Nahumu 1 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 1:1-15

1Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

Mkwiyo wa Yehova pa Ninive

2Yehova ndi Mulungu wansanje

ndiponso wobwezera;

Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.

Yehova amabwezera adani ake

ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.

3Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;

ndipo sadzalola kuti munthu

wolakwa asalangidwe.

Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,

ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.

4Amalamulira nyanja ndipo imawuma;

amawumitsa mitsinje yonse.

Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma

ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.

5Mapiri amagwedera pamaso pake

ndipo zitunda zimasungunuka.

Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,

dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.

6Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?

Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?

Ukali wake ukuyaka ngati moto;

matanthwe akunyeka pamaso pake.

7Yehova ndi wabwino,

ndiye kothawirako nthawi ya masautso.

Amasamalira amene amamudalira,

8koma ndi madzi achigumula choopsa

Iye adzawononga adani ake (Ninive);

adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.

9Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova

adzachiwononga kotheratu;

msautso sudzabweranso kachiwiri.

10Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga

ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;

adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.

11Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,

wofuna kuchitira Yehova chiwembu,

amene amapereka uphungu woyipa.

12Yehova akuti,

“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,

kaya iwowo ndi ambiri,

koma adzawonongedwa ndi kutheratu.

Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,

sindidzakuzunzanso.

13Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako

ndipo ndidzadula maunyolo ako.”

14Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,

“Sudzakhala ndi zidzukulu

zimene zidzadziwike ndi dzina lako.

Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba

amene ali mʼnyumba ya milungu yako.

Ine ndidzakukumbira manda

chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”

15Taonani, pa phiripo,

mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,

amene akulengeza za mtendere!

Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu

ndipo kwaniritsani malumbiro anu.

Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;

iwo adzawonongedwa kotheratu.

Hoffnung für Alle

Nahum 1:1-14

Eine Botschaft für die assyrische Hauptstadt Ninive

(Kapitel 1–3)

Gott zieht seine Feinde zur Rechenschaft

1In diesem Buch ist aufgeschrieben, was Gott der Stadt Ninive ankündigte. Die folgende Botschaft wurde Nahum aus dem Dorf Elkosch offenbart:

2Der Herr ist ein leidenschaftlicher Gott, der keinen neben sich duldet. Voller Zorn rächt er sich an seinen Feinden. Seine Widersacher zieht er zur Rechenschaft; ja, alle, die ihn hassen, bekommen seinen Zorn zu spüren.

3Der Herr ist geduldig, aber er besitzt auch große Macht und lässt niemanden ungestraft davonkommen.

Wenn er daherschreitet, brechen Stürme und Unwetter los, die mächtigen Wolken sind nur der Staub, den seine Füße aufwirbeln.

4Wenn er das Meer bedroht, trocknet es aus, ganze Flüsse lässt er versiegen. Die saftigen Weiden von Baschan welken dahin, die Bäume auf dem Karmel werden dürr, und der Libanon mit seinem Blütenmeer liegt da wie eine trostlose Wüste.

5Die Berge und Hügel wanken, wenn der Herr erscheint, die Erde bebt, und alle ihre Bewohner zittern vor Angst.

6Wer könnte ihm die Stirn bieten, wenn sein Zorn losbricht wie ein verheerendes Feuer? Mit seiner Glut bringt er sogar Felsen zum Bersten!

7Und doch ist der Herr voller Güte. Er kennt alle, die ihm vertrauen, und ist für sie eine sichere Zuflucht in Zeiten der Not.

8Aber die Stadt seiner Feinde zerstört er, wie eine reißende Flut schwemmt er sie fort. Ja, Finsternis wird alle verschlingen, die ihn verachten!

9Was schmiedet ihr noch Pläne gegen den Herrn? Er wird euch mit einem einzigen Schlag vernichten – ein zweites Mal könnt ihr euch nicht gegen ihn auflehnen!1,9 Oder: Was denkt ihr (Israeliten) denn über den Herrn? Er wird die Feinde mit einem einzigen Schlag vernichten – ein zweites Mal können sie sich nicht gegen ihn auflehnen!

10Ihr seid nichts als unnützes Dornengestrüpp, das ins Feuer geworfen wird und lichterloh brennt wie dürres Stroh!1,10 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text ist nicht sicher zu deuten. 11Aus dir, Ninive, kam ein Herrscher, der finstere Pläne gegen den Herrn schmiedete und nur Unheil ausbrütete.

12Doch jetzt spricht der Herr zu Jerusalem: »Wenn deine Feinde wieder anrücken und all ihre Truppen aufbieten, sollen sie niedergemäht werden wie die Halme auf einem Feld. Ich habe dich hart bestraft, doch nun ist es genug damit. 13Ich will das schwere Joch, das auf dir lastet, zerbrechen und deine Fesseln zerreißen!«

14Zum assyrischen König aber sagt der Herr:1,14 Wörtlich: Über dich aber hat der Herr geboten. »Für mich bist du schon so gut wie tot; ich habe dir das Grab geschaufelt. Du wirst keine Nachkommen mehr haben, und aus deinem Tempel werfe ich sämtliche Götzenstatuen hinaus.«