Mlaliki 2 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 2:1-26

Zosangalatsa Nʼzopandapake

1Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Tsopano ndiyese zosangalatsa kuti ndipeze zomwe ndi zabwino.” Koma izi zinaonekanso kuti ndi zopandapake. 2“Kuseka,” ndinati, “imeneyo ndi misala. Ndipo kodi chisangalalo chimabweretsa phindu lanji?” 3Ndinayesa kudzisangalatsa ndi vinyo, koma umenewu unali uchitsiru, pamenepo nʼkuti maganizo anga akutsogozedwa ndi nzeru. Ine ndinkati mwina kapena njira yotero nʼkukhala yopambana, imene anthu amatsata pofuna kusangalala pa masiku owerengeka a moyo wawo.

4Ndinagwira ntchito zikuluzikulu: Ndinadzimangira nyumba ndi kuwoka mipesa. 5Ndinalima madimba ndi minda yamitengo; ndipo ndinadzalamo mitengo ya zipatso za mitundu yonse. 6Ndinakumba mayiwe osungiramo madzi woti ndizithirira minda ya mitengo yodzalidwa ija. 7Ndinagula akapolo aamuna ndi akapolo aakazi, ndiponso ndinali ndi akapolo ena omwe anabadwira mʼnyumba mwanga. Ndinalinso ndi ngʼombe ndi nkhosa zambiri kupambana aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. 8Ndinadzikundikira siliva ndi golide, ndiponso chuma chochokera kwa mafumu ndi madera awo. Ndinali ndi amuna ndi akazi oyimba ndiponso azikazi; zinthu zokondweretsa mtima wa munthu. 9Ndinali munthu wotchuka kupambana wina aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. Mu zonsezi nzeru zanga zinali nane.

10Sindinadzimane chilichonse chimene maso anga anachifuna;

mtima wanga sindinawumane zokondweretsa.

Mtima wanga unakondwera ndi ntchito yanga yonse,

ndipo iyi ndiyo inali mphotho ya ntchito zanga zonse zolemetsa.

11Koma pamene ndinayamba kuyangʼanayangʼana zonse zimene ndinachita ndi manja anga,

ndi zimene ndinazivutikira kuti ndizipeze,

zonsezi zinali zopandapake; kungodzivuta chabe,

palibe chomwe ndinapindula pansi pano.

Nzeru ndi Uchitsiru Nʼzopandapake

12Kenaka maganizo anga anayamba kulingalira zakuti nzeru nʼchiyani,

komanso kuti misala ndi uchitsiru nʼchiyani.

Kodi munthu wodzalowa ufumu tsopanoyo angachite chiyani

choposa chimene chinachitidwa kale?

13Ndinaona kuti nzeru ndi yopambana uchitsiru,

monga momwe kuwala kumapambanira mdima.

14Munthu wanzeru amayenda maso ali patsogolo,

pamene chitsiru chimayenda mʼchimbulimbuli;

koma ndinazindikira kuti chomwe

chimawachitikira onsewo ndi chimodzi.

15Pamenepo ndinalingalira mu mtima mwanga,

“Zochitikira chitsiru zidzandichitikiranso ine.

Nanga tsono phindu langa nʼchiyani pakukhala wanzeru?”

Ndinati mu mtima mwanga,

“Ichinso ndi chopandapake.”

16Pakuti munthu wanzeru, pamodzinso ndi chitsiru sadzakumbukiridwa nthawi yayitali;

mʼmasiku amʼtsogolo awiriwo adzayiwalika.

Mmene chimafera chitsiru ndi mmenenso amafera wanzeru!

Kugwira Ntchito Nʼkopandapake

17Kotero ndinadana nawo moyo chifukwa ntchito zimene zimagwiridwa pansi pano ndi zosautsa kwa ine. Ntchito zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe. 18Ine ndinadana nazo ntchito zonse zimene ndinazigwira pansi pano, chifukwa ndinayenera kudzazisiyira wina amene adzalowa mʼmalo mwanga. 19Ndipo ndani amadziwa kuti munthu ameneyo adzakhala wanzeru kapena chitsiru? Komabe munthuyo adzakhala wolamulira zonse zimene ndinazichita pansi pano mwa nzeru zanga. Izinso ndi zopandapake. 20Motero ndinayamba kutaya mtima chifukwa cha ntchito zonse zimene ndinazivutikira pansi pano. 21Pakuti munthu atha kugwira ntchito yake mwanzeru, chidziwitso ndi luntha, ndipo kenaka nʼkusiyira wina amene sanakhetserepo thukuta. Izinso ndi zopandapake ndiponso tsoka lalikulu. 22Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zonse zolemetsa ndi zodetsa nkhawa zimene amazichita pansi pano? 23Masiku ake onse amakhala achisoni, ntchito yake imakhala yovuta; ngakhale usiku womwe, mtima wake supumula. Izinso ndi zopandapake.

