Nehemiya 3 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 3:1-32

Anthu Omanga Makoma a Yerusalemu

1Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli. 2Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.

3Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake. 4Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china. 5Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.

6Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake. 7Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate. 8Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka. 9Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo. 10Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye. 11Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo. 12Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.

13Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.

14Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.

15Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide. 16Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.

17Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake. 18Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila. 19Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya. 20Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe. 21Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.

22Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china. 23Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo. 24Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya. 25Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi, 26ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija. 27Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.

28Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake. 29Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma. 30Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake. 31Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya. 32Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.

La Bible du Semeur

Néhémie 3:1-38

L’organisation des travaux

1Eliashib, le grand-prêtre, se mit au travail avec ses collègues, les prêtres, et ils se chargèrent de la reconstruction de la porte des Brebis. Ils la consacrèrent et en posèrent les battants, puis ils continuèrent à réparer la muraille, qu’ils consacrèrent, jusqu’à la tour de Méa, puis jusqu’à la tour de Hananéel.

2A côté d’eux travaillaient les habitants de Jéricho. A leur suite, c’était Zakkour, fils d’Imri, qui bâtissait. 3Les descendants de Senaa reconstruisirent la porte des Poissons3.3 Vers le nord-ouest.. Ils en firent la charpente et en posèrent les battants, les verrous et les barres. 4A côté d’eux, Merémoth, fils d’Urie, petit-fils d’Haqqots, travaillait ; à sa suite, c’était Meshoullam, fils de Bérékia, fils de Meshézabéel ; et plus loin, Tsadoq, fils de Baana. 5Venaient ensuite les habitants de Teqoa, mais leurs notables refusèrent de travailler sous les ordres des maîtres d’œuvre. 6Yoyada, fils de Paséah, et Meshoullam, fils de Besodia, réparèrent la Vieille Porte. Ils en firent la charpente et posèrent les battants, les verrous et les barres.

7A côté d’eux travaillaient Melatia, le Gabaonite, Yadôn, le Méronothite, et les gens de Gabaon et de Mitspa qui relevaient de la juridiction du gouverneur de la province à l’ouest de l’Euphrate. 8A côté d’eux travaillait l’orfèvre Ouzziel, fils de Harhaya, et à côté de lui, Hanania le parfumeur. Ils restaurèrent Jérusalem jusqu’à l’endroit où la muraille s’élargit. 9A côté d’eux travaillait Rephaya, fils de Hour, chef de la moitié du district de Jérusalem. 10A côté d’eux, Yedaya, fils de Haroumaph, travaillait à la section située en face de sa maison. A sa suite venait Hattoush, fils de Hashabnia. 11Un second secteur de la muraille ainsi que la tour des Fours furent réparés par Malkiya, fils de Harim, et par Hashoub, fils de Pahath-Moab.

12A côté d’eux travaillait Shalloum, fils de Hallohesh, chef de l’autre moitié du district de Jérusalem, assisté de ses filles. 13Hanoun et les habitants de Zanoah3.13 Située à une trentaine de kilomètres au sud-est de Jérusalem. réparèrent la porte de la Vallée. Ils la reconstruisirent et en posèrent les battants, les verrous et les barres. De plus, ils restaurèrent la muraille sur cinq cents mètres jusqu’à la porte du Fumier. 14C’est Malkiya, fils de Rékab, chef du district de Beth-Hakkérem, qui répara la porte du Fumier. Il la rebâtit et en posa les battants, les verrous et les barres. 15Shalloun, fils de Kol-Hozé, chef du district de Mitspa, répara la porte de la Source3.15 Voir 2.14 et note.. Après l’avoir reconstruite, il la couvrit d’un toit et fixa les battants, les verrous et les barres. De plus, il releva la muraille de l’Etang de l’aqueduc, près du jardin du roi, jusqu’aux marches qui descendent de la Cité de David.

