Nahumu 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 1:1-15

1Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

Mkwiyo wa Yehova pa Ninive

2Yehova ndi Mulungu wansanje

ndiponso wobwezera;

Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.

Yehova amabwezera adani ake

ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.

3Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;

ndipo sadzalola kuti munthu

wolakwa asalangidwe.

Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,

ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.

4Amalamulira nyanja ndipo imawuma;

amawumitsa mitsinje yonse.

Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma

ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.

5Mapiri amagwedera pamaso pake

ndipo zitunda zimasungunuka.

Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,

dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.

6Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?

Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?

Ukali wake ukuyaka ngati moto;

matanthwe akunyeka pamaso pake.

7Yehova ndi wabwino,

ndiye kothawirako nthawi ya masautso.

Amasamalira amene amamudalira,

8koma ndi madzi achigumula choopsa

Iye adzawononga adani ake (Ninive);

adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.

9Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova

adzachiwononga kotheratu;

msautso sudzabweranso kachiwiri.

10Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga

ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;

adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.

11Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,

wofuna kuchitira Yehova chiwembu,

amene amapereka uphungu woyipa.

12Yehova akuti,

“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,

kaya iwowo ndi ambiri,

koma adzawonongedwa ndi kutheratu.

Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,

sindidzakuzunzanso.

13Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako

ndipo ndidzadula maunyolo ako.”

14Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,

“Sudzakhala ndi zidzukulu

zimene zidzadziwike ndi dzina lako.

Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba

amene ali mʼnyumba ya milungu yako.

Ine ndidzakukumbira manda

chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”

15Taonani, pa phiripo,

mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,

amene akulengeza za mtendere!

Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu

ndipo kwaniritsani malumbiro anu.

Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;

iwo adzawonongedwa kotheratu.

New International Reader’s Version

Nahum 1:1-15

1Here is a prophecy the Lord gave Nahum, who was from the town of Elkosh. The prophecy came in a vision and is written in a book. The prophecy is about Nineveh.

The Lord Is Angry With Nineveh

2The Lord is a jealous God who punishes people.

He pays them back for the evil things they do.

He directs his anger against them.

The Lord punishes his enemies.

He holds his anger back

until the right time to use it.

3The Lord is slow to get angry.

But he is very powerful.

The Lord will not let guilty people go

without punishing them.

When he marches out, he stirs up winds and storms.

Clouds are the dust kicked up by his feet.

4He controls the seas. He dries them up.

He makes all the rivers run dry.

Bashan and Mount Carmel dry up.

The flowers in Lebanon fade.

5He causes the mountains to shake.

The hills melt away.

The earth trembles because he is there.

The world and all those who live in it also tremble.

6Who can stand firm when his anger burns?

Who can live when he is angry?

His anger blazes out like fire.

He smashes the rocks to pieces.

7The Lord is good.

When people are in trouble,

they can go to him for safety.

He takes good care of those

who trust in him.

8But he will destroy Nineveh

with a powerful flood.

He will chase his enemies

into the place of darkness.

9The Lord will put an end

to anything they plan against him.

He won’t allow Assyria to win the battle

over his people a second time.

10His enemies will be tangled up among thorns.

Their wine will make them drunk.

They’ll be burned up like dry straw.

11Nineveh, a king has marched out from you.

He makes evil plans against the Lord.

He thinks about how he can do what is wrong.

12The Lord says,

“His army has many soldiers.

Other nations are helping them.

But they will be destroyed and pass away.

Judah, I punished you.

But I will not do it anymore.

13Now I will break Assyria’s yoke off your neck.

I will tear off the ropes that hold you.”

14Nineveh, the Lord has given an order concerning you.

He has said, “You will not have any children

to carry on your name.

I will destroy the wooden and metal statues

that are in the temple of your gods.

I will get your grave ready for you.

You are worthless.”

15Look at the mountains of Judah!

I see a messenger running to bring good news!

He’s telling us that peace has come!

People of Judah, celebrate your feasts.

Carry out your promises.

The evil Assyrians won’t attack you again.

They’ll be completely destroyed.