24Kwa munthu palibe chabwino china kuposa kudya, kumwa ndi kukondwerera ntchito zake. Izinso ndaona kuti ndi zochokera kwa Mulungu, 25pakuti popanda Iye, ndani angadye ndi kupeza chisangalalo? 26Munthu amene amakondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamusandutsa wanzeru, wozindikira ndi wachisangalalo, koma wochimwa, Mulungu amamupatsa ntchito yosonkhanitsa ndi kusunga chuma kuti adzachipereke kwa amene Mulunguyo amakondwera naye. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

Nova Versão Internacional

Eclesiastes 2:1-26

Os Prazeres Não Têm Sentido

1Eu disse a mim mesmo: Venha. Experimente a alegria. Descubra as coisas boas da vida! Mas isso também se revelou inútil. 2Concluí que o rir é loucura, e a alegria de nada vale. 3Decidi entregar-me ao vinho e à extravagância, mantendo, porém, a mente orientada pela sabedoria. Eu queria saber o que vale a pena, debaixo do céu, nos poucos dias da vida humana.

4Lancei-me a grandes projetos: construí casas e plantei vinhas para mim. 5Fiz jardins e pomares e neles plantei todo tipo de árvore frutífera. 6Construí também reservatórios para irrigar os meus bosques verdejantes. 7Comprei escravos e escravas e tive escravos que nasceram em minha casa. Além disso, tive também mais bois e ovelhas do que todos os que viveram antes de mim em Jerusalém. 8Ajuntei para mim prata e ouro, tesouros de reis e de províncias. Servi-me de cantores e cantoras, e também de um harém, as delícias dos homens. 9Tornei-me mais famoso e poderoso do que todos os que viveram em Jerusalém antes de mim, conservando comigo a minha sabedoria.

10Não me neguei nada que os meus olhos desejaram;

não me recusei a dar prazer algum ao meu coração.

Na verdade, eu me alegrei em todo o meu trabalho;

essa foi a recompensa de todo o meu esforço.

11Contudo, quando avaliei

tudo o que as minhas mãos haviam feito e o trabalho

que eu tanto me esforçara para realizar,

percebi que tudo foi inútil,

foi correr atrás do vento;

não há nenhum proveito no que se faz debaixo do sol.

A Sabedoria e a Insensatez

12Então passei a refletir na sabedoria,

na loucura e na insensatez.

O que pode fazer o sucessor do rei,

a não ser repetir o que já foi feito?

13Percebi que a sabedoria é melhor que a insensatez,

assim como a luz é melhor do que as trevas.

14O homem sábio tem olhos que enxergam2.14 Hebraico: na cabeça.,

mas o tolo anda nas trevas;

todavia, percebi que ambos têm o mesmo destino.

15Aí fiquei pensando:

O que acontece ao tolo também me acontecerá.

Que proveito eu tive em ser sábio?

Então eu disse a mim mesmo:

Isso não faz o menor sentido!

16Nem o sábio, nem o tolo serão lembrados para sempre;

nos dias futuros ambos serão esquecidos.

Como pode o sábio morrer como o tolo morre?

O Trabalho Árduo é Inútil

17Por isso desprezei a vida, pois o trabalho que se faz debaixo do sol pareceu-me muito pesado. Tudo era inútil, era correr atrás do vento. 18Desprezei todas as coisas pelas quais eu tanto me esforçara debaixo do sol, pois terei que deixá-las para aquele que me suceder. 19E quem pode dizer se ele será sábio ou tolo? Todavia, terá domínio sobre tudo o que realizei com o meu trabalho e com a minha sabedoria debaixo do sol. Isso também não faz sentido. 20Cheguei ao ponto de me desesperar por todo o trabalho no qual tanto me esforcei debaixo do sol. 21Pois um homem pode realizar o seu trabalho com sabedoria, conhecimento e habilidade, mas terá que deixar tudo o que possui como herança para alguém que não se esforçou por aquilo. Isso também é um absurdo e uma grande injustiça. 22Que proveito tem um homem de todo o esforço e de toda a ansiedade com que trabalha debaixo do sol? 23Durante toda a sua vida, seu trabalho é pura dor e tristeza; mesmo à noite a sua mente não descansa. Isso também é absurdo.

24Para o homem não existe nada melhor do que comer, beber e encontrar prazer em seu trabalho. E vi que isso também vem da mão de Deus. 25E quem aproveitou melhor as comidas e os prazeres do que eu?2.25 Várias versões antigas dizem Pois sem ele, quem poderia comer ou encontrar satisfação? 26Ao homem que o agrada, Deus dá sabedoria, conhecimento e felicidade. Quanto ao pecador, Deus o encarrega de ajuntar e armazenar riquezas para entregá-las a quem o agrada. Isso também é inútil, é correr atrás do vento.