Nehemiya 4 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 4:1-23

Adani a Nehemiya pa Ntchito Yake

1Sanibalati atamva kuti tikumanganso khoma anapsa mtima nayamba kuseka ndi kunyogodola Ayuda kwambiri. 2Ndipo anayankhula pamaso pa abale ake ndi asilikali a Samariya kuti, “Kodi Ayuda ofowokawa akuchita chiyani? Kodi iwo nʼkumanganso khoma? Kodi adzaperekanso nsembe? Kodi adzatsiriza ntchitoyi tsiku limodzi? Kodi adzachita kutenga miyala yakale ija ndi mmene inapseramo?”

3Tobiya wa ku Amoni, amene anali naye anati, “Chimene akumangacho ngati nkhandwe itakwerapo, itha kugwetsa khoma lawolo!”

4Tsono ndinayamba kupemphera kuti, “Timvereni, Inu Mulungu wathu, mmene akutinyozera. Mulole kuti mawu awo onyoza awabwerere, ndipo atengedwe ukapolo ku dziko lachilendo. 5Musawakhululukire mphulupulu zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu popeza aputa ukali wanu pamaso pa anthu omanga khoma.”

6Choncho ife tinamangabe khomalo kufikira lonse litafika theka la msinkhu wake, chifukwa chakuti anthu anagwira ntchitoyo ndi mtima wawo wonse.

7Koma pamene Sanibalati, Tobiya, Aarabu, Aamoni ndi anthu a ku Asidodi anamva kuti ntchito yokonzanso makoma a Yerusalemu ikupitirirabe ndipo kuti mipata ikutsekedwa, anapsa mtima kwambiri. 8Tsono onse anapangana za chiwembu kuti abwere ndi kudzathira nkhondo anthu a ku Yerusalemu ndi kuyambitsa mapokoso pakati pawo. 9Koma ife tinapemphera kwa Mulungu wathu ndipo tinayika alonda otiteteza kwa adaniwo usiku ndi usana.

10Pa nthawi yomweyi anthu a ku Yuda anati, “Mphamvu za anthu onyamula zinyalala zikutha ndipo pali zinyalala zambiri. Choncho ife sititha kumanga khomali.”

11Adani athunso anati, “Iwo asanadziwe izi, kapena kutiona, tidzakhala tili pakati pawo ndipo tidzawapha ndi kuyimitsa ntchitoyo.”

12Ndipo Ayuda amene ankhala pafupi ndi adani athuwo anabwera kakhumi konse kuchokera konse kumene ankakhala kudzatiwuza kuti tibwereko ku ntchito.

13Choncho kumbuyo kwa khoma, cha mʼmunsi mwake komanso malo amene anali asanathe ndinayikamo anthu mʼmabanja atatenga malupanga, mikondo ndi mauta awo. 14Popeza anthu ankachita mantha, tsono ndinawawuza anthu olemekezeka, akuluakulu ndiponso anthu onse kuti, “Musawaope. Kumbukirani kuti Ambuye ndi wamkulu ndipo ndi woopsa. Choncho menyerani nkhondo abale anu, ana aamuna ndi aakazi, akazi anu ndi nyumba zanu.”

15Adani athu atamva kuti ife tadziwa za chiwembu chawo, anadziwanso kuti Yehova walepheretsa zimene ankafuna kutichita. Choncho tinabwerera aliyense ku ntchito yake yomanga khoma.

16Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo mwake, theka la antchito anga linkagwira ntchito, pamene theka linalo limatenga mikondo, zishango, mauta ndi kuvala malaya azitsulo. Akuluakulu ankalimbikitsa Ayuda onse 17amene ankamanga khoma. Anthu onyamula zinyalala aja ankagwira ntchito ndi dzanja limodzi, dzanja linali atanyamula chida chankhondo. 18Mʼmisiri aliyense ankamangirira lupanga lake mʼchiwuno mwake akamagwira ntchito. Koma munthu woyimba lipenga anali pambali panga nthawi zonse.

