani a Nehemiya pa Ntchito Yake

1Sanibalati atamva kuti tikumanganso khoma anapsa mtima nayamba kuseka ndi kunyogodola Ayuda kwambiri. 2Ndipo anayankhula pamaso pa abale ake ndi asilikali a Samariya kuti, “Kodi Ayuda ofowokawa akuchita chiyani? Kodi iwo nʼkumanganso khoma? Kodi adzaperekanso nsembe? Kodi adzatsiriza ntchitoyi tsiku limodzi? Kodi adzachita kutenga miyala yakale ija ndi mmene inapseramo?”

3Tobiya wa ku Amoni, amene anali naye anati, “Chimene akumangacho ngati nkhandwe itakwerapo, itha kugwetsa khoma lawolo!”

4Tsono ndinayamba kupemphera kuti, “Timvereni, Inu Mulungu wathu, mmene akutinyozera. Mulole kuti mawu awo onyoza awabwerere, ndipo atengedwe ukapolo ku dziko lachilendo. 5Musawakhululukire mphulupulu zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu popeza aputa ukali wanu pamaso pa anthu omanga khoma.”

6Choncho ife tinamangabe khomalo kufikira lonse litafika theka la msinkhu wake, chifukwa chakuti anthu anagwira ntchitoyo ndi mtima wawo wonse.

7Koma pamene Sanibalati, Tobiya, Aarabu, Aamoni ndi anthu a ku Asidodi anamva kuti ntchito yokonzanso makoma a Yerusalemu ikupitirirabe ndipo kuti mipata ikutsekedwa, anapsa mtima kwambiri. 8Tsono onse anapangana za chiwembu kuti abwere ndi kudzathira nkhondo anthu a ku Yerusalemu ndi kuyambitsa mapokoso pakati pawo. 9Koma ife tinapemphera kwa Mulungu wathu ndipo tinayika alonda otiteteza kwa adaniwo usiku ndi usana.

10Pa nthawi yomweyi anthu a ku Yuda anati, “Mphamvu za anthu onyamula zinyalala zikutha ndipo pali zinyalala zambiri. Choncho ife sititha kumanga khomali.”

11Adani athunso anati, “Iwo asanadziwe izi, kapena kutiona, tidzakhala tili pakati pawo ndipo tidzawapha ndi kuyimitsa ntchitoyo.”

12Ndipo Ayuda amene ankhala pafupi ndi adani athuwo anabwera kakhumi konse kuchokera konse kumene ankakhala kudzatiwuza kuti tibwereko ku ntchito.

13Choncho kumbuyo kwa khoma, cha mʼmunsi mwake komanso malo amene anali asanathe ndinayikamo anthu mʼmabanja atatenga malupanga, mikondo ndi mauta awo. 14Popeza anthu ankachita mantha, tsono ndinawawuza anthu olemekezeka, akuluakulu ndiponso anthu onse kuti, “Musawaope. Kumbukirani kuti Ambuye ndi wamkulu ndipo ndi woopsa. Choncho menyerani nkhondo abale anu, ana aamuna ndi aakazi, akazi anu ndi nyumba zanu.”

15Adani athu atamva kuti ife tadziwa za chiwembu chawo, anadziwanso kuti Yehova walepheretsa zimene ankafuna kutichita. Choncho tinabwerera aliyense ku ntchito yake yomanga khoma.

16Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo mwake, theka la antchito anga linkagwira ntchito, pamene theka linalo limatenga mikondo, zishango, mauta ndi kuvala malaya azitsulo. Akuluakulu ankalimbikitsa Ayuda onse 17amene ankamanga khoma. Anthu onyamula zinyalala aja ankagwira ntchito ndi dzanja limodzi, dzanja linali atanyamula chida chankhondo. 18Mʼmisiri aliyense ankamangirira lupanga lake mʼchiwuno mwake akamagwira ntchito. Koma munthu woyimba lipenga anali pambali panga nthawi zonse.

19Ndipo ine ndinati kwa anthu olemekezeka ndi anthu ena onse, “Ntchitoyi ndi yayikulu ndipo ili padera lalikulu ndipo ifeyo takhala motayanatayana kwambiri pa khoma. 20Tsono kulikonse kumene muliko, mukamva kulira kwa lipenga bwerani mudzasonkhane kumene kuli ine kuno. Mulungu wathu adzatimenyera nkhondo.”

