Nahumu 3 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 3:1-19

Tsoka la Ninive

1Tsoka kwa mzinda wopha anthu,

mzinda wodzaza ndi mabodza,

mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo,

mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!

2Kulira kwa zikwapu,

mkokomo wa mikombero,

kufuwula kwa akavalo

ndiponso phokoso la magaleta!

3Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo,

kungʼanima kwa malupanga

ndi kunyezimira kwa mikondo!

Anthu ambiri ophedwa,

milumilu ya anthu akufa,

mitembo yosawerengeka,

anthu akupunthwa pa mitemboyo.

4Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere,

wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga,

amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake,

ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.

5Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ine ndikutsutsana nawe.

Ndidzakuvula chovala chako.

Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako

ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.

6Ndidzakuthira zonyansa,

ndidzakuchititsa manyazi

ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.

7Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati,

‘Ninive wasanduka bwinja,

adzamulira ndani?’

Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”

8Kodi ndiwe wopambana Tebesi,

mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo,

wozunguliridwa ndi madzi?

Mtsinjewo unali chitetezo chake,

madziwo anali linga lake.

9Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto,

Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.

10Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa

ndipo anapita ku ukapolo.

Ana ake anawaphwanyitsa pansi

mʼmisewu yonse ya mu mzindamo.

Anachita maere ogawana anthu ake otchuka,

ndipo anthu ake onse amphamvu

anamangidwa ndi maunyolo.

11Iwenso Ninive udzaledzera;

udzabisala

ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.

12Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu

yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha;

pamene agwedeza mitengoyo,

nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.

13Tayangʼana ankhondo ako,

onse ali ngati akazi!

Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako;

moto wapsereza mipiringidzo yake.

14Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu,

limbitsani chitetezo chanu!

Pondani dothi,

ikani mʼchikombole,

konzani khoma la njerwa!

15Kumeneko moto udzakupserezani;

lupanga lidzakukanthani

ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala.

Chulukanani ngati ziwala,

chulukanani ngati dzombe!

16Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu

mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga,

koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko

ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.

17Akalonga ako ali ngati dzombe,

akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe

limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira,

koma pamene dzuwa latuluka limawuluka,

ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.

18Iwe mfumu ya ku Asiriya,

abusa ako agona tulo;

anthu ako olemekezeka amwalira.

Anthu ako amwazikira ku mapiri

popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.

19Palibe chimene chingachize bala lako;

chilonda chako sichingapole.

Aliyense amene amamva za iwe

amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako,

kodi alipo amene sanazilawepo

nkhanza zako zosatha?

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

那鸿书 3:1-19

尼尼微的灾祸

1充满血腥的尼尼微有祸了!

城中充满诡诈和暴力,

害人的事从未止息。

2鞭声啪啪,车轮隆隆,

战马奔腾,战车疾驰,

3骑士冲锋,刀光闪闪,矛枪生辉;

被杀者众多,尸骨成堆,

人们被遍地的尸体绊倒。

4这全是因为尼尼微像妖媚的妓女大肆淫乱,

惯行邪术,

以淫行诱惑列国,

靠邪术欺骗各族。

5万军之耶和华说:

“我要与你为敌。

我要把你的衣裙掀到你脸上,

使列国看见你的裸体,

使列邦看见你的羞耻。

6我要把可憎之物抛在你身上,

侮辱你,

让众人观看。

7凡看见你的都要逃避,说,

尼尼微毁灭了!

谁会为她悲伤呢?’

我到哪里去寻找安慰你的人呢?”

8你能强过底比斯3:8 底比斯”希伯来文是“挪亚们”。吗?

底比斯位于尼罗河上,

四面环水,

水是她的屏障,

又是她的城墙。

9古实埃及是她无穷的力量,

人和利比亚人是她的帮手。

10可是,她却被掳到远方,

她的婴孩被摔死在各个街头。

她的官长被抽签瓜分,

她所有的首领都被锁链锁着。

11尼尼微啊,

你也必像醉汉一样,

你必寻找藏身之处躲避敌人。

12你所有的堡垒都像无花果树上的初熟果子,

一摇树,果子就掉进吃的人口中。

13看啊,

你的军队就像柔弱的女人,

你境内的关口向敌人敞开,

你的门闩被火烧毁。

14你要蓄水以防围困,

要加强防御!

要走进土坑踩泥,

拿起砖模造砖!

15但在那里,火要吞噬你,

刀剑要杀戮你,

要像蝗虫吞没你。

你只管像蝗虫一样繁殖,

如蚱蜢一般增多吧!

16你的商贾多过天上的繁星,

但他们像吃光后飞去的蝗虫。

17你的臣仆像蝗虫,

你的将领像成群的蚱蜢。

它们寒日聚集在墙上,

太阳一出来就飞走了,

无人知道它们的行踪。

18亚述王啊!

你的牧人沉睡,贵族酣眠,

你的百姓分散在群山上,

无人招聚他们。

19你的创伤无法救治,

你的伤势极其严重。

听见这消息的人必鼓掌欢呼,

因为谁没受过你无休止的暴虐呢?