Mlaliki 3 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 3:1-22

Chilichonse Chili ndi Nthawi

1Chinthu chilichonse chili ndi nthawi yake,

ndi nyengo yake yomwe anayika Mulungu:

2Nthawi yobadwa ndi nthawi yomwalira,

nthawi yodzala ndi nthawi yokolola.

3Nthawi yakupha ndi nthawi yochiritsa,

nthawi yogwetsa ndi nthawi yomanga.

4Nthawi yomva chisoni ndi nthawi yosangalala,

nthawi yolira maliro ndi nthawi yovina.

5Nthawi yotaya miyala ndi nthawi yokundika miyala,

nthawi yokumbatirana ndi nthawi yoleka kukumbatirana.

6Nthawi yofunafuna ndi nthawi yoleka kufunafuna,

nthawi yosunga ndi nthawi yotaya.

7Nthawi yongʼamba ndi nthawi yosoka,

nthawi yokhala chete ndi nthawi yoyankhula.

8Nthawi yokondana ndi nthawi yodana,

nthawi ya nkhondo ndi nthawi ya mtendere.

9Kodi wantchito amapeza phindu lanji pa ntchito yake yolemetsa? 10Ine ndinaona chipsinjo chimene Mulungu anayika pa anthu. 11Iye anapanga chinthu chilichonse kuti chikhale chabwino pa nthawi yake. Anayika nzeru zamuyaya mʼmitima ya anthu; komabe anthuwo sangathe kuzindikira zomwe Mulungu wachita kuyambira pa chiyambi mpaka chimaliziro. 12Ine ndikudziwa kuti palibenso kanthu kabwino kwa anthu kopambana kusangalala ndi kuchita zabwino pamene ali ndi moyo. 13Ndi mphatso ya Mulungu kwa munthu kuti azidya, azimwa ndi kumakondwera ndi ntchito zake zolemetsa. 14Ndikudziwa kuti chilichonse chimene Mulungu amachita chidzakhala mpaka muyaya; palibe zimene zingawonjezedwe kapena kuchotsedwa. Mulungu amazichita kuti anthu azimuopa.

15Chilichonse chimene chilipo chinalipo kale,

ndipo chimene chidzakhalapo chinalipo poyamba;

Mulungu amabwezanso zakale zimene zinapita kuti zichitikenso.

16Ndipo ndinaona chinthu chinanso pansi pano:

ku malo achiweruzo, kuyipa mtima kuli komweko,

ku malo achilungamo, kuyipa mtima kuli komweko.

17Ndinalingalira mu mtima mwanga kuti;

“Mulungu adzaweruza

olungama pamodzi ndi oyipa omwe,

pakuti anayika nthawi yochitikira chinthu chilichonse,

nthawi ya ntchito iliyonse.”

18Ndinalingaliranso kuti, “Kunena za anthu, Mulungu amawayesa ndi cholinga choti awaonetse kuti iwo ali ngati nyama. 19Zimene zimachitikira munthu, zomwezonso zimachitikira nyama; chinthu chimodzi chomwecho chimachitikira onse: Monga munthu amafa momwemonso nyama imafa. Zonsezi zimapuma mpweya umodzimodzi omwewo; munthu saposa nyama. Zonsezi ndi zopandapake. 20Zonse zimapita kumodzimodzi; zonsezi zimachokera ku fumbi, ndipo zimabwereranso ku fumbi komweko. 21Kodi ndani amene amadziwa ngati mzimu wa munthu umakwera kumwamba, ndipo mzimu wa nyama umatsikira kunsi kwa dziko?”

22Kotero ndinaona kuti palibe chinthu chabwino kwa munthu kuposa kuti munthu azisangalala ndi ntchito yake, pakuti ichi ndiye chake chenicheni. Pakuti ndani amene angamubweretse kuti adzaone zimene zidzamuchitikira iye akadzamwalira?

Священное Писание

Размышления 3:1-22

Всему своё время

1Всему есть своё время,

и для каждого дела под небом есть свой час:

2время рождаться и время умирать;

время сажать и время искоренять;

3время убивать и время исцелять;

время разрушать и время строить;

4время плакать и время смеяться;

время скорбеть и время танцевать;

5время раскидывать камни и время их собирать;

время обнимать и время воздерживаться от объятий;

6время искать и время терять;

время хранить и время выбрасывать;

7время рвать и время сшивать;

время молчать и время говорить;

8время любить и время ненавидеть;

время для войны и время для мира.

9В чём польза работнику от труда его? 10Я видел бремя, которое Всевышний возложил на людей. 11Он создал всё прекрасным в своё время. Он также вложил осознание вечности в сердца людей, но они не могут3:11 Или: «Но Он также вложил неведение в сердца людей, чтобы они не могли…» постичь всего, что делает Всевышний, от начала до конца. 12Я понял, что нет ничего лучше для людей, чем быть счастливыми и делать добро, пока они живы. 13И если кто-то может есть, пить и находить удовольствие во всяком своём труде, то это дар Всевышнего. 14Я понял, что всё, что делает Всевышний, пребудет вовек: к этому нечего прибавить и нечего от этого отнять. Всевышний делает так, чтобы люди благоговели перед Ним.

15Всё, что есть и что будет, уже было прежде,

ведь Всевышний повторяет то, что прошло3:15 Или: «Всевышний призовёт прошлое к ответу»; или: «Всевышний возвратит прошлое»..

Несправедливость в мире

16И вот что я ещё видел под солнцем:

место суда,

а там царит беззаконие,

место праведности,

а там – несправедливость.

17И подумал я:

«Всевышний будет судить обоих –

праведника и злодея,

потому что назначено время всякому событию

и всякому делу».

18И ещё я подумал о людях: «Всевышний испытывает их, чтобы показать им, что они подобны животным. 19Одна участь у людей и животных: умирают и те, и другие. Одно у тех и у других дыхание, и нет у человека никаких преимуществ перед животными. Всё пустое. 20Всё возвращается на круги свои: всё пришло из праха, и в прах всё возвратится. 21Кто знает, поднимается ли дух человека вверх, и опускается ли дух животного вниз, в землю?»

22И увидел я, что нет ничего лучше для человека, чем наслаждаться своим трудом, потому что такова его доля. Ведь кто может показать ему то, что будет после него?