16Au-delà, Néhémie, fils d’Azbouq, chef de la moitié du district de Beth-Tsour3.16 A quelques kilomètres au nord d’Hébron., travaillait dans le secteur qui s’étendait jusqu’en face du cimetière de David et allait jusqu’au réservoir artificiel et jusqu’à la caserne3.16 L’ancienne caserne des gardes du corps de David (2 S 23.8-39).. 17Au-delà travaillaient des lévites : Rehoum, fils de Bani, puis, à côté de lui, Hashabia, chef de la moitié du district de Qeïla. 18Au-delà travaillait leur collègue Bavvaï, fils de Hénadad, chef de l’autre moitié du district de Qeïla, 19et, à sa suite, Ezer, fils de Josué, chef de Mitspa, réparait un second secteur, situé en face de la montée de l’arsenal, à l’endroit où la muraille fait saillie.

20Au-delà, Baruch, fils de Zabbaï, réparait avec ardeur une autre section depuis l’angle jusqu’à l’entrée de la maison d’Eliashib, le grand-prêtre. 21Au-delà, Merémoth, fils d’Urie et petit-fils d’Haqqots, réparait un autre secteur, depuis l’entrée de la maison d’Eliashib jusqu’à son extrémité. 22Au-delà travaillaient les prêtres qui habitaient les plaines environnantes. 23Au-delà, Benjamin et Hashoub réparaient la muraille en face de leurs maisons. A côté d’eux, Azaria, fils de Maaséya et petit-fils d’Anania, travaillait à côté de sa maison. 24Au-delà, Binnouï, fils de Hénadad, renforçait un autre secteur allant de la maison d’Azaria jusqu’à l’angle en saillie de la muraille.

25Puis c’était Palal, fils d’Ouzaï, qui travaillait devant la saillie et la tour supérieure qui domine le palais royal et touche à la cour de la prison, et au-delà, Pedaya, fils de Pareosh. 26Les desservants du Temple s’étaient établis sur la colline de l’Ophel3.26 Colline de Jérusalem (voir 11.21 ; 2 Ch 27.3). Le nom s’appliquait surtout au côté nord de la colline qui se trouvait au sud-est de la ville, celle qui constituait autrefois la Cité de David, au sud du Temple. jusqu’en face de la porte des Eaux à l’est, et de la tour en saillie. 27Les gens de Teqoa travaillaient à la section suivante, depuis la grande tour en saillie jusqu’à la muraille de la colline de l’Ophel. 28A partir de la porte des Chevaux, les prêtres travaillaient chacun en face de sa maison. 29Au-delà, Tsadoq, fils d’Immer, réparait devant sa maison et ensuite Shemaya, fils de Shekania, gardien de la porte de l’Orient3.29 Peut-être l’actuelle porte Dorée., 30Hanania, fils de Shélémia, et Hanoun, le sixième fils de Tsalaph, réparèrent le secteur suivant, et au-delà, Meshoullam, fils de Bérékia, travaillait en face de sa demeure.

31Puis Malkiya, de la corporation des orfèvres, travaillait jusqu’aux maisons des desservants du Temple et des marchands, vis-à-vis de la porte de la Surveillance et jusqu’au poste de guet situé en haut de l’angle de la muraille. 32Les orfèvres et les marchands réparèrent la muraille entre ce poste de l’angle et la porte des Brebis.

Le mépris de Sanballat et Tobiya

33Lorsque Sanballat apprit que nous rebâtissions la muraille, il fut très mécontent et se mit violemment en colère. Il se moqua des Juifs 34en disant devant ses compatriotes et devant l’armée de Samarie : Qu’est-ce que ces minables Juifs veulent donc faire ? S’imagineraient-ils qu’on va les laisser agir et qu’en offrant des sacrifices à leur Dieu ils viendront maintenant à bout d’une telle entreprise ? Redonneront-ils vie à des pierres ensevelies sous des monceaux de poussière et calcinées ?

35Tobiya, l’Ammonite, qui se tenait à ses côtés ajouta : Ils n’ont qu’à bâtir ! Si un renard s’élance contre leur muraille de pierre, il la brisera.

36Ecoute, ô notre Dieu, comme on nous méprise ! Fais retomber sur eux l’humiliation qu’ils nous infligent et livre-les au pillage sur une terre d’exil. 37Ne pardonne pas leur faute et n’efface pas leur péché, car ils ont offensé ceux qui rebâtissent les remparts.

38Cependant, nous avons continué à bâtir la muraille et, sur tout le pourtour, elle fut réparée jusqu’à mi-hauteur, car chacun avait pris ce travail à cœur.