Nahumu 1 – CCL & NASV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 1:1-15

1Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

Mkwiyo wa Yehova pa Ninive

2Yehova ndi Mulungu wansanje

ndiponso wobwezera;

Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.

Yehova amabwezera adani ake

ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.

3Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;

ndipo sadzalola kuti munthu

wolakwa asalangidwe.

Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,

ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.

4Amalamulira nyanja ndipo imawuma;

amawumitsa mitsinje yonse.

Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma

ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.

5Mapiri amagwedera pamaso pake

ndipo zitunda zimasungunuka.

Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,

dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.

6Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?

Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?

Ukali wake ukuyaka ngati moto;

matanthwe akunyeka pamaso pake.

7Yehova ndi wabwino,

ndiye kothawirako nthawi ya masautso.

Amasamalira amene amamudalira,

8koma ndi madzi achigumula choopsa

Iye adzawononga adani ake (Ninive);

adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.

9Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova

adzachiwononga kotheratu;

msautso sudzabweranso kachiwiri.

10Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga

ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;

adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.

11Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,

wofuna kuchitira Yehova chiwembu,

amene amapereka uphungu woyipa.

12Yehova akuti,

“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,

kaya iwowo ndi ambiri,

koma adzawonongedwa ndi kutheratu.

Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,

sindidzakuzunzanso.

13Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako

ndipo ndidzadula maunyolo ako.”

14Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,

“Sudzakhala ndi zidzukulu

zimene zidzadziwike ndi dzina lako.

Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba

amene ali mʼnyumba ya milungu yako.

Ine ndidzakukumbira manda

chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”

15Taonani, pa phiripo,

mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,

amene akulengeza za mtendere!

Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu

ndipo kwaniritsani malumbiro anu.

Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;

iwo adzawonongedwa kotheratu.

New Amharic Standard Version

ናሆም 1:1-15

1ስለ ነነዌ ጥፋት የተነገረ ንግር፤ የኤልቆሻዊው የናሆም የራእዩ መጽሐፍ ይህ ነው፤

በነነዌ ላይ የተገለጠ የእግዚአብሔር ቍጣ

2እግዚአብሔር ቀናተኛና ተበቃይ አምላክ ነው፤

እግዚአብሔር የሚበቀል፣ በመዓትም የተሞላ ነው።

እግዚአብሔር ባላጋራዎቹን ይበቀላል፤

በጠላቶቹም ላይ ቍጣውን ያመጣል።

3እግዚአብሔር ለቍጣ የዘገየ፣ በኀይሉም ታላቅ ነው፤

እግዚአብሔር በደለኛውን ሳይቀጣ አያልፍም፤

መንገዱ በዐውሎ ነፋስና በማዕበል ውስጥ ነው፤

ደመናም የእግሩ ትቢያ ነው።

4ባሕርን ይገሥጻል፤ ያደርቀዋልም፤

ወንዞችን ሁሉ ያደርቃል።

ባሳንና ቀርሜሎስ ጠውልገዋል፤

የሊባኖስም አበቦች ረግፈዋል።

5ተራሮች በፊቱ ታወኩ፤

ኰረብቶችም ቀለጡ።

ምድር በፊቱ፣

ዓለምና በውስጧ የሚኖሩት ሁሉ ተናወጡ።

6ቍጣውን ማን ሊቋቋም ይችላል?

ጽኑ ቍጣውንስ ማን ሊሸከም ይችላል?

መዓቱ እንደ እሳት ፈስሷል፤

ዐለቶችም በፊቱ ተሰነጣጥቀዋል።

7እግዚአብሔር መልካም ነው፤

በጭንቅ ጊዜም መሸሸጊያ ነው።

ለሚታመኑበት ይጠነቀቅላቸዋል፤

8ነነዌን ግን፣

በሚያጥለቀልቅ ጐርፍ ያጠፋታል፤

ጠላቶቹንም ወደ ጨለማ ያሳድዳቸዋል።

9በእግዚአብሔር ላይ ምንም ቢያሤሩ1፥9 በእግዚአብሔር ላይ የምታሤሩት ምንድን ነው? የሚሉ አሉ።

እርሱ ያጠፋዋል፤

መከራም ዳግመኛ አይነሣም።

10በእሾኽ ይጠላለፋሉ፤

በወይን ጠጃቸውም ይሰክራሉ፤

እሳትም እንደ ገለባ1፥10 የዕብራይስጡ ትርጕም በትክክል አይታወቅም። ይበላቸዋል።

11ነነዌ ሆይ፤ በእግዚአብሔር ላይ የሚያሤር፣

ክፋትንም የሚመክር፣

ከአንቺ ዘንድ ወጥቷል።

12እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“ምንም ኀይለኞችና ብዙዎች ቢሆኑም፣

ይቈረጣሉ፤ ይጠፋሉም።

ይሁዳ ሆይ፤ ከዚህ በፊት ባስጨንቅህም፣

ከእንግዲህ አላስጨንቅህም።

13አሁንም ቀንበራቸውን ከዐንገትህ ላይ አንሥቼ እሰብራለሁ፤

የታሰርህበትንም ሰንሰለት በጥሼ እጥላለሁ።”

14አንቺ ነነዌ፤ እግዚአብሔር ስለ አንቺ እንዲህ ብሎ አዝዟል፤

“ስም የሚያስጠራ ትውልድ አይኖራችሁም፤

በአማልክታችሁ ቤት ያሉትን፣

የተቀረጹትን ምስሎችና ቀልጠው የተሠሩትን ጣዖታት እደመስሳለሁ፤

መቀበሪያህን እምስልሃለሁ፤

አንተ ክፉ ነህና።”

15እነሆ፤ የምሥራች የሚያመጣው፣

ሰላምን የሚያውጀው ሰው እግር፣

በተራሮች ላይ ነው፤

ይሁዳ ሆይ፤ በዓላትህን አክብር፤

ስእለትህንም ፈጽም፤

ከእንግዲህ ክፉዎች አይወርሩህም፤

እነርሱም ፈጽመው ይጠፋሉ።