Mlaliki 7 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 7:1-29

Nzeru

1Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino,

ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.

2Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro

kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero:

Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense;

anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.

3Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka,

pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.

4Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa,

koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.

5Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru

kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.

6Kuseka kwa zitsiru kuli ngati

kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika,

izinso ndi zopandapake.

7Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru,

ndipo chiphuphu chimawononga mtima.

8Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake,

ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.

9Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako,

pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.

10Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?”

pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.

11Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino

ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.

12Nzeru ndi chitetezo,

monganso ndalama zili chitetezo,

koma phindu la chidziwitso ndi ili:

kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.

13Taganizirani zimene Mulungu wazichita:

ndani angathe kuwongola chinthu

chimene Iye anachipanga chokhota?

14Pamene zinthu zili bwino, sangalala;

koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino:

Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo,

ndiponso nthawi imene si yabwinoyo.

Choncho munthu sangathe kuzindikira

chilichonse cha mʼtsogolo mwake.

15Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi:

munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake,

ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.

16Usakhale wolungama kwambiri

kapena wanzeru kwambiri,

udziwonongerenji wekha?

17Usakhale woyipa kwambiri,

ndipo usakhale chitsiru,

uferenji nthawi yako isanakwane?

18Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi,

ndipo usataye njira inayo.

Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.

19Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru

kupambana olamulira khumi a mu mzinda.

20Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi

amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.

21Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula,

mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,

22pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako

kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.

23Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati,

“Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,”

koma nzeruyo inanditalikira.

24Nzeru zimene zilipo,

zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri,

ndani angathe kuzidziwa?

25Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe,

ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira

ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru

ndiponso kupusa kwake kwa misala.

26Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa,

mkazi amene ali ngati khoka,

amene mtima wake uli ngati khwekhwe,

ndipo manja ake ali ngati maunyolo.

Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo,

koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.

27Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi:

“Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,

28pamene ine ndinali kufufuzabe

koma osapeza kanthu,

ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000,

koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.

29Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi:

Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama,

koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”

Thai New Contemporary Bible

ปัญญาจารย์ 7:1-29

สติปัญญา

1ชื่อเสียงดีมีค่ายิ่งกว่าน้ำหอมราคาแพง

และวันตายก็ดีกว่าวันเกิด

2ไปบ้านที่มีการไว้ทุกข์

ก็ดีกว่าไปบ้านที่มีงานเลี้ยง

เพราะความตายเป็นจุดหมายปลายทางของทุกคน

ผู้ที่ยังมีชีวิตอยู่ควรใส่ใจในข้อนี้

3โศกเศร้าดีกว่าหัวเราะ

เพราะใบหน้าโศกเศร้านั้นเป็นผลดีต่อจิตใจ

4ใจแบบคนฉลาดพบได้ในบ้านที่มีความโศกเศร้า

แต่ใจแบบคนโง่พบได้ในบ้านที่มีความรื่นเริง

5ฟังคำตำหนิของคนฉลาด

ดีกว่าฟังคนโง่ร้องเพลงสรรเสริญเยินยอ

6เสียงหัวเราะของคนโง่

ก็เหมือนเสียงแตกปะทุของหนามในไฟใต้หม้อ

นี่ก็อนิจจัง

7เมื่อคนฉลาดกดขี่ผู้อื่น

เขาก็ทำตัวเหมือนคนโง่

และเมื่อรับสินบน

ก็ทำให้ชีวิตเสื่อมทราม

8ตอนจบดีกว่าตอนเริ่ม

ความอดทนอดกลั้นดีกว่าความหยิ่งจองหอง

9อย่าปล่อยให้ใจของเจ้าโกรธเร็ว

เพราะความโกรธอยู่ในใจของคนโง่

10อย่าถามว่า “ทำไมสมัยก่อนดีกว่าเดี๋ยวนี้?”

เพราะนั่นไม่ใช่คำถามที่ฉลาดเลย

11สติปัญญาเป็นสิ่งดีเช่นเดียวกับมรดก

เป็นประโยชน์แก่ผู้ที่เห็นตะวัน

12สติปัญญาเป็นที่พักพิง

เช่นเดียวกับเงิน

แต่ข้อได้เปรียบของความรู้ก็คือ

สติปัญญาสงวนชีวิตของผู้มีปัญญาไว้

13จงพิเคราะห์ดูพระราชกิจของพระเจ้า

สิ่งที่พระองค์ทรงกระทำให้คด

ใครจะเหยียดให้ตรงได้?

