Miyambo 9 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 9:1-18

Za Nzeru ndi Uchitsiru

1Nzeru inamanga nyumba yake;

inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.

2Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake;

inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.

3Nzeruyo inatuma adzakazi ake,

kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,

4“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!”

Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,

5“Bwerani, dzadyeni chakudya changa

ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.

6Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo;

yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”

7Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo;

aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.

8Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe;

dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.

9Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru;

ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.

10Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru;

kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.

11Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka,

ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.

12Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa;

ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.

13Uchitsiru ndi mkazi waphokoso,

wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.

14Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake,

pamalo aatali a mu mzinda,

15kuti aziyitana anthu ongodutsa,

amene akunka nayenda njira zawo.

16Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,”

ndipo kwa wopanda nzeru amati,

17“Madzi akuba ndiye amatsekemera;

chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”

18Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko,

ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Мудрые изречения 9:1-18

Приглашения мудрости и глупости

1Мудрость построила себе дом,

вытесала для него семь столбов.

2Она заколола из своего скота,

смешала вино с пряностями

и на стол накрыла.

3Она разослала своих служанок

призывать с возвышенностей городских,

4сказать тем, кто безрассуден:

«Пусть все простаки обратятся ко мне!

5Идите, ешьте мою еду

и пейте вино, которое я приправила.

6Оставьте невежество – и будете жить;

ходите дорогой разума.

7Наставляющий глумливого бесчестие наживёт;

обличающий нечестивого навлечёт на себя позор.

8Не обличай глумливого, чтобы он тебя не возненавидел;

обличай мудреца, и он возлюбит тебя.

9Научи мудреца, и он станет ещё мудрее;

праведника наставь – он познания приумножит.

10Страх перед Вечным – начало мудрости,

и познание Святого – разум.

11Ведь со мною умножатся твои дни,

годы жизни твоей продлятся.

12Если ты мудр, твоя мудрость вознаградит тебя;

если глумлив – ты один и пострадаешь».

13Глупость – женщина шумливая;

она невежда и ничего не знает9:13 Или: «Глупость – женщина соблазнительная; она не знает, что такое стыд»..

14Сидит она у дверей своего дома,

на площади городской сидит она на стуле

15и зовёт проходящих мимо,

идущих прямо своим путём:

16«Пусть все простаки обратятся ко мне!»

Говорит она тем, кто безрассуден:

17«Сладка украденная вода;

вкусен хлеб, что едят утайкой!»

18И не знают они, что зовут их к духам умерших,

что гости её в глубинах мира мёртвых.