Mlaliki 9 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 9:1-18

Mathero a Zinthu Zonse ndi Wofanana

1Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani. 2Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe.

Zomwe zimachitikira munthu wabwino,

zimachitikiranso munthu wochimwa,

zomwe zimachitikira amene amalumbira,

zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.

3Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa. 4Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!

5Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa,

koma akufa sadziwa kanthu;

alibe mphotho ina yowonjezera,

ndipo palibe amene amawakumbukira.

6Chikondi chawo, chidani chawo

ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale;

sadzakhalanso ndi gawo

pa zonse zochitika pansi pano.

7Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako. 8Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse. 9Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano. 10Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru.

11Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano:

opambana pa kuthamanga si aliwiro,

kapena opambana pa nkhondo si amphamvu,

ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru,

kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri,

kapena okomeredwa mtima si ophunzira;

koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.

12Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti:

monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde,

kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha,

chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa,

pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.

Nzeru Iposa Uchitsiru

13Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri: 14Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo. 15Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo. 16Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.

17Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri

kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.

18Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo,

koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.

Het Boek

Prediker 9:1-18

Ieder deelt in hetzelfde lot

1Ook dit onderzocht ik grondig: het feit dat gelovige en wijze mensen afhankelijk zijn van Gods wil, niemand weet of hij liefde of haat zal ontmoeten. Men weet niets van tevoren. 2Iedereen krijgt te maken met dezelfde ervaringen, of hij nu goed of slecht, godsdienstig of niet godsdienstig, werelds of gelovig is. 3Ieder deelt in hetzelfde lot en dat lijkt onrechtvaardig. Daarom doen de mensen slechte en dwaze dingen en kiezen zij hun eigen onverstandige weg, want het ontbreekt hun aan hoop, het enige dat de toekomst hun brengt, is de dood. 4Er bestaat alleen hoop voor de levenden. U kunt beter een levende hond dan een dode leeuw zijn! 5Want de levenden weten tenminste dat zij op zekere dag zullen sterven. Maar de doden weten van niets, zij hebben geen loon meer te verwachten. Er wordt niet meer aan hen gedacht. 6Wat zij tijdens hun leven deden—liefhebben, haten, benijden—is allang vergeten en zij hebben niets meer van doen met wat hier op aarde gebeurt.

7Ga daarom maar gewoon door met eten en drinken en wees er blij mee, want zo heeft God het altijd al gewild. 8Draag feestkleren en zorg dat u er goed verzorgd uitziet. 9Geniet van een gelukkig leven met de vrouw van wie u houdt gedurende de dagen van uw voorbijglijdende leven, want dat komt u toe in dit leven, bij alle moeite die u zich op aarde getroost. 10Benut alle mogelijkheden die je krijgt om iets te doen, want in de dood waar u naar toe gaat, bestaat geen werk, geen voorbereiding, geen weten en geen begrijpen.

11Opnieuw keek ik over de aarde en ik zag dat de snelste man niet altijd de wedstrijd wint, dat de sterkste niet altijd als overwinnaar uit de strijd komt, dat wijze mensen vaak arm zijn en mensen met grote vaardigheden niet als vanzelfsprekend beroemd zijn. Alles komt neer op geluk, op het juiste moment op de juiste plaats zijn. 12Een mens weet nooit wanneer hem iets zal overkomen. Hij is als een vis die in het net wordt gevangen en als een vogel die in een strik komt vast te zitten.

13Bij het observeren van het menselijke maakte ook het volgende een diepe indruk op mij: 14een klein stadje met slechts enkele inwoners werd belegerd door een koning met zijn leger. 15In dat stadje woonde een wijze, arme man, die wist wat er moest gebeuren om de stad te redden, maar niemand dacht eraan hem om raad te vragen. 16Toen besefte ik dat men de arme wijze veracht en niet naar hem luistert, ook al is wijsheid beter dan kracht. 17Maar toch zijn de rustige woorden van een wijze man beter dan de kreten van een koning van dwazen. 18Wijsheid is beter dan oorlogstuig, maar één dwaas bederft veel goeds.