Mlaliki 5 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 5:1-20

Lemekeza Mulungu

1Uzisamala mayendedwe ako pamene ukupita ku nyumba ya Mulungu. Upite pafupi kuti ukamvetsere mʼmalo mopereka nsembe ya zitsiru zimene sizizindikira kuti zikuchita zolakwa.

2Usamafulumire kuyankhula,

usafulumire mu mtima mwako

kunena chilichonse pamaso pa Mulungu.

Mulungu ali kumwamba

ndipo iwe uli pa dziko lapansi,

choncho mawu ako akhale ochepa.

3Kuchuluka kwa mavuto mu mtima kumabweretsa maloto oyipa,

ndipo kuchuluka kwa mawu kumadzetsa uchitsiru.

4Pamene ulumbira kwa Mulungu usachedwe kukwaniritsa chimene walumbiracho. Iye sakondweretsedwa ndi chitsiru; kwaniritsa lumbiro lako. 5Kuli bwino kusalumbira kusiyana ndi kulumbira koma osakwaniritsa lumbirolo. 6Pakamwa pako pasakuchimwitse. Ndipo usanene kwa mthenga wa mʼNyumba ya Mulungu kuti, “Ndinalakwitsa polumbira.” Chifukwa chiyani ukufuna Mulungu akwiye ndi mawu ako ndiponso ntchito ya manja ako? 7Maloto ochuluka ndi mawu ochuluka ndi zinthu zopandapake. Kotero lemekeza Mulungu.

Chuma Nʼchopandapake

8Ngati uwona anthu osauka akuzunzika mʼdziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzawo ndi kuwalanda ufulu wawo, usadabwe ndi zinthu zimenezi; pakuti woyangʼanira ali naye wina womuyangʼanira wamkulu, ndipo pamwamba pa awiriwa pali ena akuluakulu owaposa. 9Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.

10Aliyense amene amakonda ndalama sakhutitsidwa ndi ndalamazo;

aliyense amene amakonda chuma sakhutitsidwa ndi zimene amapeza.

Izinso ndi zopandapake.

11Chuma chikachuluka

akudya nawo chumacho amachulukanso.

Nanga mwini wake amapindulapo chiyani

kuposa kumangochiyangʼana ndi maso ake?

12Wantchito amagona tulo tabwino

ngakhale adye pangʼono kapena kudya kwambiri,

koma munthu wolemera, chuma

sichimulola kuti agone.

13Ine ndinaona choyipa chomvetsa chisoni pansi pano:

chuma chokundikidwa chikupweteka mwini wake yemwe,

14kapena chuma chowonongedwa pa nthawi yatsoka,

kotero kuti pamene wabereka mwana

alibe kanthu koti amusiyire.

15Munthu anabadwa wamaliseche kuchokera mʼmimba mwa amayi ake,

ndipo monga iye anabadwira, adzapitanso choncho.

Pa zonse zimene iye anakhetsera thukuta

palibe nʼchimodzi chomwe chimene adzatenge mʼmanja mwake.

16Izinso ndi zoyipa kwambiri:

munthu adzapita monga momwe anabwerera,

ndipo iye amapindula chiyani,

pakuti amagwira ntchito yolemetsa yopanda phindu?

17Masiku ake onse ndi odzaza ndi mdima,

kukhumudwa kwakukulu, masautso ndi nkhawa.

18Tsono ndinazindikira kuti nʼchabwino ndi choyenera kuti munthu azidya ndi kumwa, ndi kukhutitsidwa ndi ntchito yake yolemetsa imene amayigwira pansi pano pa nthawi yake yochepa imene Mulungu amamupatsa, poti ichi ndiye chake. 19Komatu pamene Mulungu apereka chuma kwa munthu aliyense ndi zinthu zina, ndi kulola kuti akondwere ndi chumacho, munthuyo alandire chumacho ndi kusangalala ndi ntchito yake, imene ndi mphatso yochokera kwa Mulungu. 20Munthu wotereyu saganizirapo za masiku a moyo wake, chifukwa Mulungu amamutanganidwitsa ndi chisangalalo cha mu mtima mwake.

Luganda Contemporary Bible

Omubuulizi 5:1-20

Mutye Katonda

1Weekuume ng’oyingira mu nnyumba ya Katonda; okumusemberera n’okumuwuliriza, kisinga okuwaayo ssaddaaka ng’ez’abasirusiru abatamanyi nga bakola ebibi.

25:2 a Bal 11:35 b Yob 6:24; Nge 10:19; 20:25Toyanguyirizanga na kamwa ko okwogera ekigambo,

wadde omutima gwo ogwanguyiriza,

okwogera ekigambo mu maaso ga Katonda.

