Miyambo 5 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 5:1-23

Chenjezo kwa Mkazi Wachigololo

1Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi,

tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,

2kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru

ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.

3Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi.

Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,

4koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu;

ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.

5Mapazi ake amatsikira ku imfa;

akamayenda ndiye kuti akupita ku manda.

6Iye saganizirapo za njira ya moyo;

njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.

7Tsopano ana inu, mundimvere;

musawasiye mawu anga.

8Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo,

usayandikire khomo la nyumba yake,

9kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena;

ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,

10kapenanso alendo angadyerere chuma chako

ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.

11Potsiriza pa moyo wako udzabuwula,

thupi lako lonse litatheratu.

12Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo!

Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!

13Sindinamvere aphunzitsi anga

kapena alangizi anga.

14Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke

pakati pa msonkhano wonse.”

15Imwa madzi a mʼchitsime chakochako,

madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.

16Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu?

Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?

17Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha,

osati uyigawireko alendo.

18Yehova adalitse kasupe wako,

ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.

19Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino.

Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse,

ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.

20Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo?

Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?

21Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona,

ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.

22Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha;

zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.

23Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo,

adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Proverbios 5:1-23

Advertencia contra el adulterio

1Hijo mío, pon atención a mi sabiduría

y presta oído a mi buen juicio,

2para que al hablar mantengas la discreción

y retengas el conocimiento.

3De los labios de la adúltera fluye miel;

su lengua es más suave que el aceite.

4Pero al final resulta más amarga que la hiel

y más cortante que una espada de dos filos.

5Sus pies descienden hasta la muerte;

sus pasos van derecho al sepulcro.

6No tiene ella en cuenta el camino de la vida;

sus sendas son torcidas, y ella no lo reconoce.5:6 y ella no lo reconoce. Alt. y tú no lo sabes.

7Pues bien, hijo mío, préstame atención

y no te apartes de mis palabras.

8Aléjate de la adúltera;

no te acerques a la puerta de su casa,

9para que no entregues a otros tu vigor,

ni tus años a gente cruel;

10para que no sacies con tu fuerza a gente extraña,

ni vayan a dar en casa ajena tus esfuerzos.

11Porque al final acabarás llorando,

cuando todo tu ser5:11 todo tu ser. Lit. tu carne y tu cuerpo. se haya consumido.

12Y dirás: «¡Cómo pude aborrecer la corrección!

¡Cómo pudo mi corazón despreciar la disciplina!

13No atendí a la voz de mis maestros,

ni presté oído a mis instructores.

14Ahora estoy al borde de la ruina,

en medio de toda la comunidad».

15Bebe el agua de tu propio pozo,

el agua que fluye de tu propio manantial.

16¿Habrán de derramarse tus fuentes por las calles

y tus corrientes de aguas por las plazas públicas?

17Son tuyas, solamente tuyas,

y no para que las compartas con extraños.

18¡Bendita sea tu fuente!

¡Goza con la esposa de tu juventud!

19Es una gacela amorosa,

es una cervatilla encantadora.

¡Que sus pechos te satisfagan siempre!

¡Que su amor te cautive todo el tiempo!

20¿Por qué, hijo mío, dejarte cautivar por una adúltera?

¿Por qué abrazarte al pecho de la mujer ajena?

21Nuestros caminos están a la vista del Señor;

él examina todas nuestras sendas.

22Al malvado lo atrapan sus malas obras;

las cuerdas de su pecado lo aprisionan.

23Morirá por su falta de disciplina;

perecerá por su gran insensatez.