Mlaliki 4 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 4:1-16

Matsoka ndi Mavuto a Moyo Uno

1Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano:

ndinaona misozi ya anthu opsinjika,

ndipo iwo alibe owatonthoza;

mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo

ndipo iwonso analibe owatonthoza.

2Ndipo ndinanena kuti akufa,

amene anafa kale,

ndi osangalala kuposa amoyo,

amene akanalibe ndi moyo.

3Koma wopambana onsewa

ndi amene sanabadwe,

amene sanaone zoyipa

zimene chimachitika pansi pano.

4Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

5Chitsiru chimangoti manja ake lobodo

ndi kudzipha chokha ndi njala.

6Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere,

kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto,

ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.

7Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:

8Panali munthu amene anali yekhayekha;

analibe mwana kapena mʼbale.

Ntchito yake yolemetsa sinkatha,

ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake.

Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani?

Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?”

Izinso ndi zopandapake,

zosasangalatsa!

9Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha,

chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:

10Ngati winayo agwa,

mnzakeyo adzamudzutsa.

Koma tsoka kwa munthu amene agwa

ndipo alibe wina woti amudzutse!

11Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana.

Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?

12Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa,

koma anthu awiri akhoza kudziteteza.

Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.

Kutukuka Nʼkopandapake

13Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo. 14Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo. 15Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu. 16Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.

Nova Versão Internacional

Eclesiastes 4:1-16

As Injustiças e os Absurdos da Vida

1De novo olhei e vi toda a opressão que ocorre debaixo do sol:

Vi as lágrimas dos oprimidos,

mas não há quem os console;

o poder está do lado dos seus opressores,

e não há quem os console.

2Por isso considerei os mortos

mais felizes do que os vivos,

pois estes ainda têm que viver!

3No entanto, melhor do que ambos

é aquele que ainda não nasceu,

que não viu o mal que se faz debaixo do sol.

4Descobri que todo trabalho e toda realização surgem da competição que existe entre as pessoas. Mas isso também é absurdo, é correr atrás do vento.

5O tolo cruza os braços

e destrói a própria vida.

6Melhor é ter um punhado com tranquilidade

do que dois punhados à custa de muito esforço

e de correr atrás do vento.

7Descobri ainda outra situação absurda debaixo do sol:

8Havia um homem totalmente solitário;

não tinha filho nem irmão.

Trabalhava sem parar!

Contudo, os seus olhos não se satisfaziam com a sua riqueza.

Ele sequer perguntava:

“Para quem estou trabalhando tanto,

e por que razão deixo de me divertir?”

Isso também é absurdo;

é um trabalho por demais ingrato!

9É melhor ter companhia do que estar sozinho,

porque maior é a recompensa do trabalho de duas pessoas.

10Se um cair,

o amigo pode ajudá-lo a levantar-se.

Mas pobre do homem que cai

e não tem quem o ajude a levantar-se!

11E, se dois dormirem juntos,

vão manter-se aquecidos.

Como, porém, manter-se aquecido sozinho?

12Um homem sozinho pode ser vencido,

mas dois conseguem defender-se.

Um cordão de três dobras não se rompe com facilidade.

A Futilidade do Poder

13Melhor é um jovem pobre e sábio, do que um rei idoso e tolo, que já não aceita repreensão. 14O jovem pode ter saído da prisão e chegado ao trono, ou pode ter nascido pobre no país daquele rei. 15Percebi que, ainda assim, o povo que vivia debaixo do sol seguia o jovem, o sucessor do rei. 16O número dos que aderiram a ele era incontável. A geração seguinte, porém, não ficou satisfeita com o sucessor. Isso também não faz sentido, é correr atrás do vento.