Katonda ali mu ggulu

ng’ate ggwe oli ku nsi;

kale ebigambo byo bibeerenga bitono.

35:3 a Yob 20:8 b Mub 10:14Ng’okutawaana ennyo bwe kuleetera omuntu ebirooto,

n’ebigambo by’omusirusiru bwe bityo bwe biba nga bingi.

45:4 a Ma 23:21; Bal 11:35; Zab 119:60 b Kbl 30:2; Zab 66:13-14; 76:11Bwe weeyamanga obweyamo eri Katonda tolwanga kubutuukiriza, kubanga tasanyukira basirusiru. Tuukirizanga obweyamo bwo. 55:5 Kbl 30:2-4; Nge 20:25; Yon 2:9; Bik 5:4Obuteyama kisinga okweyama n’ototuukiriza kye weeyamye. 6Akamwa ko kaleme ku kwonoonyesa, n’ogamba oyo atumiddwa gy’oli nti, “Nakola kisobyo okweyama.” Kale lwaki weeretako okusunguwalirwa Katonda olw’ebigambo byo, n’azikiriza emirimu gy’emikono gyo? 75:7 Mub 3:14; 12:13Ebirooto entoko n’ebigambo ebingi temuli makulu; noolwekyo otyanga Katonda.

Obugagga ku Bwabwo Bwokka Butaliimu Bwereere

85:8 Zab 12:5; Mub 4:1Bw’olabanga ng’omwavu anyigirizibwa mu ssaza, amazima n’obwenkanya nga tewali, teweewuunyanga! Kubanga omukungu waalyo alinako amusinga, ate nga bombi balina ababatwala. 9Bonna balya ku bibala bya nsi eyo; kabaka yennyini mu nnimiro zaayo mw’afuna.

10Oyo alulunkanira ensimbi, tasobola kuba na nsimbi zimumala;

wadde oyo alulunkanira obugagga n’amagoba:

na kino nakyo butaliimu.

11Ebintu nga bwe byeyongera obungi,

n’ababirya gye bakoma okweyongera.

Kale nnyini byo agasibwa ki,

okuggyako okusanyusa amaaso ge?

125:12 Yob 20:20Otulo tuwoomera omupakasi

ne bw’aba agabana bitono oba bingi.

Naye obugagga bw’omugagga obuyitiridde,

tebumuganya kwebaka.

Okukola n’Essanyu

135:13 Mub 6:1-2Waliwo ekibi ekinene kye nalaba wansi w’enjuba:

nannyini bugagga abuterekera mu kwerumya,

14ebyembi bw’ebigwawo eby’obugagga ebyo bibula,

kale bw’aba ne mutabani

tewabaawo mutabani we ky’asigaza.

155:15 a Yob 1:21 b Zab 49:17; 1Ti 6:7 c Mub 1:3Omuntu nga bwe yava mu lubuto lwa nnyina n’ajja mu nsi nga talina kintu,

bw’atyo bw’aliddayo nga mwereere ng’ava mu nsi.

Tewali ky’aggya mu mirimu gye,

wadde kyayinza okugenda nakyo mu mukono gwe.

165:16 Nge 11:29; Mub 1:3Na kino kya bulumi bwereere:

nga bwe yajja era bw’atyo bw’aligenda;

mugaso ki gwe yafuna mu kugoberera empewo?

17Era yamala obulamu bwe bwonna mu kizikiza ne mu buyinike,

ne mu kweraliikirira, ne mu bulumi ne mu kunyiiga.

185:18 a Mub 2:3 b Mub 2:10, 24Ne ndyoka ntegeera nti kituufu omuntu okulya n’okunywa n’okulaba nga yeyagalira mu kutakabana ne mu kukola kwe wansi w’enjuba, mu nnaku ze entono Katonda z’amuwadde, kubanga ekyo gwe mugabo gwe. 195:19 a 1By 29:12; 2By 1:12 b Mub 6:2 c Yob 31:2 d Mub 2:24; 3:13Ate Katonda bw’awa omuntu obugagga, n’ebintu n’amusobozesa okubyeyagaliramu, n’okutegeera omugabo gwe n’okusanyukira by’akoze, ekyo kiba kirabo ekivudde ewa Katonda. 205:20 Ma 12:7, 18Emirundi giba mitono gy’alowoolezaamu ekiseera ky’obulamu ky’amaze, kubanga Katonda ajjuza omutima gw’omuntu oyo essanyu.