Mlaliki 5 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 5:1-20

Lemekeza Mulungu

1Uzisamala mayendedwe ako pamene ukupita ku nyumba ya Mulungu. Upite pafupi kuti ukamvetsere mʼmalo mopereka nsembe ya zitsiru zimene sizizindikira kuti zikuchita zolakwa.

2Usamafulumire kuyankhula,

usafulumire mu mtima mwako

kunena chilichonse pamaso pa Mulungu.

Mulungu ali kumwamba

ndipo iwe uli pa dziko lapansi,

choncho mawu ako akhale ochepa.

3Kuchuluka kwa mavuto mu mtima kumabweretsa maloto oyipa,

ndipo kuchuluka kwa mawu kumadzetsa uchitsiru.

4Pamene ulumbira kwa Mulungu usachedwe kukwaniritsa chimene walumbiracho. Iye sakondweretsedwa ndi chitsiru; kwaniritsa lumbiro lako. 5Kuli bwino kusalumbira kusiyana ndi kulumbira koma osakwaniritsa lumbirolo. 6Pakamwa pako pasakuchimwitse. Ndipo usanene kwa mthenga wa mʼNyumba ya Mulungu kuti, “Ndinalakwitsa polumbira.” Chifukwa chiyani ukufuna Mulungu akwiye ndi mawu ako ndiponso ntchito ya manja ako? 7Maloto ochuluka ndi mawu ochuluka ndi zinthu zopandapake. Kotero lemekeza Mulungu.

Chuma Nʼchopandapake

8Ngati uwona anthu osauka akuzunzika mʼdziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzawo ndi kuwalanda ufulu wawo, usadabwe ndi zinthu zimenezi; pakuti woyangʼanira ali naye wina womuyangʼanira wamkulu, ndipo pamwamba pa awiriwa pali ena akuluakulu owaposa. 9Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.

10Aliyense amene amakonda ndalama sakhutitsidwa ndi ndalamazo;

aliyense amene amakonda chuma sakhutitsidwa ndi zimene amapeza.

Izinso ndi zopandapake.

11Chuma chikachuluka

akudya nawo chumacho amachulukanso.

Nanga mwini wake amapindulapo chiyani

kuposa kumangochiyangʼana ndi maso ake?

12Wantchito amagona tulo tabwino

ngakhale adye pangʼono kapena kudya kwambiri,

koma munthu wolemera, chuma

sichimulola kuti agone.

13Ine ndinaona choyipa chomvetsa chisoni pansi pano:

chuma chokundikidwa chikupweteka mwini wake yemwe,

14kapena chuma chowonongedwa pa nthawi yatsoka,

kotero kuti pamene wabereka mwana

alibe kanthu koti amusiyire.

15Munthu anabadwa wamaliseche kuchokera mʼmimba mwa amayi ake,

ndipo monga iye anabadwira, adzapitanso choncho.

Pa zonse zimene iye anakhetsera thukuta

palibe nʼchimodzi chomwe chimene adzatenge mʼmanja mwake.

16Izinso ndi zoyipa kwambiri:

munthu adzapita monga momwe anabwerera,

ndipo iye amapindula chiyani,

pakuti amagwira ntchito yolemetsa yopanda phindu?

17Masiku ake onse ndi odzaza ndi mdima,

kukhumudwa kwakukulu, masautso ndi nkhawa.

18Tsono ndinazindikira kuti nʼchabwino ndi choyenera kuti munthu azidya ndi kumwa, ndi kukhutitsidwa ndi ntchito yake yolemetsa imene amayigwira pansi pano pa nthawi yake yochepa imene Mulungu amamupatsa, poti ichi ndiye chake. 19Komatu pamene Mulungu apereka chuma kwa munthu aliyense ndi zinthu zina, ndi kulola kuti akondwere ndi chumacho, munthuyo alandire chumacho ndi kusangalala ndi ntchito yake, imene ndi mphatso yochokera kwa Mulungu. 20Munthu wotereyu saganizirapo za masiku a moyo wake, chifukwa Mulungu amamutanganidwitsa ndi chisangalalo cha mu mtima mwake.

O Livro

Eclesiastes 5:1-20

Atitude para com Deus

1Quando entrares na casa de Deus, fá-lo numa atitude de reflexão! Entra com a intenção de escutar e não de oferecer sacrifícios, como fazem os insensatos, que nem sequer compreendem que fazem mal. 2Não fales precipitadamente, nem faças promessas irrefletidas a Deus, pois ele está nos céus e tu aqui na Terra; mede bem o que dizes.

3Assim como os muitos sonhos nascem da muita atividade, assim também, quanto mais se fala, mais riscos se correm de se proferirem disparates.

4Por isso, quando fizeres uma promessa a Deus, cumpre-a sem tardar; Deus não gosta de gente inconsequente, cumpre aquilo que prometeste. 5Vale muito mais não prometer coisa nenhuma do que prometer e depois não cumprir. 6Neste caso, a tua boca fez-te pecar. Não tentes defender-te, dizendo ao mensageiro de Deus que se tratou de um engano. Isso suscitaria a cólera de Deus, o qual acabaria com a tua prosperidade.

7Andar na vida a sonhar, em vez de realizar atos concretos, é tão inútil como proferir muitas palavras sem sentido. Por isso, tem cuidado em temer a Deus.

Riquezas são ilusão

8Se vires algum pobre oprimido pelo rico e a violência a substituir a justiça, em qualquer ponto da terra, não te surpreendas! Porque cada funcionário está sob as ordens de um outro, que lhe é superior, e o chefe de todos eles tem ainda alguém que lhe está acima. 9Todos devem usufruir do que a terra produz; até o mais alto magistrado se serve dela.

10Aquele que ama o dinheiro, nunca tem o bastante. É uma loucura pensar que a riqueza traz felicidade!

11Quanto mais tiveres, mais gastarás, até ao limite dos teus recursos. Por isso, de que serve ser-se rico? Apenas para ver o dinheiro fugir por entre os dedos!

12O trabalhador dorme bem, quer tenha pouco ou muito para comer, mas o rico, por causa dos muitos cuidados que lhe traz a fortuna, sofre de insónias.

13Há outra situação dramática, que verifiquei por toda a parte, a de alguém que põe dinheiro de lado, mas para seu próprio prejuízo. 14Se investir e perder capital num mau negócio, nada terá para deixar ao filho. 15Deixará a Terra, como quando chegou, sem nada possuir. 16Isto é igualmente um problema sério, porque todo o seu trabalho de nada lhe serviu; andou a trabalhar para o vento. 17O resto da sua vida será obscurecida por numerosos cuidados, sofrimentos e irritações.

18No entanto, vi uma coisa boa, uma pessoa a comer e a beber, a aproveitar os resultados do seu trabalho, durante o tempo de vida que Deus lhe deu. Essa é a porção que lhe cabe. 19Na verdade, é muito bom, se uma pessoa tiver recebido de Deus riqueza e saúde e puder desfrutar delas. Gozar do seu trabalho e aceitar a parte que lhe toca na vida é, na verdade, um dom de Deus. 20A pessoa que fizer isso não necessitará de olhar para trás, com tristeza, porque Deus lhe enche o coração de felicidade.