Miyambo 27 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 27:1-27

1Usamanyadire za mawa,

pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.

2Munthu wina akutamande, koma osati wekha;

mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.

3Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri,

koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.

4Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa.

Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.

5Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino

kuposa chikondi chobisika.

6Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino,

koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.

7Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi,

koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.

8Munthu amene wasochera ku nyumba kwake,

ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.

9Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima,

ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.

10Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako,

ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto;

mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.

11Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga;

pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.

12Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,

koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.

13Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole;

ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.

14Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri,

anthu adzamuyesa kuti akutemberera.

15Mkazi wolongolola ali ngati

mvula yamvumbi.

16Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo

kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.

17Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake,

chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.

18Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake,

ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.

19Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi,

chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.

20Manda sakhuta,

nawonso maso a munthu sakhuta.

21Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo,

chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.

22Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo

ndi musi ngati chimanga,

uchitsiru wakewo sudzachoka.

23Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili.

Kodi usamalire bwino ziweto zako?

24Paja chuma sichikhala mpaka muyaya,

ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.

25Pamene udzu watha, msipu nʼkumera;

ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,

26ana ankhosa adzakupatsani chovala

ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.

27Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri

kuti muzidya inuyo ndi banja lanu

ndi kudyetsa antchito anu aakazi.

Священное Писание

Мудрые изречения 27:1-27

1Не хвастайся завтрашним днём,

ты ведь не знаешь, что он принесёт.

2Пусть другой тебя хвалит, а не твои уста, –

посторонний, а не твой язык.

3Камень увесист, тяжёл и песок,

но раздражение от глупца тяжелее обоих.

4Ярость жестока и гнев неукротим,

но кто может устоять против ревности?

5Лучше открытый упрёк,

чем скрытая любовь.

6Друг искренен, даже если он ранит,

а враг рассыпает поцелуи.

7Сытым и сотовый мёд отвратителен,

а голодным и горькое кажется сладким.

8Что птица, оставившая гнездо,

то человек, который ушёл из дома.

9Как ароматное масло и благовоние радуют сердце,

так приятно слышать и душевный совет от друга.

10Не бросай своего друга и друга своего отца;

в беде не беги сразу к родственникам,

ведь друг поблизости будет полезнее, чем родня вдали.

11Будь мудрым, сын мой, и сердце моё порадуй;

тогда я буду знать, что ответить попрекающему меня.

12Разумный увидит опасность – и скроется,

а простаки пойдут дальше – и пострадают.

13Можешь смело забирать одежду у поручившегося за незнакомца;

можешь удержать её в залог у ручавшегося за чужого27:13 Ср. Исх. 22:26-27; Втор. 24:10-13..

14Громогласно благословляющего ближнего ранним утром

сочтут проклинающим.

15Несмолкающая капель в дождливый день

и сварливая жена схожи друг с другом;

16пытаться сдержать её – что сдерживать ветер

или масло в руке зажать.

17Как железо оттачивает железо,

так и люди совершенствуют друг друга.

18Кто возделывает инжир, будет есть его плоды,

а кто заботится о своём господине, будет в чести.

19Как вода отражает лицо,

так человеческое сердце – человека.

20Мир мёртвых и царство смерти не знают сытости;

ненасытны и человеческие глаза.

21В тигле испытывается серебро,

в горне плавильном – золото,

а похвалами – человек.

22Глупца истолки хоть в ступе,

как пестом пшеницу, –

не отделится от него его глупость.

23Следи за тем, в каком виде твои отары,

хорошо наблюдай за своими стадами,

24ведь богатство не вечно,

и власть не на все поколения.

25Когда вывезут сено, и появится новая поросль,

и станут собирать траву со склонов горных,

26тогда ягнята одеждой тебя снабдят,

а козлы пойдут на покупку поля.

27У тебя будет вдоволь козьего молока,

чтобы кормить себя и свою семью

и давать пропитание служанкам.