Mlaliki 3 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 3:1-22

Chilichonse Chili ndi Nthawi

1Chinthu chilichonse chili ndi nthawi yake,

ndi nyengo yake yomwe anayika Mulungu:

2Nthawi yobadwa ndi nthawi yomwalira,

nthawi yodzala ndi nthawi yokolola.

3Nthawi yakupha ndi nthawi yochiritsa,

nthawi yogwetsa ndi nthawi yomanga.

4Nthawi yomva chisoni ndi nthawi yosangalala,

nthawi yolira maliro ndi nthawi yovina.

5Nthawi yotaya miyala ndi nthawi yokundika miyala,

nthawi yokumbatirana ndi nthawi yoleka kukumbatirana.

6Nthawi yofunafuna ndi nthawi yoleka kufunafuna,

nthawi yosunga ndi nthawi yotaya.

7Nthawi yongʼamba ndi nthawi yosoka,

nthawi yokhala chete ndi nthawi yoyankhula.

8Nthawi yokondana ndi nthawi yodana,

nthawi ya nkhondo ndi nthawi ya mtendere.

9Kodi wantchito amapeza phindu lanji pa ntchito yake yolemetsa? 10Ine ndinaona chipsinjo chimene Mulungu anayika pa anthu. 11Iye anapanga chinthu chilichonse kuti chikhale chabwino pa nthawi yake. Anayika nzeru zamuyaya mʼmitima ya anthu; komabe anthuwo sangathe kuzindikira zomwe Mulungu wachita kuyambira pa chiyambi mpaka chimaliziro. 12Ine ndikudziwa kuti palibenso kanthu kabwino kwa anthu kopambana kusangalala ndi kuchita zabwino pamene ali ndi moyo. 13Ndi mphatso ya Mulungu kwa munthu kuti azidya, azimwa ndi kumakondwera ndi ntchito zake zolemetsa. 14Ndikudziwa kuti chilichonse chimene Mulungu amachita chidzakhala mpaka muyaya; palibe zimene zingawonjezedwe kapena kuchotsedwa. Mulungu amazichita kuti anthu azimuopa.

15Chilichonse chimene chilipo chinalipo kale,

ndipo chimene chidzakhalapo chinalipo poyamba;

Mulungu amabwezanso zakale zimene zinapita kuti zichitikenso.

16Ndipo ndinaona chinthu chinanso pansi pano:

ku malo achiweruzo, kuyipa mtima kuli komweko,

ku malo achilungamo, kuyipa mtima kuli komweko.

17Ndinalingalira mu mtima mwanga kuti;

“Mulungu adzaweruza

olungama pamodzi ndi oyipa omwe,

pakuti anayika nthawi yochitikira chinthu chilichonse,

nthawi ya ntchito iliyonse.”

18Ndinalingaliranso kuti, “Kunena za anthu, Mulungu amawayesa ndi cholinga choti awaonetse kuti iwo ali ngati nyama. 19Zimene zimachitikira munthu, zomwezonso zimachitikira nyama; chinthu chimodzi chomwecho chimachitikira onse: Monga munthu amafa momwemonso nyama imafa. Zonsezi zimapuma mpweya umodzimodzi omwewo; munthu saposa nyama. Zonsezi ndi zopandapake. 20Zonse zimapita kumodzimodzi; zonsezi zimachokera ku fumbi, ndipo zimabwereranso ku fumbi komweko. 21Kodi ndani amene amadziwa ngati mzimu wa munthu umakwera kumwamba, ndipo mzimu wa nyama umatsikira kunsi kwa dziko?”

22Kotero ndinaona kuti palibe chinthu chabwino kwa munthu kuposa kuti munthu azisangalala ndi ntchito yake, pakuti ichi ndiye chake chenicheni. Pakuti ndani amene angamubweretse kuti adzaone zimene zidzamuchitikira iye akadzamwalira?

O Livro

Eclesiastes 3:1-22

Tudo tem um tempo próprio

1Existe um tempo próprio para tudo e há uma época para cada coisa debaixo do céu.

2Há um tempo para nascer e um tempo para morrer;

um tempo para plantar e um tempo para colher o que se semeou;

3um tempo para matar e um tempo para curar as feridas;

um tempo para destruir e um tempo para reconstruir;

4um tempo para chorar e um tempo para rir;

um tempo para lamentar e um tempo para dançar de alegria;

5um tempo para espalhar pedras e um tempo para as juntar;

um tempo para abraçar e um tempo para afastar quem se chega a nós;

6um tempo para andar à procura e um tempo para perder;

um tempo para armazenar e um tempo para distribuir;

7um tempo para rasgar e um tempo para coser;

um tempo para estar calado e um tempo para falar;

8um tempo para amar e um tempo para odiar;

um tempo para a guerra e um tempo para a paz.

9O que é que uma pessoa realmente obtém com o seu esforço? 10Pensei nisto, em relação às várias espécies de trabalho que Deus dá à humanidade. 11Tudo tem o seu tempo próprio e ainda que Deus tenha posto no coração do ser humano a ideia da eternidade, mesmo assim o homem não consegue atingir inteiramente o propósito das obras de Deus, desde o princípio até ao fim. 12Por isso, concluí que, primeiramente, não há nada melhor para o ser humano do que ser feliz e gozar a vida, tanto quanto puder. 13Em segundo lugar, que deve comer, beber e desfrutar do fruto do seu trabalho, pois estas coisas são um dom de Deus.

14Uma coisa eu sei, é que tudo quanto Deus faz é perfeito, é para sempre; nada se lhe pode acrescentar ou tirar e a intenção de Deus é que as pessoas temam o Deus todo-poderoso. 15Aquilo que acontece agora, no presente, como o que vai acontecer mais tarde, já se produziu no passado. Deus faz com que os mesmos factos se repitam uma e outra vez.

16Observei também isto sobre a Terra, que a maldade reina onde o direito deveria ser aplicado e onde deveria ser feita justiça. 17E disse para comigo: “Com certeza que, no momento próprio, Deus julgará tudo quanto o ser humano faz, tanto o bem como o mal!”

18E assim dei-me conta que Deus permite que o mundo continue no curso do pecado, para poder testar a humanidade e para que os próprios homens verifiquem que não são melhores do que os animais. 19Pois tanto estes como aqueles respiram o mesmo ar e ambos morrem. A humanidade não tem vantagens reais sobre os animais. Eis outra coisa absurda! 20Tudo vai ter ao mesmo lugar, pois todos são pó e ao pó voltarão. 21Quem pode provar que o fôlego do homem vai para cima e o dos animais fica no pó da terra?

22Dessa forma, constatei que não há nada melhor para o homem do que ser feliz no seu trabalho; é esse o seu quinhão na Terra; ninguém o fará voltar à vida, para ver o que acontecerá depois dele. Por isso, que desfrute do presente!