Miyambo 26 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 26:1-28

1Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola,

ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.

2Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira,

ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.

3Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu,

choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.

4Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake,

kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.

5Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake,

kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.

6Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga

kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.

7Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu

ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.

8Kupereka ulemu kwa chitsiru

zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.

9Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa

ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.

10Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda,

ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.

11Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake

chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.

12Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo

kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.

13Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango,

mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”

14Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake,

momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.

15Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale;

zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.

16Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru

kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.

17Munthu wongolowera mikangano imene si yake

ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.

18Monga munthu wamisala amene

akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,

19ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake,

amene amati, “Ndimangoseka chabe!”

20Pakasowa nkhuni, moto umazima;

chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.

21Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto,

ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.

22Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma;

chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.

23Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi

ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.

24Munthu wachidani amayankhula zabwino

pamene mu mtima mwake muli chinyengo.

25Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire,

pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.

26Ngakhale amabisa chidani mochenjera,

koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.

27Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha;

ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.

28Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka,

ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Proverbios 26:1-28

1Ni la nieve es para el verano,

ni la lluvia para la cosecha,

ni los honores para el necio.

2Como el gorrión sin rumbo o la golondrina sin nido,

la maldición sin motivo jamás llega a su destino.

3El látigo es para los caballos,

el freno para los asnos,

y el garrote para la espalda del necio.

4No respondas al necio según su necedad,

o tú mismo pasarás por necio.

5Respóndele al necio como se merece,

para que no se tenga por sabio.

6Enviar un mensaje por medio de un necio

es como cortarse los pies o sufrir26:6 sufrir. Lit. beber. violencia.

7Inútil es el proverbio en la boca del necio,

como inútiles son las piernas de un tullido.

8Rendirle honores al necio es tan absurdo

como atar una piedra a la honda.

9El proverbio en la boca del necio

es como espina en la mano del borracho.

10Como arquero que hiere a todo el que pasa

es quien contrata al necio en su casa.26:10 Texto de difícil traducción.

11Como vuelve el perro a su vómito,

así el necio insiste en su necedad.

12¿Te has fijado en quien se cree muy sabio?

Más se puede esperar de un necio que de gente así.

13Dice el perezoso: «Hay una fiera en el camino.

¡Por las calles un león anda suelto!»

14Sobre sus goznes gira la puerta;

sobre la cama, el perezoso.

15El perezoso mete la mano en el plato,

pero le pesa llevarse el bocado a la boca.

16El perezoso se cree más sabio

que siete sabios que saben responder.

17Meterse en pleitos ajenos

es como agarrar a un perro por las orejas.

18Como loco que dispara

mortíferas flechas encendidas,

19es quien engaña a su amigo y explica:

«¡Tan solo estaba bromeando!»

20Sin leña se apaga el fuego;

sin chismes se acaba el pleito.

21Con el carbón se hacen brasas, con la leña se prende fuego,

y con un pendenciero se inician los pleitos.

22Los chismes son como ricos bocados:

se deslizan hasta las entrañas.

23Como baño de plata26:23 como baño de plata. Lit. como plata de escoria. sobre vasija de barro

son los labios zalameros de un corazón malvado.

24El que odia se esconde tras sus palabras,

pero en lo íntimo alberga perfidia.

25No le creas, aunque te hable con dulzura,

porque su corazón rebosa de abominaciones.26:25 porque su corazón … abominaciones. Lit. porque siete abominaciones hay en su corazón.

26Tal vez disimule con engaños su odio,

pero en la asamblea se descubrirá su maldad.

27Cava una fosa, y en ella caerás;

echa a rodar piedras, y te aplastarán.

28La lengua mentirosa odia a sus víctimas;

la boca lisonjera lleva a la ruina.