Mlaliki 7 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 7:1-29

Nzeru

1Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino,

ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.

2Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro

kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero:

Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense;

anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.

3Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka,

pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.

4Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa,

koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.

5Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru

kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.

6Kuseka kwa zitsiru kuli ngati

kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika,

izinso ndi zopandapake.

7Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru,

ndipo chiphuphu chimawononga mtima.

8Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake,

ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.

9Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako,

pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.

10Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?”

pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.

11Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino

ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.

12Nzeru ndi chitetezo,

monganso ndalama zili chitetezo,

koma phindu la chidziwitso ndi ili:

kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.

13Taganizirani zimene Mulungu wazichita:

ndani angathe kuwongola chinthu

chimene Iye anachipanga chokhota?

14Pamene zinthu zili bwino, sangalala;

koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino:

Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo,

ndiponso nthawi imene si yabwinoyo.

Choncho munthu sangathe kuzindikira

chilichonse cha mʼtsogolo mwake.

15Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi:

munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake,

ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.

16Usakhale wolungama kwambiri

kapena wanzeru kwambiri,

udziwonongerenji wekha?

17Usakhale woyipa kwambiri,

ndipo usakhale chitsiru,

uferenji nthawi yako isanakwane?

18Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi,

ndipo usataye njira inayo.

Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.

19Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru

kupambana olamulira khumi a mu mzinda.

20Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi

amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.

21Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula,

mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,

22pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako

kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.

23Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati,

“Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,”

koma nzeruyo inanditalikira.

24Nzeru zimene zilipo,

zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri,

ndani angathe kuzidziwa?

25Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe,

ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira

ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru

ndiponso kupusa kwake kwa misala.

26Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa,

mkazi amene ali ngati khoka,

amene mtima wake uli ngati khwekhwe,

ndipo manja ake ali ngati maunyolo.

Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo,

koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.

27Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi:

“Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,

28pamene ine ndinali kufufuzabe

koma osapeza kanthu,

ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000,

koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.

29Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi:

Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama,

koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”

Bibelen på hverdagsdansk

Prædikerens Bog 7:1-29

Tanker om livet

1Et godt ry er vigtigere end kostbar parfume, ligesom den dag, man dør, er vigtigere end den dag, man blev født. 2Det er vigtigere at gå til begravelse end at gå til fest, for døden indhenter os alle, og det bør man altid huske på. 3Sorg er vigtigere end latter, for det giver én noget at tænke over. 4Den kloge tænker over dødens alvor, mens tåben slår tiden ihjel med morskab.

5Det er bedre at lytte til en vismands kritik end til en tåbes ros. 6En tåbes latter er som tjørnekviste, der knitrer lystigt under gryden, men hurtigt brænder ud. Det er der intet formål med. 7Uhæderlighed gør den vise til en tåbe, bestikkelse gør sindet korrupt. 8At kunne føre en sag igennem til sin afslutning er vigtigere end at kunne begynde den, tålmodighed er bedre end stolthed. 9Lad dig ikke provokere til vrede, for det er tåbeligt at gå rundt og bære nag. 10Lad være at sukke efter „de gode, gamle dage”, for det afslører din mangel på visdom.

11Det er godt at få en arv, og det er godt at have visdom. 12Både visdom og rigdom giver sikkerhed i livet, men visdommen har dog et fortrin: Den er bedre til at holde et menneske i live.

13Tænk på, hvordan Gud handler. Hvem kan rette det ud, som han har gjort skævt? 14Glæd dig, når du oplever fremgang. Men når modgangen kommer, så husk på, at begge dele kommer fra Gud, og du kan aldrig vide, hvad fremtiden bringer.

15Jeg har set mange uretfærdige ting i mit liv. Jeg har set et godt menneske dø i en al for ung alder, og jeg har set et ondt menneske leve længe på trods af sin ondskab. 16Tro ikke, at Gud automatisk velsigner dig på grund af din store godhed eller visdom. Du kunne blive dybt skuffet. 17På den anden side er det farligt at være ond eller tåbelig. Du kunne risikere at dø i en ung alder. 18Lyt til begge advarsler, for et gudfrygtigt menneske vil følge begge råd.

19Ti officerer kan beskytte en by, men visdom giver endnu mere beskyttelse, 20for intet menneske er så godt, at det altid handler rigtigt og aldrig synder.

21Lyt ikke til alt, hvad der bliver sladret om, for du kunne risikere at høre din egen tjener kritisere dig, 22og du ved jo, hvor ofte du selv har kritiseret andre.

23Jeg tænkte dybt over alt, hvad jeg så, for jeg ville gerne forstå det hele, men det lykkedes dog ikke. 24Livets mening og dybe sammenhæng overgår min forstand. Intet menneske forstår det til bunds. 25Alligevel undersøgte jeg alle ting grundigt og stillede spørgsmål for gennem visdom at kunne forstå tingenes sammenhæng. Jeg var sikker på, at gudløshed er tåbeligt, og tåbelighed er vanvid.

26Jeg fandt også ud af noget andet: En forførende kvinde er dødsensfarlig. Hendes lidenskab er en fælde og hendes arme som lænker. Den, der lever ret for Gud, kan undslippe fælden, men en synder bliver et let bytte.

27-28Jeg har efterhånden stillet mange spørgsmål om livet og opdaget mange ting, men hvad jeg virkelig søgte efter, fandt jeg ikke. Blandt 1000 mænd fandt jeg kun én eneste, der var retskaffen, og blandt kvinder fandt jeg ingen.

29Jeg er overbevist om, at Gud har skabt menneskene, som de bør være. De har bare så mange sære ting for.