19Ndipo ine ndinati kwa anthu olemekezeka ndi anthu ena onse, “Ntchitoyi ndi yayikulu ndipo ili padera lalikulu ndipo ifeyo takhala motayanatayana kwambiri pa khoma. 20Tsono kulikonse kumene muliko, mukamva kulira kwa lipenga bwerani mudzasonkhane kumene kuli ine kuno. Mulungu wathu adzatimenyera nkhondo.”

21Choncho enafe tinapitiriza kugwira ntchito, pamene theka lina linkanyamula mikondo kuyambira mʼbandakucha mpaka nyenyezi zitaoneka. 22Pa nthawi imeneyo ndinawuzanso anthuwo kuti, “Aliyense pamodzi ndi wantchito wake agone mu Yerusalemu kuti tikhale ndi otilondera usiku ndi kuti masana tizigwira ntchito.” 23Choncho ine, anzanga, antchito anga, ndi anthu otiteteza amene ankanditsata panalibe ndi mmodzi yemwe anavula zovala zake pogona. Aliyense anasunga chida chake chankhondo pambali pake.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

尼希米記 4:1-23

尼希米戰勝阻力

1參巴拉聽說我們正在重建城牆,非常憤怒,就嘲笑猶太人, 2當著他的同僚和撒瑪利亞軍兵的面說:「這群弱小的猶太人在做什麼呢?要重建城牆嗎?要獻祭嗎?要在一日之間建好嗎?要用廢墟中燒過的石頭來建造嗎?」

3他身旁的多比雅說:「他們建的石牆,一隻狐狸上去就能踩倒!」

4我禱告說:「我們的上帝啊,求你垂聽,因為我們正在被人恥笑。求你使他們對我們的凌辱歸到他們自己頭上,使他們被擄到外邦。 5不要遮掩他們的惡行,也不要從你面前塗抹他們的罪惡,因為他們在這些建造的人面前惹你發怒。」

6眾人全心做工,把整個城牆連接起來,高達原來的一半。

7參巴拉多比雅阿拉伯人、亞捫人和亞實突人聽說耶路撒冷的城牆正在重建、缺口正在填補,非常憤怒, 8便一起圖謀襲擊耶路撒冷,使城內混亂。 9但我們向我們的上帝禱告,並設立守衛晝夜防備他們。

10猶大人說:「工人已經精疲力盡,還有太多瓦礫有待清理,我們自己無法重建城牆。」 11我們的敵人說:「我們要趁他們不知不覺,進入他們中間殺死他們,阻止他們的工作。」 12靠近敵人居住的猶太人十次來告訴我們,說敵人會從各方來襲擊我們4·12 本節希伯來文意義不明。13於是,我按宗族派人手持刀劍、長矛和弓箭守衛在城牆後面低窪的空地上。 14我察看形勢後,起來對貴族、官員和其他民眾說:「不要怕他們!要記住,主偉大而可畏。要為你們的兄弟、兒女、妻子和家園而戰。」

15敵人聽說我們知道了他們的陰謀,上帝已破壞他們的詭計,就沒有來。我們回到城牆那裡,繼續各人的工作。 16從那時起,我的僕人一半繼續修築城牆,一半身穿盔甲,手持長矛、盾牌和弓箭負責守衛。官長都站在修築城牆的所有猶大人後面。 17搬運工人一手工作,一手拿兵器。 18修築城牆的人工作的時候都腰間配劍。吹號的人在我旁邊, 19我對貴族、官員和其餘的民眾說:「這工程浩大,範圍廣闊,我們在城牆上相隔很遠, 20因此你們一聽見號角聲,就要聚到我那裡。我們的上帝必為我們爭戰!」

21這樣,從黎明直到星星出現,我們的人一半工作,一半手持兵器守衛。 22那時,我又吩咐眾人各帶僕人在耶路撒冷住宿。他們夜間可以幫我們守衛,白天幫我們工作。 23我和我的兄弟、僕人及跟從我的守衛都衣不解帶,刀不離身4·23 刀不離身」或譯「出去打水時也帶著刀」。