Mlaliki 10 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 10:1-20

1Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira,

choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.

2Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino,

koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.

3Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu,

zochita zake ndi zopanda nzeru

ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.

4Ngati wolamulira akukwiyira,

usachoke pa ntchito yako;

kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.

5Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano,

kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:

6Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba,

pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.

7Ndaona akapolo atakwera pa akavalo,

pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.

8Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha;

amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.

9Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo;

amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.

10Ngati nkhwangwa ili yobuntha

yosanoledwa,

pamafunika mphamvu zambiri potema,

koma luso limabweretsa chipambano.

11Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka

ngati njokayo yakuluma kale.

12Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa,

koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.

13Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa;

potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala

14ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu.

Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo,

ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?

15Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa;

ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.

16Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana,

ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.

17Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka

ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake,

kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.

18Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka;

ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.

19Phwando ndi lokondweretsa anthu,

ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo,

koma ndalama ndi yankho la chilichonse.

20Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako,

kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako,

pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako

nʼkukafotokoza zomwe wanena.