Miyambo 29 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 29:1-27

1Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri,

adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.

2Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa,

koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.

3Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake,

koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.

4Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo,

koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.

5Munthu woshashalika mnzake,

akudziyalira ukonde mapazi ake.

6Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake,

koma wochita chilungamo amayimba lokoma.

7Munthu wolungama amasamalira anthu osauka,

koma woyipa salabadira zimenezi.

8Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda,

koma anthu anzeru amaletsa ukali.

9Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru,

chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.

10Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro

koma anthu olungama amasamalira moyo wake.

11Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake,

koma munthu wanzeru amadzigwira.

12Ngati wolamulira amvera zabodza,

akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.

13Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti:

Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.

14Ngati mfumu iweruza osauka moyenera,

mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.

15Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru

koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.

16Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka,

koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.

17Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere

ndi kusangalatsa mtima wako.

18Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo;

koma wodala ndi amene amasunga malamulo.

19Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi;

ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.

20Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo

kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.

21Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana,

potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.

22Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano,

ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.

23Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa,

koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.

24Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe;

amalumbira koma osawulula kanthu.

25Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha,

koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.

26Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima,

koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.

27Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo;

koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.