Nehemiya 11 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 11:1-36

Nzika Zatsopano za mu Yerusalemu

1Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo. 2Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.

3Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu. 4Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini.

Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa:

Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi. 5Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni. 6Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.

7Nazi zidzukulu za Benjamini:

Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya. 8Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928. 9Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.

10Ansembe anali awa:

Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini; 11Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu, 12ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya, 13ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri 14ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.

15Alevi anali awa:

Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni. 16Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu. 17Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni. 18Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.

19Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa:

Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.

20Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.

21Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.

22Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu. 23Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.

24Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.

25Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake, 26ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti, 27Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo. 28Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo, 29ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti, 30Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.

31Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake, 32ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya, 33ku Hazori, Rama ndi Gitaimu, 34ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati, 35ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.

36Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.

King James Version

Nehemiah 11:1-36

1And the rulers of the people dwelt at Jerusalem: the rest of the people also cast lots, to bring one of ten to dwell in Jerusalem the holy city, and nine parts to dwell in other cities. 2And the people blessed all the men, that willingly offered themselves to dwell at Jerusalem.

3¶ Now these are the chief of the province that dwelt in Jerusalem: but in the cities of Judah dwelt every one in his possession in their cities, to wit, Israel, the priests, and the Levites, and the Nethinims, and the children of Solomon’s servants. 4And at Jerusalem dwelt certain of the children of Judah, and of the children of Benjamin. Of the children of Judah; Athaiah the son of Uzziah, the son of Zechariah, the son of Amariah, the son of Shephatiah, the son of Mahalaleel, of the children of Perez;11.4 Perez: also called, Pharez 5And Maaseiah the son of Baruch, the son of Col-hozeh, the son of Hazaiah, the son of Adaiah, the son of Joiarib, the son of Zechariah, the son of Shiloni. 6All the sons of Perez that dwelt at Jerusalem were four hundred threescore and eight valiant men. 7And these are the sons of Benjamin; Sallu the son of Meshullam, the son of Joed, the son of Pedaiah, the son of Kolaiah, the son of Maaseiah, the son of Ithiel, the son of Jesaiah. 8And after him Gabbai, Sallai, nine hundred twenty and eight. 9And Joel the son of Zichri was their overseer: and Judah the son of Senuah was second over the city. 10Of the priests: Jedaiah the son of Joiarib, Jachin. 11Seraiah the son of Hilkiah, the son of Meshullam, the son of Zadok, the son of Meraioth, the son of Ahitub, was the ruler of the house of God. 12And their brethren that did the work of the house were eight hundred twenty and two: and Adaiah the son of Jeroham, the son of Pelaliah, the son of Amzi, the son of Zechariah, the son of Pashur, the son of Malchiah, 13And his brethren, chief of the fathers, two hundred forty and two: and Amashai the son of Azareel, the son of Ahasai, the son of Meshillemoth, the son of Immer, 14And their brethren, mighty men of valour, an hundred twenty and eight: and their overseer was Zabdiel, the son of one of the great men.11.14 the son…: or, the son of Haggedolim 15Also of the Levites: Shemaiah the son of Hashub, the son of Azrikam, the son of Hashabiah, the son of Bunni; 16And Shabbethai and Jozabad, of the chief of the Levites, had the oversight of the outward business of the house of God.11.16 had…: Heb. were over 17And Mattaniah the son of Micha, the son of Zabdi, the son of Asaph, was the principal to begin the thanksgiving in prayer: and Bakbukiah the second among his brethren, and Abda the son of Shammua, the son of Galal, the son of Jeduthun. 18All the Levites in the holy city were two hundred fourscore and four. 19Moreover the porters, Akkub, Talmon, and their brethren that kept the gates, were an hundred seventy and two.11.19 the gates: Heb. at the gates

20¶ And the residue of Israel, of the priests, and the Levites, were in all the cities of Judah, every one in his inheritance. 21But the Nethinims dwelt in Ophel: and Ziha and Gispa were over the Nethinims.11.21 Ophel: or, the tower 22The overseer also of the Levites at Jerusalem was Uzzi the son of Bani, the son of Hashabiah, the son of Mattaniah, the son of Micha. Of the sons of Asaph, the singers were over the business of the house of God. 23For it was the king’s commandment concerning them, that a certain portion should be for the singers, due for every day.11.23 a certain…: or, a sure ordinance 24And Pethahiah the son of Meshezabeel, of the children of Zerah the son of Judah, was at the king’s hand in all matters concerning the people.11.24 Zerah: also called, Zarah 25And for the villages, with their fields, some of the children of Judah dwelt at Kirjath-arba, and in the villages thereof, and at Dibon, and in the villages thereof, and at Jekabzeel, and in the villages thereof, 26And at Jeshua, and at Moladah, and at Beth-phelet, 27And at Hazar-shual, and at Beer-sheba, and in the villages thereof, 28And at Ziklag, and at Mekonah, and in the villages thereof, 29And at En-rimmon, and at Zareah, and at Jarmuth, 30Zanoah, Adullam, and in their villages, at Lachish, and the fields thereof, at Azekah, and in the villages thereof. And they dwelt from Beer-sheba unto the valley of Hinnom. 31The children also of Benjamin from Geba dwelt at Michmash, and Aija, and Beth-el, and in their villages,11.31 from: or, of11.31 at: or, to 32And at Anathoth, Nob, Ananiah, 33Hazor, Ramah, Gittaim, 34Hadid, Zeboim, Neballat, 35Lod, and Ono, the valley of craftsmen. 36And of the Levites were divisions in Judah, and in Benjamin.