Mlaliki 9 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 9:1-18

Mathero a Zinthu Zonse ndi Wofanana

1Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani. 2Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe.

Zomwe zimachitikira munthu wabwino,

zimachitikiranso munthu wochimwa,

zomwe zimachitikira amene amalumbira,

zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.

3Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa. 4Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!

5Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa,

koma akufa sadziwa kanthu;

alibe mphotho ina yowonjezera,

ndipo palibe amene amawakumbukira.

6Chikondi chawo, chidani chawo

ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale;

sadzakhalanso ndi gawo

pa zonse zochitika pansi pano.

7Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako. 8Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse. 9Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano. 10Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru.

11Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano:

opambana pa kuthamanga si aliwiro,

kapena opambana pa nkhondo si amphamvu,

ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru,

kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri,

kapena okomeredwa mtima si ophunzira;

koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.

12Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti:

monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde,

kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha,

chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa,

pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.

Nzeru Iposa Uchitsiru

13Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri: 14Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo. 15Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo. 16Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.

17Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri

kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.

18Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo,

koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.

O Livro

Eclesiastes 9:1-18

O destino de todos

1Também isto cuidadosamente tomei em consideração, que os justos e os sábios estão dependentes da vontade de Deus. Os homens não sabem sequer se virão a conhecer o amor ou o ódio. Não podem prever coisa nenhuma. 2Acontece o mesmo a toda a gente, tanto ao justo como ao ímpio, ao bom e ao mau, ao puro e ao impuro, ao que consagra sacrifícios e louvores e àquele que não os oferece. O que acontece com o homem bom, ocorre também com o pecador, e o que faz juramentos passa pelas mesmas circunstâncias que aquele que evita jurar.

3Essa é a razão por que os homens não procuram ser bons e escolhem os seus maus caminhos; porque na vida não lhes resta senão, como esperança, a morte. 4A esperança é apenas para os vivos. Um cão vivo vale mais que um leão morto!

5Os vivos, esses sabem, pelo menos, que hão de morrer! Os mortos não sabem nada, nem sequer têm memória. 6Tudo o que fizeram, os seus amores, ódios, invejas, tudo se foi com eles e já não têm participação, de espécie alguma, naquilo que se passa aqui na Terra. 7Por isso, come e bebe com alegria, porque Deus já se agradou do que fazes! 8Veste sempre roupa de festa e nunca deixes de ungir a tua cabeça com óleo! 9Vive feliz com a mulher que amas, cada dia da breve existência que Deus te concede aqui no mundo. Esse é o quinhão com que Deus te recompensa pelo que passas aqui em baixo. 10Tudo o que fizeres, fá-lo bem, porque no mundo dos mortos9.10 Sheol. Segundo o pensamento hebraico do Antigo Testamento, é o lugar dos mortos, mas não necessariamente como um sepulcro ou sepultura, que é um lugar de morte e definhamento, mas sim um lugar de existência consciente, embora sombria e infeliz., para onde acabarás por ir, não há realizações, nem planos para fazer, nem coisas para compreender e analisar.

11Voltei-me de novo para o que se passa sobre a face da Terra e vi que os que correm mais rápido não são sempre os que ganham as corridas, nem são os mais fortes que ganham sempre as batalhas. Também vi que os homens mais sábios são frequentemente pobres e que os mais capazes não são necessariamente famosos; o tempo e a sorte sobrevêm a todos.

12O ser humano nunca é capaz de prever quando sobrevirão tempos maus. Como o peixe capturado na rede ou o pássaro apanhado na armadilha, assim vê a desgraça cair-lhe em cima, repentinamente.

A sabedoria é melhor que a tolice

13Há ainda outra coisa que me impressionou bastante, enquanto observava os assuntos dos homens. 14Havia uma pequena localidade, apenas com alguns habitantes. Veio um poderoso rei atacá-la com o seu exército e sitiá-la com grandes engenhos bélicos. 15Vivia ali um homem sábio, muito pobre, que sabia como salvar aquela povoação, mas ninguém se preocupou em ir ter com ele. 16Então dei-me conta de que, apesar da sabedoria ser melhor do que a força, se uma pessoa sábia for pobre será desprezada, e aquilo que ela disser não será tido em consideração. 17Mesmo assim, vale mais escutar as palavras sábias de um homem sensato, falando calmamente, do que os gritos dum rei de tolos. 18A sabedoria tem mais valor do que um arsenal de guerra, mas um só erro é capaz de destruir os bens que ela concede.