Kugwa kwa Ninive
1Wodzathira nkhondo akubwera
kudzalimbana nawe, Ninive.
Tetezani malinga anu,
dziyangʼanani ku msewu,
konzekerani nkhondo,
valani dzilimbe.
2Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo
ngati ulemerero wa Israeli,
ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu
ndipo anawononganso mpesa wawo.
3Zishango za ankhondo ake ndi zofiira;
asilikali ake avala zovala zofiirira.
Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira
tsiku la kukonzekera kwake.
Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
4Magaleta akuthamanga mʼmisewu
akungothamangathamanga pa mabwalo.
Akuoneka ngati miyuni yoyaka;
akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
5Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka,
koma iwo akubwera napunthwa.
Akuthamangira ku linga la mzinda;
akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
6Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje
ndipo nyumba yaufumu yagwa.
7Zatsimikizika kuti mzinda
utengedwa ndi kupita ku ukapolo.
Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda
ndipo akudziguguda pachifuwa.
8Ninive ali ngati dziwe,
ndipo madzi ake akutayika.
Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!”
Koma palibe amene akubwerera.
9Funkhani siliva!
Funkhani golide!
Katundu wake ndi wochuluka kwambiri,
chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa!
Mitima yasweka, mawondo akuwombana,
anthu akunjenjemera ndipo
nkhope zasandulika ndi mantha.
11Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti,
malo amene mikango inkadyetserako ana ake,
kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako,
ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake
ndiponso kuphera nyama mkango waukazi,
kudzaza phanga lake ndi zimene wapha
ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
13Yehova Wamphamvuzonse akuti,
“Ine ndikutsutsana nawe.
Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo,
ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono;
sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi.
Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
La destrucción de Nínive
1Nínive, un destructor avanza contra ti.
Monta guardia en la fortaleza;
vigila el camino;
renueva tus fuerzas;
refuerza tu poder.
2Porque el Señor restaura el esplendor de Jacob,
como el esplendor de Israel,
aunque los destructores lo han arrasado;
han arruinado sus viñas.
3Rojo es el escudo de sus valientes;
de escarlata se visten los guerreros.
El metal de sus carros brilla como fuego
mientras se alistan para la batalla
y los guerreros agitan sus lanzas.2:3 Según el texto hebreo; la LXX y la Siríaca dicen batalla y se inquietan los jinetes.
4Por las calles se precipitan los carros,
irrumpen con violencia por las plazas.
Su aspecto es como antorchas de fuego,
como relámpagos zigzagueantes.
Caída y saqueo de Nínive
5Nínive convoca a sus tropas escogidas,
que en su carrera se atropellan.
Corren a la muralla
para preparar la protección,
6pero se abren las compuertas de los ríos
y el palacio se derrumba.
7Está decidido:
la ciudad2:7 ciudad. Alt. reina. está desnuda y es llevada al exilio.
Gimen sus criadas como palomas
y se golpean el pecho.
8Nínive es como un estanque roto
cuyas aguas se derraman.
«¡Deténganse! ¡Deténganse!», les gritan,
pero nadie vuelve atrás.
9¡Saqueen la plata!
¡Saqueen el oro!
El tesoro es inagotable,
y abundan las riquezas y los objetos preciosos.
10¡Destrucción, ruina, devastación!
Desfallecen los corazones,
tiemblan las rodillas,
se estremecen los cuerpos,
palidecen los rostros.
La bestia salvaje morirá
11¿Qué fue de la guarida de los leones
y de la cueva donde alimentaban a los leoncillos,
donde el león, la leona y sus cachorros
se guarecían sin que nadie los perturbara?
12¿Qué fue del león,
que despedazaba para sus crías
y estrangulaba para sus leonas,
que llenaba de presas su caverna
y de carne su guarida?
13«Pero ahora yo vengo contra ti»,
afirma el Señor de los Ejércitos.
«Convertiré en humo tus carros de guerra
y mataré a filo de espada a tus leoncillos.
Pondré fin en el país a tus rapiñas
y no volverá a oírse la voz de tus mensajeros».