Nahumu 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 1:1-15

1Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

Mkwiyo wa Yehova pa Ninive

2Yehova ndi Mulungu wansanje

ndiponso wobwezera;

Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.

Yehova amabwezera adani ake

ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.

3Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;

ndipo sadzalola kuti munthu

wolakwa asalangidwe.

Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,

ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.

4Amalamulira nyanja ndipo imawuma;

amawumitsa mitsinje yonse.

Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma

ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.

5Mapiri amagwedera pamaso pake

ndipo zitunda zimasungunuka.

Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,

dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.

6Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?

Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?

Ukali wake ukuyaka ngati moto;

matanthwe akunyeka pamaso pake.

7Yehova ndi wabwino,

ndiye kothawirako nthawi ya masautso.

Amasamalira amene amamudalira,

8koma ndi madzi achigumula choopsa

Iye adzawononga adani ake (Ninive);

adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.

9Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova

adzachiwononga kotheratu;

msautso sudzabweranso kachiwiri.

10Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga

ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;

adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.

11Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,

wofuna kuchitira Yehova chiwembu,

amene amapereka uphungu woyipa.

12Yehova akuti,

“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,

kaya iwowo ndi ambiri,

koma adzawonongedwa ndi kutheratu.

Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,

sindidzakuzunzanso.

13Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako

ndipo ndidzadula maunyolo ako.”

14Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,

“Sudzakhala ndi zidzukulu

zimene zidzadziwike ndi dzina lako.

Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba

amene ali mʼnyumba ya milungu yako.

Ine ndidzakukumbira manda

chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”

15Taonani, pa phiripo,

mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,

amene akulengeza za mtendere!

Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu

ndipo kwaniritsani malumbiro anu.

Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;

iwo adzawonongedwa kotheratu.

New Serbian Translation

Књига пророка Наума 1:1-15

1Пророштво о Ниниви. Књига виђења Наума из Елкоша.

Господњи гнев против Ниниве

2Бог је љубоморан и освећује се Господ.

Он је Господ освете и господар гнева.

Господ се свети својим душманима

и гаји гнев према својим непријатељима.

3Господ се споро гневи, велике је силе,

али кривца нипошто не оставља некажњена.

У олујном ветру, у вихору пут је његов

и облак му је прашина под ногама.

4Кад море прекори, он га исушује

и све реке чини сувим.

Вену Васан и Кармил,

вене цват Ливана.

5Због њега се горе тресу,

а брегови растачу.

Земља се пред њим подиже

и сав свет и сви који на њему живе.

6Ко да стоји пред гневом његовим?

Ко да издржи пламен срдње његове?

Јер гнев се његов излио као лава

и стене се пред њим дробе.

7Господ је добар,

заштита је у дану невоље

и познаје оне што у њему уточиште траже.

8Он ће силном поплавом

да докрајчи Ниниву,

а своје ће душмане у мрак да одагна.

9Шта год да сплеткарите против Господа,

он ће то да докрајчи.

Невоља се неће подигнути двапут.

10Нека су и као трње сплетени

и као пијани од свог пића,

прогутани биће сасвим ко стрњика сува.

11Од тебе ће доћи онај

који сплеткари зло против Господа,

опаки саветник.

12Овако каже Господ:

„Иако су Асирци и сложни и иако бројни,

и такви биће сасечени и изгажени.

А ја сам те тлачио, народе мој,

али те више тлачити нећу.

13Ево, сада ћу да скршим његов јарам на теби,

изломићу твоје окове.“

14Господ је заповедио против тебе:

„Твоје име неће имати потомке.

Из куће твојих богова

срушићу кипове и ливене идоле.

Гроб ти спремам

јер си безвредан.“

15Ево, на горама су ноге благовесника

који мир објављује!

Прослављај, Јудо, празнике своје!

Испуни своје завете

јер те више неће газити опаки.

Сатрће се сасвим.