Mlaliki 11 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 11:1-10

Kuponya Chakudya pa Madzi

1Ponya chakudya chako pa madzi,

udzachipezanso patapita masiku ambiri.

2Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu,

pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.

3Ngati mitambo yadzaza ndi madzi,

imagwetsa mvula pa dziko lapansi.

Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto,

ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.

4Amene amayangʼana mphepo sadzadzala;

amene amayangʼana mitambo sadzakolola.

5Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo,

kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi,

momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu,

Mlengi wa zinthu zonse.

6Dzala mbewu zako mmawa

ndipo madzulo usamangoti manja lobodo,

pakuti sudziwa chimene chidzapindula,

mwina ichi kapena icho,

kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.

Kumbukira Mlengi Wako

7Kuwala nʼkwabwino,

ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.

8Munthu akakhala wa zaka zambiri,

mulekeni akondwerere zaka zonsezo,

koma iye azikumbukira masiku a mdima,

pakuti adzakhala ochuluka.

Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.

9Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono,

ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako.

Tsatira zimene mtima wako ukufuna,

ndiponso zimene maso ako akuona,

koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo

Mulungu adzakuweruza.

10Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako,

upewe zokupweteka mʼthupi mwako,

pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.

Hoffnung für Alle

Prediger 11:1-10

Wer nicht wagt, der nicht gewinnt!

1Setz dein Hab und Gut ein, um Handel zu treiben, und eines Tages wird es dir Gewinn bringen.11,1 Wörtlich: Lass dein Brot über das Wasser fahren, dann wirst du es wiederfinden nach langer Zeit. – Die Bedeutung dieses Sprichwortes ist unsicher. 2Verteil deinen Besitz auf möglichst viele Stellen, denn du weißt nicht, ob ein großes Unglück über das Land kommt und alles zerstört.

3Wenn die Wolken voll Wasser sind, wird es auch regnen, und wohin ein Baum fällt, dort bleibt er liegen.

4Wer immer nur auf das passende Wetter wartet, wird nie säen; und wer ängstlich auf jede Wolke schaut, wird nie ernten.

5Du weißt nicht, aus welcher Richtung der Wind kommen wird; du siehst nicht, wie ein Kind im Mutterleib Gestalt annimmt. Ebenso wenig kannst du die Taten Gottes ergründen, der alles bewirkt.

6Säe am Morgen deine Saat aus, leg aber auch am Abend die Hände nicht in den Schoß! Denn du weißt nicht, ob das eine oder das andere gedeiht – oder vielleicht sogar beides zusammen!

Genieß deine Jugend!

7Wie schön ist es, am Leben zu sein und das Licht der Sonne zu sehen! 8Freu dich über jedes neue Jahr, das du erleben darfst! Auch wenn noch viele vor dir liegen – denk daran, dass die Dunkelheit danach lange dauert! Alles, was dann kommt, ist vergeblich!

9Du junger Mensch, genieße deine Jugend und freu dich in der Blüte deines Lebens! Tu, was dein Herz dir sagt und was deinen Augen gefällt! Aber sei dir bewusst, dass Gott dich für alles zur Rechenschaft ziehen wird! 10Lass dich nicht von Kummer und Sorgen beherrschen und halte allen Schmerz von dir fern! Denn Jugend und Frische11,10 Wörtlich: und Schwärze (= dunkles Haar). sind vergänglich.