Miyambo 6 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 6:1-35

Za Moyo wa Uchitsiru

1Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole,

ngati walonjeza kumulipirira mlendo,

2ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena,

wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.

3Tsono popeza iwe mwana wanga

wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse:

pita msanga ukamupemphe mnansi wako;

kuti akumasule!

4Usagone tulo,

usawodzere.

5Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje,

ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.

6Pita kwa nyerere, mlesi iwe;

kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!

7Zilibe mfumu,

zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,

8komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe

ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.

9Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe?

Kodi tulo tako tidzatha liti?

10Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono

ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,

11umphawi udzakugwira ngati mbala

ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.

12Munthu wachabechabe, munthu woyipa,

amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,

13amatsinzinira maso ake,

namakwakwaza mapazi ake

ndi kulozaloza ndi zala zake,

14amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo

ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.

15Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa;

adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.

16Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo,

zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:

17maso onyada,

pakamwa pabodza,

manja akupha munthu wosalakwa,

18mtima wokonzekera kuchita zoyipa,

mapazi othamangira msanga ku zoyipa,

19mboni yonama yoyankhula mabodza

komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.

Chenjezo pa za Chigololo

20Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako;

ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.

21Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse,

uzimangirire mʼkhosi mwako.

22Ukamayenda, zidzakulozera njira;

ukugona, zidzakulondera;

ukudzuka, zidzakuyankhula.

23Paja malamulo awa ali ngati nyale,

malangizowa ali ngati kuwunika,

ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo

moyo weniweni,

24kukupulumutsa kwa mkazi wadama,

zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.

25Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake,

asakukope ndi zikope zake,

26paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi

ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.

27Kodi munthu angathe kutenga moto

zovala zake osapsa?

28Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto

mapazi ake osapserera?

29Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina.

Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.

30Paja anthu sayinyoza mbala ikaba

chifukwa chakuti ili ndi njala.

31Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri,

ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.

32Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru.

Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.

33Adzalandira mabala ndi mʼnyozo,

ndipo manyazi ake sadzamuchokera.

34Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa,

ndipo sadzachita chifundo pobwezera.

35Iye savomera dipo lililonse;

sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.