Miyambo 30 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 30:1-33

Mawu a Aguri

1Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:

Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa.

Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.

2“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;

ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.

3Sindinaphunzire nzeru,

ndipo Woyerayo sindimudziwa.

4Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?

Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake?

Ndani anamanga madzi mʼchovala chake?

Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi?

Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa!

Ndipo mwana wake dzina lake ndani?

5“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;

Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.

6Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,

kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”

7“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri

musandimane zimenezo ndisanafe:

8Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.

Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma.

Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku

9kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,

nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’

Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba,

potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”

10“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake

kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”

11“Alipo ena amene amatemberera abambo awo,

ndipo sadalitsa amayi awo.

12Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima

komatu sanachotse zoyipa zawo.

13Pali ena ndi odzitukumula kwambiri,

amene amakweza zikope modzitukumula.

14Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga

ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni

moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi.

Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”

15“Msundu uli ndi ana aakazi awiri

iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’ ”

“Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta,

zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’

16Manda, mkazi wosabala,

nthaka yosakhuta madzi

ndiponso moto womangoyakirayakira!”

17Aliyense amene amanyoza abambo ake,

ndi kunyozera kumvera amayi ake,

makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso

ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.

18Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,

zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.

19Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;

mmene iyendera njoka pa thanthwe;

mmene chiyendera chombo pa nyanja;

ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.

20Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:

Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake

iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”

21Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,

pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:

22Kapolo amene wasanduka mfumu,

chitsiru chimene chakhuta,

23mkazi wonyozeka akakwatiwa

ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.

24Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,

komatu ndi zochenjera kwambiri:

25Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,

komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;

26mbira zili ngati anthu opanda mphamvu

komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;

27dzombe lilibe mfumu,

komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.

28Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja

komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.

29“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,

pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:

30Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,

ndipo suthawa kanthu kalikonse.

31Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,

ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.

32“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,

kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa,

ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!

33Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,

ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka,

ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

New International Reader’s Version

Proverbs 30:1-33

The Sayings of Agur

1These sayings are the words of Agur, son of Jakeh. These sayings came from God.

This man said to Ithiel:

“I am weary, God.

But I can still have success.

2Surely I am only a dumb animal and not a man.

I don’t understand as other men do.

3I haven’t learned wisdom.

And I don’t know the things the Holy One knows.

4Who has gone up to heaven and come down?

Whose hands have gathered up the wind?

Who has wrapped up the waters in a coat?

Who has set in place all the boundaries of the earth?

What is his name? What is his son’s name?

Surely you know!

5“Every word of God is perfect.

He is like a shield to those who trust in him.

He keeps them safe.

6Don’t add to his words.

If you do, he will correct you.

He will prove that you are a liar.

7Lord, I ask you for two things.

Don’t refuse me before I die.

8Keep lies far away from me.

Don’t make me either poor or rich,

but give me only the bread I need each day.

9If you don’t, I might have too much.

Then I might say I don’t know you.

I might say, ‘Who is the Lord?’

Or I might become poor and steal.

Then I would bring shame to the name of my God.

10“Don’t tell lies about a servant when you talk to their master.

If you do, they will curse you, and you will pay for your lies.

11“Some people curse their fathers.

Others don’t bless their mothers.

12Some are pure in their own eyes.

But their dirty sins haven’t been washed away.

13Some have eyes that are very proud.

They look down on others.

14Some people have teeth like swords.

The teeth in their jaws are as sharp as knives.

They are ready to eat up the poor people of the earth.

They are ready to eat up those who are the most needy.

15“A leech has two daughters.

They cry out, ‘Give! Give!’

“Three things are never satisfied.

Four things never say, ‘Enough!’

16The first is the grave.

The second is a woman who can’t have a baby.

The third is land, which never gets enough water.

And the fourth is fire, which never says, ‘Enough!’

17“One person makes fun of their father.

Another doesn’t honor their mother when she is old.

The ravens of the valley will peck out their eyes.

Then the vultures will eat them.

18“Three things are too amazing for me.

There are four things I don’t understand.

19The first is the way of an eagle in the sky.

The second is the way of a snake on a rock.

The third is the way of a ship on the ocean.

And the fourth is the way of a man with a young woman.

20“This is the way of a woman who commits adultery.

She eats and wipes her mouth.

Then she says, ‘I haven’t done anything wrong.’

21“Under three things the earth shakes.

Under four things it can’t stand up.

22The first is a servant who becomes a king.

The second is a foolish and ungodly person who gets plenty to eat.

23The third is a mean woman who gets married.

And the fourth is a servant who takes the place of the woman she works for.

24“Four things on earth are small.

But they are very wise.

25The first are ants, which aren’t very strong.

But they store up their food in the summer.

26The second are hyraxes, which aren’t very powerful.

But they make their home among the rocks.

27The third are locusts, which don’t have a king.

But they all march forward in ranks.

28And the fourth are lizards, which your hand can catch.

But you will find them in kings’ palaces.

29“Three things walk as if they were kings.

Four things move as kings do.

30The first is a lion, which is mighty among the animals. It doesn’t back away from anything.

31The second is a rooster, which walks proudly.

The third is a billy goat.

And the fourth is a king, who is secure against any who might oppose him.

32“Do you do foolish things?

Do you think you are better than others?

Do you plan evil?

If you do, put your hand over your mouth and stop talking!

33If you churn cream, you will produce butter.

If you twist a nose, you will produce blood.

And if you stir up anger, you will produce a fight.”