Miyambo 28 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 28:1-28

1Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa,

koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.

2Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri,

koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.

3Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake

ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.

4Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa,

koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.

5Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama,

koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.

6Munthu wosauka wa makhalidwe abwino

aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.

7Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu,

koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.

8Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka

amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.

9Wokana kumvera malamulo

ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.

10Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa

adzagwera mu msampha wake womwe,

koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.

11Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru,

koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.

12Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu;

koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.

13Wobisa machimo ake sadzaona mwayi,

koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.

14Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse,

koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.

15Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa

ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.

16Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza

koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.

17Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu

adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake;

wina aliyense asamuthandize.

18Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa

koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.

19Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka,

koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.

20Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri,

koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.

21Kukondera si kwabwino,

ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.

22Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera

koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.

23Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake

mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.

24Amene amabera abambo ake kapena amayi ake

namanena kuti “kumeneko sikulakwa,”

ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.

25Munthu wadyera amayambitsa mikangano,

koma amene amadalira Yehova adzalemera.

26Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru,

koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.

27Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu,

koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.

28Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala,

koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

Luganda Contemporary Bible

Engero 28:1-28

128:1 a 2Bk 7:7 b Lv 26:17; Zab 53:5 c Zab 138:3Abakozi b’ebibi badduka nga tewali abagoba,

naye abatuukirivu babeera n’obuvumu ng’empologoma.

2Eggwanga bwe lijeema, liba n’abafuzi bangi,

naye olw’omuntu alina okutegeera n’okumanya obutebenkevu budda nate mu nsi.

3Omufuzi anyigiriza abaavu,

afaanana nga enkuba etonnya ezikiriza n’eterekaawo birime.

4Abo abava ku mateeka ga Mukama batendereza aboonoonyi,

naye abo abagakuuma babawakanya.

5Abantu abakozi b’ebibi tebategeera bwenkanya,

naye abo abanoonya Mukama babutegeerera ddala bulungi.

628:6 Nge 19:1Omuntu omwavu atambulira mu butuukirivu,

asinga omugagga ow’amakubo amakyamu.

728:7 Nge 23:19-21Oyo akuuma amateeka ga Mukama mwana eyeegendereza,

naye mukwano gw’ab’omululu akwasa kitaawe ensonyi.

828:8 a Kuv 18:21 b Yob 27:17; Nge 13:22 c Zab 112:9; Nge 14:31; Luk 14:12-14Ayongera ku bugagga bwe mu bukumpanya,

abukuŋŋaanyiza omulala anaayinza okuba ow’ekisa eri abaavu.

928:9 Zab 66:18; 109:7; Nge 15:8; Is 1:13Atassaayo mwoyo kuwulira mateeka ga Mukama,

n’okusaba kwe tekukkirizibwa.

1028:10 Nge 26:27Buli akyamya abatuukirivu mu kkubo ebbi,

aligwa mu katego ke ye,

naye abatuukirivu balisikira ebirungi.

11Omugagga alowooza nti mugezi,

naye omwavu alina okutegeera, amunyooma.

1228:12 a 2Bk 11:20 b Nge 11:10; 29:2Abatuukirivu bwe bawangula wabaawo okujaguza okw’amaanyi,

naye abakakanyalira mu kukola ebikyamu bwe bafuna obuyinza abantu beekweka.

1328:13 a Yob 31:33 b Zab 32:1-5; 1Yk 1:9Oyo akweka ebibi bye, talifuna mukisa kukulaakulana,

naye buli abyatula n’abireka, alisaasirwa.

14Alina omukisa omuntu atya Mukama ebbanga lyonna,

naye oyo akakanyaza omutima gwe abonaabona.

15Ng’empologoma ewuluguma oba eddubu eritiisatiisa,

bw’abeera omufuzi omubi atulugunya abateesobola.

16Omufuzi nantagambwako tafuga na bwenkanya,

naye oyo akyawa amagoba agafuniddwa mu bukyamu alibeera n’essanyu ery’obulamu obuwangaazi.

1728:17 Lub 9:6Omuntu alumirizibwa olw’okutta munne,

alibeera mu kutegana okutuusa okufa,

tewabanga n’omu amuyamba.

1828:18 Nge 10:9Omuntu atambulira mu bugolokofu alinunulibwa talibeerako kabi,

naye oyo ow’amakubo amabi aligwa mbagirawo.

1928:19 Nge 12:11Omuntu alima ennimiro ye aliba n’emmere nnyingi,

naye oyo ali mu birowoozo ebitaliimu alifa bwavu.

2028:20 nny 22; Nge 10:6; 1Ti 6:9Omusajja omwesigwa aliweebwa emikisa mingi,

naye oyo ayanguyiriza okugaggawala talirema kubonerezebwa.

2128:21 a Nge 18:5 b Ez 13:19Okuttira abantu ku liiso ng’osala emisango si kirungi,

naye ate olw’okunoonya akookulya omuntu ayinza okuzza omusango.

2228:22 nny 20; Nge 23:6Omusajja omukodo yeegomba okugaggawala,

naye nga tamanyi nti obwavu bumulindiridde.

2328:23 Nge 27:5-6Oyo anenya omuntu, oluvannyuma aliganja,

okusinga oyo awaaniriza n’olulimi.

2428:24 a Nge 19:26 b Nge 18:9Buli anyaga kitaawe, oba nnyina,

n’agamba nti, “Si nsonga,” afaanana n’oyo azikiriza.

2528:25 Nge 29:25Omuntu ow’omululu aleeta oluyombo,

naye oyo eyeesiga Mukama aligaggawazibwa.

2628:26 Zab 4:5; Nge 3:5Eyeesiga omutima gwe, musirusiru,

naye oyo atambulira mu magezi alifuna emirembe.

2728:27 Ma 15:7; 24:19; Nge 19:17; 22:9Agabira abaavu talibaako ne kye yeetaaga,

naye abakodowalira anaabanga n’ebikolimo bingi.

2828:28 nny 12Abakozi b’ebibi bwe babeera mu buyinza, abantu beekweka,

naye abakozi b’ebibi bwe bazikirira, abatuukirivu bakulaakulana.