Miyambo 5 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 5:1-23

Chenjezo kwa Mkazi Wachigololo

1Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi,

tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,

2kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru

ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.

3Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi.

Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,

4koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu;

ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.

5Mapazi ake amatsikira ku imfa;

akamayenda ndiye kuti akupita ku manda.

6Iye saganizirapo za njira ya moyo;

njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.

7Tsopano ana inu, mundimvere;

musawasiye mawu anga.

8Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo,

usayandikire khomo la nyumba yake,

9kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena;

ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,

10kapenanso alendo angadyerere chuma chako

ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.

11Potsiriza pa moyo wako udzabuwula,

thupi lako lonse litatheratu.

12Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo!

Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!

13Sindinamvere aphunzitsi anga

kapena alangizi anga.

14Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke

pakati pa msonkhano wonse.”

15Imwa madzi a mʼchitsime chakochako,

madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.

16Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu?

Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?

17Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha,

osati uyigawireko alendo.

18Yehova adalitse kasupe wako,

ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.

19Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino.

Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse,

ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.

20Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo?

Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?

21Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona,

ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.

22Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha;

zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.

23Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo,

adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.

Nova Versão Internacional

Provérbios 5:1-23

Advertência contra o Adultério

1Meu filho, dê atenção à minha sabedoria,

incline os ouvidos para perceber o meu discernimento.

2Assim você manterá o bom senso,

e os seus lábios guardarão o conhecimento.

3Pois os lábios da mulher imoral destilam mel,

sua voz é mais suave que o azeite;

4mas no final é amarga como fel,

afiada como uma espada de dois gumes.

5Os seus pés descem para a morte;

os seus passos conduzem diretamente para a sepultura.

6Ela nem percebe que anda por caminhos tortuosos

e não enxerga a vereda da vida.

7Agora, então, meu filho, ouça-me;

não se desvie das minhas palavras.

8Fique longe dessa mulher;

não se aproxime da porta de sua casa,

9para que você não entregue aos outros o seu vigor

nem a sua vida a algum homem cruel,

10para que estranhos não se fartem do seu trabalho

e outros não se enriqueçam à custa do seu esforço.

11No final da vida você gemerá,

com sua carne e seu corpo desgastados.

12Você dirá: “Como odiei a disciplina!

Como o meu coração rejeitou a repreensão!

13Não ouvi os meus mestres

nem escutei os que me ensinavam.

14Cheguei à beira da ruína completa,

à vista de toda a comunidade”.

15Beba das águas da sua cisterna,

das águas que brotam do seu próprio poço.

16Por que deixar que as suas fontes transbordem pelas ruas,

e os seus ribeiros pelas praças?

17Que elas sejam exclusivamente suas,

nunca repartidas com estranhos.

18Seja bendita a sua fonte!

Alegre-se com a esposa da sua juventude.

19Gazela amorosa, corça graciosa;

que os seios de sua esposa sempre o fartem de prazer,

e sempre o embriaguem os carinhos dela.

20Por que, meu filho, ser desencaminhado pela mulher imoral?

Por que abraçar o seio de uma leviana5.20 Ou de uma mulher casada?

21O Senhor vê os caminhos do homem

e examina todos os seus passos.

22As maldades do ímpio o prendem;

ele se torna prisioneiro das cordas do seu pecado.

23Certamente morrerá por falta de disciplina;

andará cambaleando por causa da sua insensatez.