1Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
Mkwiyo wa Yehova pa Ninive
2Yehova ndi Mulungu wansanje
ndiponso wobwezera;
Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.
Yehova amabwezera adani ake
ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
3Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;
ndipo sadzalola kuti munthu
wolakwa asalangidwe.
Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,
ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
4Amalamulira nyanja ndipo imawuma;
amawumitsa mitsinje yonse.
Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma
ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
5Mapiri amagwedera pamaso pake
ndipo zitunda zimasungunuka.
Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,
dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
6Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?
Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?
Ukali wake ukuyaka ngati moto;
matanthwe akunyeka pamaso pake.
7Yehova ndi wabwino,
ndiye kothawirako nthawi ya masautso.
Amasamalira amene amamudalira,
8koma ndi madzi achigumula choopsa
Iye adzawononga adani ake (Ninive);
adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
9Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova
adzachiwononga kotheratu;
msautso sudzabweranso kachiwiri.
10Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga
ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;
adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
11Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,
wofuna kuchitira Yehova chiwembu,
amene amapereka uphungu woyipa.
12Yehova akuti,
“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,
kaya iwowo ndi ambiri,
koma adzawonongedwa ndi kutheratu.
Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,
sindidzakuzunzanso.
13Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako
ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
14Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,
“Sudzakhala ndi zidzukulu
zimene zidzadziwike ndi dzina lako.
Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba
amene ali mʼnyumba ya milungu yako.
Ine ndidzakukumbira manda
chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
15Taonani, pa phiripo,
mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,
amene akulengeza za mtendere!
Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu
ndipo kwaniritsani malumbiro anu.
Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;
iwo adzawonongedwa kotheratu.
1A prophecy concerning Nineveh. The book of the vision of Nahum the Elkoshite.
The Lord’s anger against Nineveh
2The Lord is a jealous and avenging God;
the Lord takes vengeance and is filled with wrath.
The Lord takes vengeance on his foes
and vents his wrath against his enemies.
3The Lord is slow to anger but great in power;
the Lord will not leave the guilty unpunished.
His way is in the whirlwind and the storm,
and clouds are the dust of his feet.
4He rebukes the sea and dries it up;
he makes all the rivers run dry.
Bashan and Carmel wither
and the blossoms of Lebanon fade.
5The mountains quake before him
and the hills melt away.
The earth trembles at his presence,
the world and all who live in it.
6Who can withstand his indignation?
Who can endure his fierce anger?
His wrath is poured out like fire;
the rocks are shattered before him.
7The Lord is good,
a refuge in times of trouble.
He cares for those who trust in him,
8but with an overwhelming flood
he will make an end of Nineveh;
he will pursue his foes into the realm of darkness.
9Whatever they plot against the Lord
he will bring1:9 Or What do you foes plot against the Lord? / He will bring it to an end;
trouble will not come a second time.
10They will be entangled among thorns
and drunk from their wine;
they will be consumed like dry stubble.1:10 The meaning of the Hebrew for this verse is uncertain.
11From you, Nineveh, has one come forth
who plots evil against the Lord
and devises wicked plans.
12This is what the Lord says:
‘Although they have allies and are numerous,
they will be destroyed and pass away.
Although I have afflicted you, Judah,
I will afflict you no more.
13Now I will break their yoke from your neck
and tear your shackles away.’
14The Lord has given a command concerning you, Nineveh:
‘You will have no descendants to bear your name.
I will destroy the images and idols
that are in the temple of your gods.
I will prepare your grave,
for you are vile.’
15Look, there on the mountains,
the feet of one who brings good news,
who proclaims peace!
Celebrate your festivals, Judah,
and fulfil your vows.
No more will the wicked invade you;
they will be completely destroyed.1:15 In Hebrew texts this verse (1:15) is numbered 2:1.