Nehemiya 1 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 1:1-11

Pemphero la Nehemiya

1Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya:

Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa, 2Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.

3Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”

4Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba. 5Ndinkati:

“Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu. 6Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani. 7Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.

8“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina. 9Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’

10“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu. 11Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.”

Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

Священное Писание

Неемия 1:1-11

Молитва Неемии об Иерусалиме

1Слова Неемии, сына Ахалии:

В месяце кислеве, в двадцатом году правления царя Артаксеркса1:1 Артаксеркс I Лонгиман (Долгорукий) правил Персидской империей с 464 по 424 гг. до н. э. (поздней осенью 446 г. до н. э.), когда я находился в крепости города Сузы, 2Ханани – один из моих братьев – пришёл из Иудеи с некоторыми другими людьми, и я расспросил их об уцелевших жителях Иудеи, которые вернулись из плена, и об Иерусалиме.

3Они сказали мне:

– Те, кто прошёл через плен и вернулся в провинцию Иудея, сейчас в большой беде и бесчестии. Стена Иерусалима разрушена, а его ворота сожжены.

4Услышав это, я сел и заплакал. Несколько дней я скорбел, постился и молился пред Богом небесным. 5Я говорил:

– О Вечный1:5 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь., Бог небес, Бог великий и грозный, верный соглашению любви с теми, кто любит Тебя и слушается Твоих повелений, 6да будут уши Твои внимательны и глаза Твои открыты, чтобы услышать молитву Твоего раба, которой я молюсь пред Тобой день и ночь за Твоих рабов, народ Исраила. Я признаюсь в грехах, которыми мы, исраильтяне, включая меня и дом моего отца, согрешили против Тебя. 7Мы поступали пред Тобой нечестиво. Мы не слушались повелений, установлений и законов, которые Ты дал Своему рабу Мусе.

8Вспомни повеление, которое Ты дал Своему рабу Мусе, сказав: «Если вы нарушите верность, Я рассею вас среди народов, 9но если вы вернётесь ко Мне и станете слушаться Моих повелений, то даже если ваши изгнанники будут находиться на краю земли, Я соберу вас оттуда и приведу на место, которое Я избрал, чтобы Мне там поклонялись»1:8-9 См. Лев. 26:27-28, 33; Втор. 28:64; 30:1-5..

10Они – Твои рабы и Твой народ, который Ты искупил Своей великой силой и могучей рукой. 11О Владыка, да будут уши Твои внимательны к моей молитве и к молитве других Твоих рабов, которые любят чтить Твоё имя. Дай сегодня Твоему рабу успех, даровав ему расположение царя.

Я был виночерпием1:11 Виночерпий был одним из самых важных лиц при дворе, которому царь доверял свою жизнь. царя.