Miyambo 30 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 30:1-33

Mawu a Aguri

1Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:

Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa.

Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.

2“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;

ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.

3Sindinaphunzire nzeru,

ndipo Woyerayo sindimudziwa.

4Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?

Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake?

Ndani anamanga madzi mʼchovala chake?

Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi?

Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa!

Ndipo mwana wake dzina lake ndani?

5“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;

Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.

6Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,

kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”

7“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri

musandimane zimenezo ndisanafe:

8Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.

Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma.

Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku

9kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,

nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’

Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba,

potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”

10“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake

kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”

11“Alipo ena amene amatemberera abambo awo,

ndipo sadalitsa amayi awo.

12Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima

komatu sanachotse zoyipa zawo.

13Pali ena ndi odzitukumula kwambiri,

amene amakweza zikope modzitukumula.

14Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga

ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni

moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi.

Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”

15“Msundu uli ndi ana aakazi awiri

iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’ ”

“Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta,

zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’

16Manda, mkazi wosabala,

nthaka yosakhuta madzi

ndiponso moto womangoyakirayakira!”

17Aliyense amene amanyoza abambo ake,

ndi kunyozera kumvera amayi ake,

makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso

ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.

18Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,

zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.

19Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;

mmene iyendera njoka pa thanthwe;

mmene chiyendera chombo pa nyanja;

ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.

20Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:

Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake

iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”

21Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,

pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:

22Kapolo amene wasanduka mfumu,

chitsiru chimene chakhuta,

23mkazi wonyozeka akakwatiwa

ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.

24Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,

komatu ndi zochenjera kwambiri:

25Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,

komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;

26mbira zili ngati anthu opanda mphamvu

komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;

27dzombe lilibe mfumu,

komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.

28Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja

komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.

29“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,

pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:

30Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,

ndipo suthawa kanthu kalikonse.

31Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,

ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.

32“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,

kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa,

ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!

33Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,

ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka,

ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

New Serbian Translation

Приче Соломонове 30:1-33

Агурове приче

1Поруке Агура, Јекајевог сина,

пророштво овог човека казано Итилу,

Итилу и Укалу.

2„Елем, ја сам простији од било кога

и немам памети људске;

3нисам се поучио мудрости

и знање Светог немам.

4Ко се то успео на небеса па сишао?

Ко је сабрао ветар у шаке своје?

Ко је то увио воде у плашт?

Ко је поставио све земљине крајеве?

Како му је име

и како му се син зове,

знаш ли?

5Свака је Божија реч опробана.

Он је штит онима који у њему уточиште налазе.

6Не додаји речима његовим

да те не би прекорио,

да се не би показало да си лажов.

7Две ствари од тебе тражим,

не ускрати ми их док сам жив:

8бескорисну, лажљиву реч од мене удаљи;

не дај ми сиромаштва и богатства,

дај ми хлеба да једем тек да се наједем;

9да се не бих заситио, па се одрекао

и рекао ’Ко је Господ?’

Или да не бих осиромашио, па крао

и ружио име Бога свога.

10Не клевећи слугу господару његовом

да те не би проклињао, па би крив био.

11Неки сој проклиње оца свога

и мајку своју не благосиља.

12Неки је сој себи самом чист

па од измета свог остаје неопран.

13О, како неки сој уздиже очи

и како му је поглед надмен!

14Неком су соју зуби ко мачеви

а вилице ко ножеви,

да са земље прождеру убоге

и несрећнике људског рода.

15Пијавица има две ћерке –

Дај и Дај.

Три су ствари незасите

и четири никада не кажу ’Доста!’:

16Свет мртвих,

јалова утроба,

земља воде никад сита

и ватра што не каже ’Доста!’

17Око што се оцу руга

и презире послушност мајци,

искљуцаће поточни гаврани

и појешће орлићи.

18Три су ми ствари зачуђујуће

и четири су ми непознате:

19орлов лет по небесима,

пузање змије по стени,

пловидба лађе посред мора

и пут мушкарца са девојком.

20А пут жене прељубнице је овакав:

она једе, обрише уста па каже:

’Никакво зло нисам урадила!’

21Под три ствари земља се потреса

и четири не може да носи:

22слугу када се зацари,

будалу кад је сита хлеба,

23невољену, а удату жену,

и слушкињу кад замени газдарицу своју.

24Четири су створа малена на земљи,

а опет су преко мере учињена мудрим:

25мрави, нејак народ,

али лети себи припремају храну;

26дамани, нејак народ,

али дом свој на стенама праве;

27скакавци, иако без цара,

ал’ сви лете у поретку;

28гуштер, иако га с обе руке хваташ,

ено га у одајама царским.

29Три су створа корака поносног

и четири што отмено газе:

30лав, од свих звери јачи, ни пред чим не узмиче;

31петао када се шепури,

јарац

и цар са војском поред себе.

32Ако си будаласт био себе уздижући,

ако ли си сплеткарио,

руку на уста стави.

33Јер када се млеко бућка, настаје масло;

и када се нос истрља, крв процури;

а када бес ускипи, то доноси свађу.“