Nehemiya 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 3:1-32

Anthu Omanga Makoma a Yerusalemu

1Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli. 2Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.

3Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake. 4Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china. 5Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.

6Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake. 7Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate. 8Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka. 9Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo. 10Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye. 11Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo. 12Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.

13Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.

14Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.

15Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide. 16Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.

17Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake. 18Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila. 19Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya. 20Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe. 21Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.

22Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china. 23Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo. 24Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya. 25Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi, 26ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija. 27Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.

28Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake. 29Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma. 30Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake. 31Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya. 32Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.

New Russian Translation

Неемия 3:1-32

Строители стены

1Первосвященник Элиашив и его собратья священники принялись отстраивать Овечьи ворота. Они освятили их и установили на место двери их; они освятили их до башни Сотни и от нее до башни Хананела. 2Соседний участок строили жители Иерихона, а рядом с ними строил Заккур, сын Имрия.

3Рыбные ворота были отстроены сыновьями Сенаи. Они положили их балки и установили их двери, замки и засовы. 4Меремоф, сын Урии, сына Гаккоца, восстановил следующий участок. Рядом с ним восстанавливал Мешуллам, сын Берехии, сына Мешезавела, а возле него – Цадок, сын Бааны. 5Следующий участок стены был восстановлен жителями Текоа, но их знать не подставила плечи под работу для своего Владыки3:5 Или: «своих господ»; или: «своего господина»..

6Старые ворота были восстановлены Иоиадой, сыном Пасеаха, и Мешулламом, сыном Бесодии. Они положили их балки и поставили на место их двери, замки и засовы. 7Рядом с ними восстанавливали жители Гаваона и Мицпы – гаваонитянин Мелатия и меронофянин Иадон – подвластные наместнику провинции за Евфратом. 8Уззиил, сын Харгаии, из ювелиров, восстановил следующий участок стены, а рядом с ним – Ханания, из составителей благовоний. Они восстановили Иерусалим до самой Широкой стены. 9Рефая, сын Хура, правитель половины Иерусалимского округа, восстановил следующий участок. 10Рядом с ними и напротив своего дома восстанавливал Иедаия, сын Харумафа, а возле него – Хаттуш, сын Хашавнии. 11Малхия, сын Харима, и Хашшув, сын Пахат-Моава, восстановили следующий участок и Печную башню. 12Шаллум, сын Аллохеша, правитель второй половины Иерусалимского округа, с помощью своих дочерей восстановил следующий участок.

13Ворота Долины были восстановлены Хануном и жителями Заноаха. Они отстроили их и установили на место их двери, замки и засовы. Еще они восстановили тысячу локтей3:13 Около 500 м. стены до самых Навозных ворот.

14Навозные ворота были восстановлены Малхией, сыном Рехава, правителем округа Бет-Карем. Он отстроил их и установил их двери, замки и засовы.

15Ворота Источника были восстановлены Шаллуном, сыном Колхозея, правителем округа Мицпа. Он отстроил их, соорудил над ними крышу и установил их двери, замки и засовы. Еще он восстановил стену у пруда Силоам3:15 Евр.: «Шелах», вариант названия «Шилоах». См. Ин. 9:7., у Царского сада, до самых ступеней, что спускаются из Города Давида3:15 Город Давида – старая часть города Иерусалима на горе Сион, где находилась крепость и царский дворец (см. 2 Цар. 5:7-9). Также в 12:37.. 16За ним – до места напротив гробниц Давида, и далее до выкопанного пруда и дома воинов – восстанавливал Неемия, сын Азбука, правитель половины округа Бет-Цур.

17За ним восстанавливали левиты под руководством Рехума, сына Бани. Рядом с ним стену восстанавливал Хашавия, правитель половины округа Кеила, за свой округ. 18Возле него восстанавливали их земляки под руководством Биннуя, сына Хенадада, правителя второй половины округа Кеила. 19Рядом с которым следующий участок – от места напротив подъема к оружейному складу до самого угла – восстановил Эзер, сын Иисуса, правитель Мицпы. 20Возле него следующий участок – от угла до входа в дом первосвященника Элиашива – ревностно восстановил Барух, сын Заббая. 21Рядом с ним следующий участок – от входа в дом Элиашива до конца дома – восстановил Меремоф, сын Урии, сына Гаккоца.

22За ним восстанавливали священники из окрестностей. 23За ними, напротив своего дома, восстанавливали Вениамин и Хашшув, а за ними, рядом со своим домом, восстанавливал Азария, сын Маасеи, сына Анании. 24Рядом с ним следующий участок – от дома Азарии до угла и поворота – восстановил Биннуй, сын Хенадада, 25а Фалал, сын Узая, трудился напротив угла и башни, выступающей из верхнего царского дворца, рядом со двором стражи. Возле него Педая, сын Пароша, 26и храмовые слуги, живущие на холме Офел, восстанавливали до места напротив Водных ворот к востоку и выступающей башни. 27Рядом с ними следующий участок – от большой выступающей башни до стены Офела – восстановили жители Текоа.

28За Конскими воротами восстанавливали священники – каждый напротив своего дома. 29За ними – напротив своего дома – восстанавливал Цадок, сын Иммера, а за ним – Шемая, сын Шекании, сторож Восточных ворот. 30За ним следующий участок восстанавливали Ханания, сын Шелемии, и Ханун, шестой сын Цалафа. За ними, напротив своего жилища, восстанавливал Мешуллам, сын Берехии. 31За ним – до самого дома храмовых слуг и купцов, что напротив Смотровых3:31 Евр.: «Гаммифкад». ворот, и до самой комнаты над углом – восстанавливал Малхия, из ювелиров. 32А между комнатой над углом и Овечьими воротами восстанавливали ювелиры и купцы.