14จงสุขใจในยามดี

แต่เมื่อถึงยามทุกข์ยากก็จงใคร่ครวญ

พระเจ้าทรงบันดาลทั้งยามดีและยามร้าย

มนุษย์จึงไม่สามารถรู้อะไรเลยเกี่ยวกับอนาคตของตน

15ในชีวิตอนิจจังนั้น ข้าพเจ้าเห็นทั้งสองสิ่งนี้มาแล้ว

คนชอบธรรมต้องพินาศทั้งๆ ที่ชอบธรรม

และคนชั่วร้ายอายุยืนทั้งๆ ที่ชั่วร้าย

16อย่าเป็นคนชอบธรรมเกินไป

และอย่าฉลาดเกินไป

จะทำลายตัวเองทำไม?

17อย่าชั่วร้ายเกินไป

และอย่าโง่เง่าเต่าตุ่น

เรื่องอะไรจะต้องตายก่อนกำหนด?

18เป็นการดีที่จะยึดสิ่งหนึ่งไว้

และไม่ปล่อยให้อีกสิ่งหลุดมือไป

ผู้ที่ยำเกรงพระเจ้าจะหลีกเลี่ยงเรื่องสุดโต่งทั้งหมดนี้ไปได้7:18 หรือติดตามทั้งสองสิ่งได้

19สติปัญญาทำให้คนฉลาดมีอำนาจ

มากยิ่งกว่าผู้ครอบครองสิบคนที่ครองเมือง

20ไม่มีสักคนเดียวในโลกนี้ที่ดีพร้อม

ที่ทำแต่สิ่งที่ถูกต้องและไม่เคยทำบาปเลย

21อย่าใส่ใจทุกถ้อยคำที่ใครๆ พูดกัน

มิฉะนั้นท่านอาจได้ยินคนใช้ของท่านเองแช่งด่าท่าน

22เพราะท่านก็รู้อยู่แก่ใจว่า

ตัวท่านเองแช่งด่าคนอื่นหลายครั้ง

23ทั้งหมดนี้ข้าพเจ้าทดสอบด้วยสติปัญญาแล้ว และข้าพเจ้ากล่าวว่า

“เราตั้งใจจะเป็นคนฉลาด”

แต่มันก็เกินไขว่คว้า

24สติปัญญาจะเป็นอะไรก็ตามแต่

มันช่างไกลลิบลับและลึกซึ้งนัก

ใครเล่าจะค้นพบได้?

25ข้าพเจ้าจึงมุ่งหาความเข้าใจ

พินิจพิเคราะห์และเสาะหาสติปัญญากับมูลเหตุของสิ่งต่างๆ

และพยายามเข้าใจความโง่เขลาของความชั่ว

และความบ้าบอของความโฉดเขลา

26ข้าพเจ้าพบว่าสิ่งที่ขมขื่นยิ่งกว่าความตาย

ก็คือผู้หญิงซึ่งเป็นกับดัก

ใจของนางเป็นบ่วงแร้ว

มือของนางคือโซ่ตรวน

ผู้ที่พระเจ้าโปรดปรานจะรอดพ้นจากนาง

แต่คนบาปต้องติดกับของนาง

27ปัญญาจารย์7:27 หรือผู้นำของชุมชนกล่าวว่า “ดูเถิด ข้าพเจ้าค้นพบสิ่งนี้คือ

“การนำเอาสิ่งหนึ่งมาปะติดปะต่อกับอีกสิ่งเพื่อหามูลเหตุ

28ขณะที่หาอยู่แต่ยังไม่พบ

ข้าพเจ้าก็พบว่าในพันคนจะมีผู้ชายซื่อตรงคนหนึ่ง

แต่ไม่มีผู้หญิงซื่อตรงสักคน

29ข้าพเจ้าพบแต่เพียงว่า

พระเจ้าทรงสร้างมนุษย์ให้ซื่อตรง

แต่มนุษย์สรรหากลอุบายต่างๆ นานา”