Miyambo 8 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 8:1-36

Nzeru Ikuyitana

1Kodi nzeru sikuyitana?

Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?

2Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira,

imayima pa mphambano ya misewu.

3Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda,

pa makomo olowera imafuwula kuti,

4Inu anthu, ndikuyitana inu;

ndikuyitanatu anthu onse.

5Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera;

inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.

6Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri;

ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.

7Pakamwa panga pamayankhula zoona

ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.

8Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama;

mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.

9Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona;

kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.

10Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva,

nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.

11Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali,

ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.

12Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera.

Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.

13Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa.

Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama,

kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.

14Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino;

ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.

15Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira.

Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.

16Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula.

Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.

17Ndimakonda amene amandikonda,

ndipo amene amandifunafuna amandipeza.

18Ine ndili ndi chuma ndi ulemu,

chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.

19Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala;

zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.

20Ndimachita zinthu zolungama.

Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.

21Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda

ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.

22“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba.

Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.

23Ndinapangidwa kalekalelo,

pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.

24Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi,

zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.

25Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo,

mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,

26lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake;

lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.

27Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga,

pamene ankalemba malire a nyanja yozama,

28pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga

ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,

29pamene anayikira nyanja malire

kuti madzi asadutse malirewo,

ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.

30Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri;

ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku,

kusangalala nthawi zonse pamaso pake.

31Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse

ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”

32“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni;

odala anthu amene amasunga njira zanga.

33Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru;

musanyozere mawu anga.

34Wodala munthu amene amandimvera,

amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku,

kudikirira pa chitseko changa.

35Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo

ndipo Yehova amamukomera mtima.

36Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha;

onse amene amandida amakonda imfa.”

King James Version

Proverbs 8:1-36

1Doth not wisdom cry? and understanding put forth her voice? 2She standeth in the top of high places, by the way in the places of the paths. 3She crieth at the gates, at the entry of the city, at the coming in at the doors. 4Unto you, O men, I call; and my voice is to the sons of man. 5O ye simple, understand wisdom: and, ye fools, be ye of an understanding heart. 6Hear; for I will speak of excellent things; and the opening of my lips shall be right things. 7For my mouth shall speak truth; and wickedness is an abomination to my lips.8.7 an…: Heb. the abomination of my lips 8All the words of my mouth are in righteousness; there is nothing froward or perverse in them.8.8 froward: Heb. wreathed 9They are all plain to him that understandeth, and right to them that find knowledge. 10Receive my instruction, and not silver; and knowledge rather than choice gold. 11For wisdom is better than rubies; and all the things that may be desired are not to be compared to it.

12I wisdom dwell with prudence, and find out knowledge of witty inventions.8.12 prudence: or, subtilty 13The fear of the LORD is to hate evil: pride, and arrogancy, and the evil way, and the froward mouth, do I hate. 14Counsel is mine, and sound wisdom: I am understanding; I have strength. 15By me kings reign, and princes decree justice. 16By me princes rule, and nobles, even all the judges of the earth. 17I love them that love me; and those that seek me early shall find me. 18Riches and honour are with me; yea, durable riches and righteousness. 19My fruit is better than gold, yea, than fine gold; and my revenue than choice silver. 20I lead in the way of righteousness, in the midst of the paths of judgment:8.20 lead: or, walk 21That I may cause those that love me to inherit substance; and I will fill their treasures.

22The LORD possessed me in the beginning of his way, before his works of old. 23I was set up from everlasting, from the beginning, or ever the earth was. 24When there were no depths, I was brought forth; when there were no fountains abounding with water. 25Before the mountains were settled, before the hills was I brought forth: 26While as yet he had not made the earth, nor the fields, nor the highest part of the dust of the world.8.26 fields: or, open places8.26 the highest…: or, the chief part 27When he prepared the heavens, I was there: when he set a compass upon the face of the depth:8.27 a compass: or, a circle 28When he established the clouds above: when he strengthened the fountains of the deep: 29When he gave to the sea his decree, that the waters should not pass his commandment: when he appointed the foundations of the earth: 30Then I was by him, as one brought up with him: and I was daily his delight, rejoicing always before him; 31Rejoicing in the habitable part of his earth; and my delights were with the sons of men.

32Now therefore hearken unto me, O ye children: for blessed are they that keep my ways. 33Hear instruction, and be wise, and refuse it not. 34Blessed is the man that heareth me, watching daily at my gates, waiting at the posts of my doors. 35For whoso findeth me findeth life, and shall obtain favour of the LORD.8.35 obtain: Heb. bring forth 36But he that sinneth against me wrongeth his own soul: all they that hate me love death.