Mlaliki 8 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 8:1-17

1Ndani angafanane ndi munthu wanzeru?

Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu?

Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu

ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.

Za Kumvera Mfumu

2Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu. 3Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho. 4Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”

5Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse,

ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.

6Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse,

ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.

7Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo,

ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?

8Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga,

choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake.

Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa,

kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.

9Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza. 10Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.

11Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa. 12Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu. 13Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.

14Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino. 15Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.

16Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku, 17pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.

New Russian Translation

Екклесиаст 8:1-17

1Кто подобен мудрецу?

Кто понимает значение вещей?

Мудрость просвещает лицо человека

и смягчает его суровый вид.

Повинуйся царю

2Я говорю: повинуйся повелению царя, потому что ты поклялся перед Богом. 3Не спеши покинуть царя и не отстаивай худого дела, потому что он может сделать все, что ему угодно. 4Слово царя властно, кто может сказать ему: «Что ты делаешь?»

5Кто повинуется его повелениям, не попадет в беду,

мудрое сердце знает нужное время и правильное поведение,

6потому что у всякого дела есть свое время и свой устав,

но несчастья человека тяжким бременем лежат на нем.

7Человек не знает будущего,

и кто может сказать ему что будет?

8Человек не властен удержать ветер8:8 Или: «дух».,

также как он не властен и над днем своей смерти.

Воин не может получить увольнение во время битвы,

и нечестивый не спасется своим нечестием.

Одна участь всему

9Все это увидел я, когда решил постичь разумом все, что делается под солнцем. Иногда человек властвует над другим ему во вред8:9 Или: «себе самому во вред».. 10Еще я видел, что хоронили нечестивых, которые когда-то приходили в храм, но позже они были забыты в том городе, где творили зло. Это тоже суета.

11Когда не скоро выносят приговор за преступление, сердца людей исполняются желанием совершать зло. 12Хотя грешник сто раз совершает грех и долго живет, все же я знаю, что будет лучше тем, кто боится Бога и благоговеет перед Ним. 13А грешнику не будет процветания, и дни его, подобно тени, не продлятся долго, потому что он не боится Бога.

14Есть еще нечто суетное, что случается на земле: праведник получает то, что заслуживает нечестивый, а нечестивый получает то, что заслуживает праведник. И сказал я, что это тоже суета. 15Итак, я воздаю хвалу веселью, потому что нет ничего лучше для человека под солнцем, как есть, пить и веселиться. И радость будет сопровождать его в трудах во все дни его жизни, которые Бог дал ему под солнцем.

16Когда я решил познать мудрость и понаблюдать за трудом человека на земле – его глаза не видят сна ни днем ни ночью, – 17тогда я увидел все, что сделал Бог. Человек не может постичь того, что происходит под солнцем. Как бы человек ни старался постичь этого, он не сможет найти смысла. Даже если какой-нибудь мудрец скажет, что он-то знает, на самом деле он не постиг этого.