Nehemiya 11 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 11:1-36

Nzika Zatsopano za mu Yerusalemu

1Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo. 2Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.

3Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu. 4Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini.

Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa:

Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi. 5Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni. 6Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.

7Nazi zidzukulu za Benjamini:

Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya. 8Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928. 9Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.

10Ansembe anali awa:

Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini; 11Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu, 12ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya, 13ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri 14ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.

15Alevi anali awa:

Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni. 16Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu. 17Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni. 18Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.

19Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa:

Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.

20Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.

21Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.

22Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu. 23Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.

24Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.

25Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake, 26ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti, 27Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo. 28Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo, 29ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti, 30Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.

31Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake, 32ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya, 33ku Hazori, Rama ndi Gitaimu, 34ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati, 35ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.

36Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.

La Bible du Semeur

Néhémie 11:1-36

Le repeuplement de Jérusalem et l’organisation de la ville

1Les chefs du peuple s’installèrent à Jérusalem. Pour le reste du peuple, on tira au sort pour faire venir s’établir à Jérusalem, la ville sainte, une famille sur dix. Les neuf autres pouvaient rester dans les autres localités. 2Certains hommes s’offrirent volontairement pour habiter à Jérusalem. Leurs compatriotes les bénirent. 3Dans les villes de Juda habitaient les Israélites, les prêtres, les lévites, les desservants du Temple et les descendants des serviteurs de Salomon, chacun dans sa propriété et sa ville respective. Et voici la liste des chefs de la province qui se fixèrent à Jérusalem. 4De plus, des gens des tribus de Juda et de Benjamin s’établirent à Jérusalem : De la tribu de Juda : Ataya, fils d’Ozias, ayant pour descendants : Zacharie, Amaria, Shephatia, Mahalaléel, de la lignée de Pérets, 5et Maaséya, fils de Baruch, dont les ascendants étaient Kol-Hozé, Hazaya, Adaya, Yoyarib, Zacharie et Shiloni. 6Les descendants de Pérets qui s’établirent à Jérusalem furent en tout 468 hommes d’âge adulte.

7Membres de la tribu de Benjamin : Sallou, fils de Meshoullam, qui avait pour ascendants : Yoëd, Pedaya, Kolaya, Maaséya, Itiel et Esaïe. 8Il y avait en outre Gabbaï et Sallaï. Cela fait en tout 928 hommes. 9Joël, fils de Zikri, était leur responsable ; et Juda, fils de Hassenoua, était l’adjoint de la ville.

10Parmi les prêtres : Yedaeya, fils de Yoyarib, Yakîn, 11Seraya, fils de Hilqiya, qui avait pour ascendants Meshoullam, Tsadoq, Merayoth et Ahitoub, responsable en chef du temple de Dieu. 12822 membres de son lignage étaient occupés au service du Temple. Il y avait aussi Adaya, fils de Yeroham, qui avait pour ascendants Pelalia, Amtsi, Zacharie, Pashhour et Malkiya, 13ainsi que 242 chefs de groupes familiaux de sa lignée. Il y avait Amashsaï, fils d’Azaréel, dont les ascendants étaient Ahzaï, Meshillémoth, Immer. 14Avec les autres hommes valeureux de sa lignée, ils étaient au nombre de 128. Zabdiel, fils de Guedolim, en était le chef. 15Parmi les lévites, Shemaya, fils de Hashoub, descendant d’Azriqam, d’Hashabia et de Bounni, 16Shabthaï et Yozabad, qui faisaient partie des chefs des lévites, étaient chargés des travaux extérieurs du Temple. 17Mattania, fils de Michée, descendant de Zabdi, descendant d’Asaph, qui était responsable d’entonner la louange lors de la prière, Baqbouqia, le second parmi ses frères, et Abda, fils de Shammoua, descendant de Galal et Yedoutoun. 18284 lévites habitaient la ville sainte. 19Il y avait encore 172 portiers, chargés de surveiller les portes : Aqqoub et Talmôn, et les membres de leur groupe familial. 20Le reste des Israélites, des prêtres et des lévites étaient établis dans toutes les villes de Juda, chacun dans son patrimoine. 21Les desservants du Temple habitaient le quartier de l’Ophel11.21 Voir 3.26 et note.. Tsiha et Guishpa étaient leurs chefs.

22Le responsable des lévites à Jérusalem était Ouzzi, fils de Bani, qui avait pour ascendants Hashabia, Mattania et Michée, descendants d’Asaph. Les descendants d’Asaph étaient les musiciens chargés du service musical dans le Temple. 23Ils étaient soumis à des ordonnances royales qui réglaient leur activité jour par jour.

24Petahya, fils de Meshézabéel, de la lignée de Zérah, fils de Juda, était le délégué du roi pour toutes les affaires civiles.

Les localités repeuplées par des Judéens

25D’autres membres de la tribu de Juda s’établirent dans les localités de la campagne à Qiryath-Arba11.25 C’est-à-dire Hébron (voir Gn 23.2 ; Jos 15.54). et les villages qui en dépendent, à Dibôn et les villages qui en dépendent, à Yeqabtséel et les localités qui en dépendent, 26à Yéshoua, à Molada, à Beth-Paleth ; 27à Hatsar-Shoual, à Beer-Sheva et les villages qui en dépendent, 28à Tsiqlag, à Mekona et les villages qui en dépendent, 29à Eyn-Rimmôn, à Tsorea, à Yarmouth, 30à Zanoah, à Adoullam et les localités qui en dépendent, à Lakish et les fermes des environs, à Azéqa et les villages qui en dépendent. Ils occupèrent ainsi toute la région depuis Beer-Sheva jusqu’à la vallée de Hinnom.

31Les membres de la tribu de Benjamin occupèrent Guéba, Mikmas, Aya, Béthel et les villages qui en dépendent, 32Anatoth, Nob, Anania, 33Hatsor, Rama, Guittaïm, 34Hadid, Tseboïm, Neballath, 35Lod et Ono, la vallée des Artisans.

36Certains groupes de lévites de Juda allèrent s’installer parmi les Benjaminites.