Miyambo 9 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 9:1-18

Za Nzeru ndi Uchitsiru

1Nzeru inamanga nyumba yake;

inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.

2Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake;

inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.

3Nzeruyo inatuma adzakazi ake,

kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,

4“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!”

Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,

5“Bwerani, dzadyeni chakudya changa

ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.

6Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo;

yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”

7Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo;

aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.

8Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe;

dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.

9Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru;

ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.

10Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru;

kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.

11Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka,

ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.

12Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa;

ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.

13Uchitsiru ndi mkazi waphokoso,

wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.

14Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake,

pamalo aatali a mu mzinda,

15kuti aziyitana anthu ongodutsa,

amene akunka nayenda njira zawo.

16Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,”

ndipo kwa wopanda nzeru amati,

17“Madzi akuba ndiye amatsekemera;

chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”

18Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko,

ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya.

King James Version

Proverbs 9:1-18

1Wisdom hath builded her house, she hath hewn out her seven pillars: 2She hath killed her beasts; she hath mingled her wine; she hath also furnished her table.9.2 her beasts: Heb. her killing 3She hath sent forth her maidens: she crieth upon the highest places of the city, 4Whoso is simple, let him turn in hither: as for him that wanteth understanding, she saith to him, 5Come, eat of my bread, and drink of the wine which I have mingled. 6Forsake the foolish, and live; and go in the way of understanding. 7He that reproveth a scorner getteth to himself shame: and he that rebuketh a wicked man getteth himself a blot. 8Reprove not a scorner, lest he hate thee: rebuke a wise man, and he will love thee. 9Give instruction to a wise man, and he will be yet wiser: teach a just man, and he will increase in learning. 10The fear of the LORD is the beginning of wisdom: and the knowledge of the holy is understanding. 11For by me thy days shall be multiplied, and the years of thy life shall be increased. 12If thou be wise, thou shalt be wise for thyself: but if thou scornest, thou alone shalt bear it.

13¶ A foolish woman is clamorous: she is simple, and knoweth nothing. 14For she sitteth at the door of her house, on a seat in the high places of the city, 15To call passengers who go right on their ways: 16Whoso is simple, let him turn in hither: and as for him that wanteth understanding, she saith to him, 17Stolen waters are sweet, and bread eaten in secret is pleasant.9.17 eaten…: Heb. of secrecies 18But he knoweth not that the dead are there; and that her guests are in the depths of hell.