21Choncho enafe tinapitiriza kugwira ntchito, pamene theka lina linkanyamula mikondo kuyambira mʼbandakucha mpaka nyenyezi zitaoneka. 22Pa nthawi imeneyo ndinawuzanso anthuwo kuti, “Aliyense pamodzi ndi wantchito wake agone mu Yerusalemu kuti tikhale ndi otilondera usiku ndi kuti masana tizigwira ntchito.” 23Choncho ine, anzanga, antchito anga, ndi anthu otiteteza amene ankanditsata panalibe ndi mmodzi yemwe anavula zovala zake pogona. Aliyense anasunga chida chake chankhondo pambali pake.

New Russian Translation

Неемия 4:1-23

Противодействие строительству стены

1Когда Санбаллат услышал о том, что мы строим стену, он разозлился и сильно разгневался. Он издевался над иудеями 2и перед своими союзниками и самарийским войском говорил:

– Что делают эти жалкие иудеи? Неужели они восстановят свою стену? Неужели они станут приносить жертвы? Неужели они когда-нибудь закончат строительство? Неужто они оживят камни, притом обожженные, из этих груд праха?

3Аммонитянин Товия, стоящий рядом с ним, сказал:

– Да что они там строят, если даже лисица, взобравшись на эту каменную стену, обрушит ее!

4Услышь нас, Боже наш, потому что мы в презрении. Обрати их оскорбления на их же головы. Отдай их как добычу в землю плена. 5Не покрывай их вины и грехов их не удаляй от Своих глаз, потому что они оскорбляли строителей.

6И мы строили стену, и она достигла половины своей высоты, потому что народ работал от всего сердца. 7Но когда Санбаллат, Товия, арабы с аммонитянами и жители Ашдода услышали о том, что восстановление иерусалимских стен продвигается и проломы заделываются, они очень разозлились. 8Все вместе они сговорились пойти на Иерусалим войной и устроить в нем беспорядки. 9Но мы молились нашему Богу и выставляли против них стражу днем и ночью, чтобы отвратить эту угрозу.

10А тем временем народ иудейский говорил:

– Силы носильщиков на исходе, а здесь так много мусора, что мы не можем отстраивать стену.

11А наши враги говорили:

– Прежде чем они узнают о том, что происходит, или увидят нас, мы окажемся прямо среди них, перебьем их и остановим работу.

12Иудеи, которые жили рядом с ними, приходили и раз десять говорили нам:

– Со всех сторон они пойдут на нас4:12 Возможный текст; смысл этого места в еврейском тексте неясен..

13Тогда я разместил народ за самыми низкими участками стены на открытых местах, поставив их по семьям, с мечами, копьями и луками. 14Осмотрев все, я встал и сказал знати, начальствующим и остальному народу:

– Не бойтесь их. Помните Владыку, Который велик и грозен, и сражайтесь за своих братьев, сыновей, дочерей, жен и дома.

15Когда наши враги услышали, что мы знаем об их сговоре и о том, что Бог расстроил их планы, мы все вернулись к стене, каждый – к своей работе. 16С того дня и впредь половина моих слуг трудилась на постройке, а другая половина держала копья, щиты, луки и латы. Вожди находились позади всего дома иудейского, 17который строил стену. Носильщики тяжестей делали свою работу одной рукой, а в другой держали оружие, 18и каждый из строителей во время работы был препоясан мечом. А трубач находился рядом со мной.

19И я сказал знати, начальствующим и остальному народу:

– Работа велика и обширна, и мы разбросаны по стене далеко друг от друга. 20Где бы вы ни услышали звук рога, бегите к нам туда, откуда доносится звук. Наш Бог будет сражаться за нас!

21И мы продолжали работу, и половина людей держали копья от первых лучей солнца до появления звезд. 22В то время я еще сказал народу:

– Пусть каждый человек и его помощник ночуют в Иерусалиме, чтобы они могли сторожить ночью и работать днем.

23Ни я, ни мои братья, ни мои слуги, ни стражники, которые меня сопровождали, не снимали одежд; каждый держал свое оружие, когда ходил за водой4:23 Возможный текст; смысл этого места в еврейском тексте неясен..