Miyambo 30 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 30:1-33

Mawu a Aguri

1Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:

Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa.

Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.

2“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;

ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.

3Sindinaphunzire nzeru,

ndipo Woyerayo sindimudziwa.

4Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?

Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake?

Ndani anamanga madzi mʼchovala chake?

Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi?

Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa!

Ndipo mwana wake dzina lake ndani?

5“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;

Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.

6Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,

kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”

7“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri

musandimane zimenezo ndisanafe:

8Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.

Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma.

Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku

9kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,

nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’

Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba,

potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”

10“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake

kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”

11“Alipo ena amene amatemberera abambo awo,

ndipo sadalitsa amayi awo.

12Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima

komatu sanachotse zoyipa zawo.

13Pali ena ndi odzitukumula kwambiri,

amene amakweza zikope modzitukumula.

14Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga

ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni

moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi.

Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”

15“Msundu uli ndi ana aakazi awiri

iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’ ”

“Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta,

zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’

16Manda, mkazi wosabala,

nthaka yosakhuta madzi

ndiponso moto womangoyakirayakira!”

17Aliyense amene amanyoza abambo ake,

ndi kunyozera kumvera amayi ake,

makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso

ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.

18Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,

zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.

19Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;

mmene iyendera njoka pa thanthwe;

mmene chiyendera chombo pa nyanja;

ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.

20Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:

Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake

iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”

21Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,

pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:

22Kapolo amene wasanduka mfumu,

chitsiru chimene chakhuta,

23mkazi wonyozeka akakwatiwa

ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.

24Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,

komatu ndi zochenjera kwambiri:

25Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,

komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;

26mbira zili ngati anthu opanda mphamvu

komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;

27dzombe lilibe mfumu,

komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.

28Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja

komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.

29“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,

pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:

30Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,

ndipo suthawa kanthu kalikonse.

31Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,

ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.

32“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,

kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa,

ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!

33Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,

ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka,

ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

Het Boek

Spreuken 30:1-33

1Dit zijn de woorden van Agur, de zoon van Jake—het zijn woorden van God. De strijder zegt: ‘God, ik heb zoveel moeite gedaan, ik kan niet meer!

2Ik schiet tegenover iedereen tekort en het ontbreekt mij aan verstand.

3Ik heb geen wijsheid verkregen en begrijp ook niets van alles wat heilig is.’

4Wie ging er naar de hemel en kwam weer terug? Wie houdt de wind stevig vast? Wie heeft al het water in een mantel gebonden? Wie gaf de aarde haar vorm en omtrek? Hoe heet Hij en hoe heet zijn Zoon? Zeg het mij als u het weet.

5Gods woorden zijn puur en zuiver, Hij beschermt ieder die op Hem vertrouwt.

6Voeg niets aan zijn woorden toe, want dan straft Hij u, omdat u een leugenaar bent.

7God, ik heb twee dingen aan U gevraagd en geef mij die alstublieft voordat ik sterf:

8houd ongeloof en leugens bij mij weg, geef mij armoe noch rijkdom, maar alleen wat ik nodig heb.

9Want als ik verzadigd zou zijn, zou ik U misschien verloochenen door te zeggen: ‘Wie is de Here?’ En als ik arm was, zou ik misschien gaan stelen en daardoor uw naam oneer aandoen.

10Klaag een knecht niet aan bij zijn meester, anders vervloekt hij u misschien en beschouwt God u als schuldig.

11Er zijn mensen die hun ouders vervloeken,

12mensen die zichzelf goed vinden, maar in werkelijkheid zondig zijn,

13mensen die hooghartig om zich heen kijken en anderen verachten,

14mensen die hun tanden als zwaarden en hun kiezen als messen gebruiken, om daarmee de noodlijdenden en de armen te vermalen.

15De bloedzuiger heeft twee dochters: ze zijn onverzadigbaar en willen steeds meer. Drie dingen zijn absoluut niet te verzadigen, voor de volgende vier dingen is het nooit genoeg:

16het graf, een onvruchtbare baarmoeder, de aarde die nooit genoeg water heeft, en het vuur. Geen van die vier zegt ooit: ‘Nu is het genoeg.’

17Het oog waaruit minachting voor een vader spreekt of dat opstandig kijkt naar een moeder, wordt uitgepikt door de raven bij de beek, wordt voedsel voor de jonge adelaars.

18Veel dingen zijn voor mij onbegrijpelijk, de volgende vier kan ik niet bevatten:

19een adelaar die hoog aan de hemel zweeft, een slang die moeiteloos over een gladde rots kruipt, een schip dat veilig door de golven vaart en wat gebeurt tussen een man en zijn jonge vrouw.

20En minstens zo onbegrijpelijk is het gedrag van een vrouw die overspel pleegt: zij zondigt, kleedt zich weer aan en zegt: ‘Ik heb niets verkeerds gedaan.’

21Mensen hebben een afschuw van veel dingen en de volgende vier dingen zijn onverdraaglijk:

22een knecht die macht krijgt, een dwaas die in weelde leeft,

23een verbitterde vrouw die toch trouwt en een dienares die de plaats van haar meesteres inneemt.

24De volgende vier zijn weliswaar klein, maar hebben van God grote wijsheid gekregen:

25de mieren hebben weliswaar geen verstand, maar zijn toch zo verstandig in de zomer hun voedsel te verzamelen,

26klipdassen mogen dan redeloze dieren zijn, maar hebben wel hun hol in de rotsen,

27hoewel sprinkhanen geen leider hebben, trekken zij op in geordende groepen,

28de hagedis is met de hand te pakken, maar leeft zelfs in koninklijke paleizen.

29Er zijn veel indrukwekkende dingen op aarde, de volgende vier bijvoorbeeld:

30een oude leeuw, een bejaarde koning der dieren die voor niemand aan de kant gaat,

31een soepel rennende windhond, een trotse bok en een onoverwinnelijke koning.

32Hebt u in uw woede dwaas gehandeld of hebt u kwaad in de zin, zwijg dan en voer uw plan niet uit!

33Want door melk te karnen ontstaat boter, door te hard op de neus te drukken ontstaat een bloedneus en door woede op te wekken ontstaat ruzie.