Mlaliki 12 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 12:1-14

1Uzikumbukira mlengi wako

masiku a unyamata wako,

masiku oyipa asanafike,

nthawi isanafike pamene udzanena kuti,

“Izi sizikundikondweretsa.”

2Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala,

mwezi ndi nyenyezi zidzada.

Mitambo idzabweranso mvula itagwa.

3Nthawi imene manja ako adzanjenjemera,

miyendo yako idzafowoka,

pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka,

ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.

4Makutu ako adzatsekeka,

ndipo sudzamva phokoso lakunja;

sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo

kapena kulira kwa mbalame mmawa.

5Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera,

amaopa kuyenda mʼmisewu;

Mutu umatuwa kuti mbuu,

amayenda modzikoka ngati ziwala

ndipo chilakolako chimatheratu.

Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya

ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.

6Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke,

kapena mbale yagolide isanasweke;

mtsuko usanasweke ku kasupe,

kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.

7Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera,

mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.

8“Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki.

“Zonse ndi zopandapake!”

Mawu Otsiriza

9Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri. 10Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.

11Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi. 12Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi.

Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.

13Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa:

uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake,

pakuti umenewu ndiwo udindo

wa anthu onse.

14Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse,

kuphatikizanso zinthu zonse zobisika,

kaya zabwino kapena zoyipa.

Korean Living Bible

전도서 12:1-14

1너는 아직 젊을 때, 곧 고난의 날이 오기 전에, 아무 낙이 없다고 말할 때가 되기 전에 너의 창조자를 기억하라.

2네가 너무 늙어 해와 달과 별이 보이지 않고 슬픔이 떠날 날이 없을 때 그를 기억하려고 하면 늦을 것이다.

312:3 3-5절은의역하였음.그 때에는 너를 보호하던 팔도 떨 것이며 지금 강한 너의 다리도 약해질 것이다. 그리고 이빨이 거의 다 빠져 음식을 잘 씹지 못할 것이며 눈은 어두워서 보지 못할 것이다.

4귀는 어두워서 거리에서 들려오는 소리를 듣지 못할 것이며 음식을 씹는 소리가 적을 것이다. 그리고 깊은 잠을 자지 못할 것이며 음성도 떨릴 것이다.

5그때 너는 높은 곳을 두려워할 것이며 걷는 것도 위험할 것이다. 머리는 온통 희어지고 거동하기가 불편해서 몸을 제대로 끌고 다닐 수 없을 것이며 모든 의욕과 정욕은 사라질 것이다. 그렇게 되면 결국 조객들이 네 집을 찾아들 날도 멀지 않을 것이다.

612:6 또는 ‘혼줄’은줄이 끊어지고 몸의 모든 기능이 정지되며

7육은 본래의 흙으로 돌아가고 영은 그것을 주신 하나님께로 돌아가기 전에 너의 창조자를 기억하라.

8전도자가 말한다. “헛되고 헛되며 모든 것이 헛될 뿐이다!”

인간의 본분

9전도자는 지혜로운 사람이었기 때문에 자기가 아는 것을 사람들에게 계속 가르쳤으며 그는 또 깊이 생각하고 연구하는 중에 많은 금언을 모아 정리하였다.

10이 전도자는 바르고 고운 말을 찾으려고 애썼으므로 그가 기록한 것은 거짓이 없고 진실하다.

11지혜로운 자들의 말은 양떼를 모는 채찍 같고 그들이 수집한 명언은 잘 박힌 못과 같은 것이니 그것은 다 우리의 목자 되시는 하나님이 주신 것이다.

12내 아들아, 이 밖에 조심할 일이 있다: 아무리 책을 많이 써도 끝이 없으니 지나치게 공부하는 것은 몸을 피곤하게 할 뿐이다.

13이제 모든 것을 다 들었으니 결론은 이것이다: 하나님을 두려운 마음으로 섬기고 그의 명령에 순종하라. 이것이 사람의 본분이다.

14선하건 악하건 하나님은 우리가 하는 모든 일을 은밀한 것까지 다 심판하실 것이다.